Add parallel Print Page Options

Mliri wa Imfa ya Ana Oyamba Kubadwa

11 Tsopano Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzalanga Farao pamodzi ndi Aigupto onse ndi mliri umodzi wotsiriza. Zikadzachitika izi iye adzakulolani kuti mutuluke mʼdziko lino. Ndithu pamene azidzakutulutsani adzachita ngati akukuyingitsani. Awuze anthu kuti mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense apemphe kwa mnansi wake ziwiya zasiliva ndi golide.” Tsono Yehova anachititsa Aigupto kuti akomere mtima Aisraeli. Komanso Mose anali wotchuka kwambiri mʼdziko la Igupto, pamaso pa nduna za Farao ndi anthu onse.

Tsono Mose anawuza Farao kuti, “Pakati pa usiku, Yehova adzayenda pakati pa anthu a ku Igupto. Ndipo mwana aliyense wamwamuna wachisamba adzafa, kuyambira mwana wamwamuna wa Farao amene amakhala pa mpando waufumu, mpaka mwana wamwamuna wachisamba wa mdzakazi wake amene ali naye pa mtondo, komanso ana oyamba a ziweto. Kudzakhala kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, kumene sikunachitikepo ndipo sikudzachitikanso. Koma pakati pa Aisraeli, ngakhale galu sadzawuwa munthu aliyense kapena chiweto!” Kotero mudzadziwa kuti Yehova ndiye wasiyanitsa pakati pa Igupto ndi Israeli. Nduna zanu zonse zidzabwera kwa ine, kugwada pamaso panga ndi kunena kuti, “Pita iwe ndi anthu ako onse amene akukutsatirawa! Zimenezi zikadzachitika ine ndidzachoka.” Ndipo Mose anachoka kwa Farao atakwiya kwambiri.

Yehova ananena kwa Mose kuti, “Farao adzakana kukumvera, kuti zodabwitsa zanga zichuluke mʼdziko la Igupto.” 10 Mose ndi Aaroni anachita zodabwitsa zonsezi pamaso pa Farao koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli atuluke mʼdziko lake.

The Plague on the Firstborn

11 Now the Lord had said to Moses, “I will bring one more plague on Pharaoh and on Egypt. After that, he will let you go(A) from here, and when he does, he will drive you out completely.(B) Tell the people that men and women alike are to ask their neighbors for articles of silver and gold.”(C) (The Lord made the Egyptians favorably disposed(D) toward the people, and Moses himself was highly regarded(E) in Egypt by Pharaoh’s officials and by the people.)

So Moses said, “This is what the Lord says: ‘About midnight(F) I will go throughout Egypt.(G) Every firstborn(H) son in Egypt will die, from the firstborn son of Pharaoh, who sits on the throne, to the firstborn son of the female slave, who is at her hand mill,(I) and all the firstborn of the cattle as well. There will be loud wailing(J) throughout Egypt—worse than there has ever been or ever will be again. But among the Israelites not a dog will bark at any person or animal.’ Then you will know that the Lord makes a distinction(K) between Egypt and Israel. All these officials of yours will come to me, bowing down before me and saying, ‘Go,(L) you and all the people who follow you!’ After that I will leave.”(M) Then Moses, hot with anger, left Pharaoh.

The Lord had said to Moses, “Pharaoh will refuse to listen(N) to you—so that my wonders(O) may be multiplied in Egypt.” 10 Moses and Aaron performed all these wonders before Pharaoh, but the Lord hardened Pharaoh’s heart,(P) and he would not let the Israelites go out of his country.