Add parallel Print Page Options

Madzi Otuluka Mʼthanthwe

17 Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku chipululu cha Sini, ndi kumayenda malo ndi malo monga momwe anawalamulira Yehova. Iwo anamanga misasa yawo ku Refidimu koma kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa. Kotero iwo anakangana ndi Mose nati, “Tipatse madzi akumwa.”

Mose anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukukangana ndi ine? Chifukwa chiyani mukumuyesa Yehova?”

Koma anthu anali ndi ludzu pamenepo ndipo anangʼungʼudza pamaso pa Mose namufunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto kuti ife, ana athu pamodzi ndi ziweto zathu tife ndi ludzu?”

Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, “Kodi ndichite chiyani ndi anthu awa? Iwo atsala pangʼono kundigenda ndi miyala.”

Yehova anati kwa Mose, “Pita patsogolo pa anthuwo. Tenga ndodo imene unamenyera nyanja ya Nailo pamodzi ndi akuluakulu ena a Israeli ndi kunyamuka. Ine ndidzayima patsogolo pako pafupi ndi thanthwe la ku Horebu. Ukamenye thanthwelo, madzi adzatuluka kuti anthu amwe.” Motero Mose anachita zimenezi pamaso pa akuluakulu a Israeli. Ndipo iye anatcha malowo Masa ndi Meriba chifukwa Aisraeli anakangana ndi kuyesa Yehova ponena kuti, “Kodi pakati pathu pali Yehova kapena palibe?”

Aisraeli Agonjetsa Aamaleki

Amaleki anabwera ku Refidimu kudzamenyana ndi Aisraeli. Mose anati kwa Yoswa, “Sankha amuna amphamvu ndipo upite ukamenyane ndi Amaleki. Mawa ndidzayima pamwamba pa phiri nditagwira ndodo ya Mulungu.”

10 Ndipo Yoswa anachitadi monga Mose anamulamulira. Iye anapita kukamenyana ndi Aamaleki ndipo Mose, Aaroni ndi Huri anapita pamwamba pa phiri. 11 Mose ankati akakweza manja ake, Aisraeli amapambana, koma akatsitsa manja akewo Amaleki amapambana. 12 Manja a Mose atatopa, Aaroni ndi Huri anatenga mwala ndi kuyika pansi ndipo Mose anakhalapo. Aaroni ndi Huri anagwirizitsa manja a Mose wina mbali ina winanso mbali ina. Choncho manja a Mose analimba mpaka kulowa kwa dzuwa. 13 Kotero Yoswa anagonjetsa asilikali ankhondo a Amaleki ndi lupanga.

14 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Lemba izi mʼbuku kuti zidzakumbukirike ndipo uwonetsetse kuti Yoswa amve zimenezi, chifukwa Ine ndidzafafaniziratu Amaleki pa dziko lapansi, kotero kuti palibe amene adzawakumbukire.”

15 Mose anamanga guwa lansembe ndipo analitcha Yehova Chipambano Changa (Yehova Nisi). 16 Ndipo anati, “Kwezani mbendera ya Yehova. Yehova adzachitabe nkhondo ndi mibado yonse ya Aamaleki.”

Water From the Rock

17 The whole Israelite community set out from the Desert of Sin,(A) traveling from place to place as the Lord commanded. They camped at Rephidim,(B) but there was no water(C) for the people to drink. So they quarreled with Moses and said, “Give us water(D) to drink.”(E)

Moses replied, “Why do you quarrel with me? Why do you put the Lord to the test?”(F)

But the people were thirsty(G) for water there, and they grumbled(H) against Moses. They said, “Why did you bring us up out of Egypt to make us and our children and livestock die(I) of thirst?”

Then Moses cried out to the Lord, “What am I to do with these people? They are almost ready to stone(J) me.”

The Lord answered Moses, “Go out in front of the people. Take with you some of the elders of Israel and take in your hand the staff(K) with which you struck the Nile,(L) and go. I will stand there before you by the rock at Horeb.(M) Strike(N) the rock, and water(O) will come out of it for the people to drink.” So Moses did this in the sight of the elders of Israel. And he called the place Massah[a](P) and Meribah[b](Q) because the Israelites quarreled and because they tested the Lord saying, “Is the Lord among us or not?”

The Amalekites Defeated

The Amalekites(R) came and attacked the Israelites at Rephidim.(S) Moses said to Joshua,(T) “Choose some of our men and go out to fight the Amalekites. Tomorrow I will stand on top of the hill with the staff(U) of God in my hands.”

10 So Joshua fought the Amalekites as Moses had ordered, and Moses, Aaron and Hur(V) went to the top of the hill. 11 As long as Moses held up his hands, the Israelites were winning,(W) but whenever he lowered his hands, the Amalekites were winning. 12 When Moses’ hands grew tired, they took a stone and put it under him and he sat on it. Aaron and Hur held his hands up—one on one side, one on the other—so that his hands remained steady till sunset.(X) 13 So Joshua overcame the Amalekite(Y) army with the sword.

14 Then the Lord said to Moses, “Write(Z) this on a scroll as something to be remembered and make sure that Joshua hears it, because I will completely blot out(AA) the name of Amalek(AB) from under heaven.”

15 Moses built an altar(AC) and called(AD) it The Lord is my Banner. 16 He said, “Because hands were lifted up against[c] the throne of the Lord,[d] the Lord will be at war against the Amalekites(AE) from generation to generation.”(AF)

Footnotes

  1. Exodus 17:7 Massah means testing.
  2. Exodus 17:7 Meribah means quarreling.
  3. Exodus 17:16 Or to
  4. Exodus 17:16 The meaning of the Hebrew for this clause is uncertain.