Add parallel Print Page Options

Kubadwa kwa Mose

Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo. Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu. Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo. Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.

Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge. Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”

Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”

Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo. Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera. 10 Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”

Mose Athawira ku Midiyani

11 Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake. 12 Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga. 13 Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”

14 Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”

15 Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime. 16 Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo. 17 Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.

18 Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”

19 Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”

20 Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”

21 Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake. 22 Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”

23 Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu. 24 Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo. 25 Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.

The Birth of Moses

Now a man of the tribe of Levi(A) married a Levite woman,(B) and she became pregnant and gave birth to a son. When she saw that he was a fine(C) child, she hid him for three months.(D) But when she could hide him no longer, she got a papyrus(E) basket[a] for him and coated it with tar and pitch.(F) Then she placed the child in it and put it among the reeds(G) along the bank of the Nile. His sister(H) stood at a distance to see what would happen to him.

Then Pharaoh’s daughter went down to the Nile to bathe, and her attendants were walking along the riverbank.(I) She saw the basket among the reeds and sent her female slave to get it. She opened it and saw the baby. He was crying, and she felt sorry for him. “This is one of the Hebrew babies,” she said.

Then his sister asked Pharaoh’s daughter, “Shall I go and get one of the Hebrew women to nurse the baby for you?”

“Yes, go,” she answered. So the girl went and got the baby’s mother. Pharaoh’s daughter said to her, “Take this baby and nurse him for me, and I will pay you.” So the woman took the baby and nursed him. 10 When the child grew older, she took him to Pharaoh’s daughter and he became her son. She named(J) him Moses,[b] saying, “I drew(K) him out of the water.”

Moses Flees to Midian

11 One day, after Moses had grown up, he went out to where his own people(L) were and watched them at their hard labor.(M) He saw an Egyptian beating a Hebrew, one of his own people. 12 Looking this way and that and seeing no one, he killed the Egyptian and hid him in the sand. 13 The next day he went out and saw two Hebrews fighting. He asked the one in the wrong, “Why are you hitting your fellow Hebrew?”(N)

14 The man said, “Who made you ruler and judge over us?(O) Are you thinking of killing me as you killed the Egyptian?” Then Moses was afraid and thought, “What I did must have become known.”

15 When Pharaoh heard of this, he tried to kill(P) Moses, but Moses fled(Q) from Pharaoh and went to live in Midian,(R) where he sat down by a well. 16 Now a priest of Midian(S) had seven daughters, and they came to draw water(T) and fill the troughs(U) to water their father’s flock. 17 Some shepherds came along and drove them away, but Moses got up and came to their rescue(V) and watered their flock.(W)

18 When the girls returned to Reuel(X) their father, he asked them, “Why have you returned so early today?”

19 They answered, “An Egyptian rescued us from the shepherds. He even drew water for us and watered the flock.”

20 “And where is he?” Reuel asked his daughters. “Why did you leave him? Invite him to have something to eat.”(Y)

21 Moses agreed to stay with the man, who gave his daughter Zipporah(Z) to Moses in marriage. 22 Zipporah gave birth to a son, and Moses named him Gershom,[c](AA) saying, “I have become a foreigner(AB) in a foreign land.”

23 During that long period,(AC) the king of Egypt died.(AD) The Israelites groaned in their slavery(AE) and cried out, and their cry(AF) for help because of their slavery went up to God. 24 God heard their groaning and he remembered(AG) his covenant(AH) with Abraham, with Isaac and with Jacob. 25 So God looked on the Israelites and was concerned(AI) about them.

Footnotes

  1. Exodus 2:3 The Hebrew can also mean ark, as in Gen. 6:14.
  2. Exodus 2:10 Moses sounds like the Hebrew for draw out.
  3. Exodus 2:22 Gershom sounds like the Hebrew for a foreigner there.