Add parallel Print Page Options

Zopereka Zomangira Chihema

25 Yehova ananena kwa Mose kuti, “Uza Aisraeli kuti abweretse chopereka kwa Ine. Iwe ulandire choperekacho mʼmalo mwanga kuchokera kwa munthu amene akupereka mwakufuna kwake. Zopereka zimene ulandire kwa anthuwo ndi izi: Golide, siliva ndi mkuwa. Nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa, ubweya wambuzi; zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha; mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira; miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.

“Iwo andipangire malo wopatulika, ndipo Ine ndidzakhala pakati pawo. Umange chihema ndiponso ziwiya zamʼkatimo monga momwe Ine ndidzakuonetsere.

Bokosi la Chipangano

10 “Tsono apange bokosi lamatabwa amtengo wa mkesha, ndipo kutalika kwake kukhale masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69. 11 Bokosilo ulikute ndi golide wabwino kwambiri, mʼkati mwake ndi kunja komwe, ndipo upange mkombero wagolide kuzungulira bokosilo. 12 Upange mphete zinayi zagolide ndipo uzimangirire ku miyendo yake inayi ya bokosilo, mbali ina ziwiri ndi mbali inanso ziwiri. 13 Kenaka upange mizati yamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide. 14 Ndipo ulowetse nsichizo mʼmphete zija za mbali zonse ziwiri za bokosilo kuti azinyamulira. 15 Nsichizo zizikhala mʼmphete za bokosilo nthawi zonse, zisamachotsedwe. 16 Ndipo udzayike mʼbokosilo miyala iwiri yolembedwapo malamulo imene Ine ndidzakupatse.

17 “Upange chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69. 18 Ndipo upange Akerubi awiri agolide osula ndi nyundo, uwayike mbali ziwiri za chivundikirocho, 19 kerubi mmodzi mbali ina ndi wina mbali inayo. Akerubiwa uwapangire limodzi ndi chivundikirocho mʼmapeto mwa mbali ziwirizo. 20 Mapiko a Akerubiwo adzatambasukire pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo kuti achiphimbe. Akerubiwo adzakhale choyangʼanana, aliyense kuyangʼana chivundikirocho. 21 Uyike chivundikirocho pamwamba pa bokosi ndipo mʼbokosilo uyikemo miyala ya malamulo, imene ndidzakupatse. 22 Ndizidzakumana nawe pamenepo, pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo, pakati pa Akerubi awiriwo, ndikumadzakupatsa malamulo onse okhudzana ndi Aisraeli.

Tebulo la Buledi Woperekedwa kwa Mulungu

23 “Upange tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69. 24 Tebulolo ulikute ndi golide wabwino kwambiri ndipo upange mkombero wagolide mʼmbali mwake. 25 Upange feremu yozungulira tebulo, mulifupi mwake ngati chikhatho cha dzanja, ndipo uyike mkombero wagolide kuzungulira feremuyo. 26 Upange mphete zinayi zagolide, ndipo uzilumikize ku ngodya zake zinayi, kumene kuli miyendo yake inayi. 27 Mphetezo uziyike kufupi ndi feremu kuti azikolowekamo nsichi zonyamulira tebuloyo. 28 Upange nsichi zamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide kuti azinyamulira tebulolo. 29 Upange mbale ndi zipande zagolide wabwino, pamodzinso ndi mitsuko ndi mabeseni zogwiritsa ntchito popereka nsembe. 30 Pa tebulopo uyikepo buledi woperekedwa kosalekeza, kuti azikhala pamaso panga nthawi zonse.

Choyikapo Nyale

31 “Upange choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri. Tsinde lake ndi mphanda zake zikhale zosulidwa ndi nyundo. Zikho zake zokhala ndi mphukira ndi maluwa ake zipangidwire kumodzi. 32 Mʼmbali mwake mukhale mphanda zisanu ndi imodzi, zitatu mbali iliyonse. 33 Zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa zikhale pa mphanda yoyamba. Pa mphanda yachiwiri pakhalenso zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa. Ndipo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zikhale chimodzimodzi ndipo zituluke mʼchoyikapo nyalecho. 34 Pa choyikapo nyalecho pakhale zikho zinayi zopangidwa ngati maluwa amtowo ali ndi mphukira ndi maluwa. 35 Mphukira yoyamba ikhale mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zoyamba za pa choyikapo nyale. Mphukira yachiwiri ikhale mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zinazo. Ndipo mphukira yachitatu ikhale mʼmunsi mwa nthambi zina ziwirinso. Zonse pamodzi zikhale nthambi zisanu ndi imodzi 36 Mphukira ndi nthambi zonse zisulidwe kumodzi ndi choyikapo nyalecho ndi golide wabwino kwambiri.

37 “Ndipo upange nyale zisanu ndi ziwiri ndi kuziyika pa choyikapo nyalecho kuti ziwunikire kutsogolo. 38 Mbaniro ndi zowolera phulusa zikhale zagolide wabwino kwambiri. 39 Choyikapo nyale ndi zipangizo zonse zipangidwe ndi golide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34. 40 Uwonetsetse kuti wapanga zonse monga momwe ndikukuonetsera pa phiri pano.”

Offerings for the Tabernacle(A)

25 The Lord said to Moses, “Tell the Israelites to bring me an offering. You are to receive the offering for me from everyone whose heart prompts(B) them to give. These are the offerings you are to receive from them: gold, silver and bronze; blue, purple and scarlet yarn(C) and fine linen; goat hair; ram skins dyed red and another type of durable leather[a];(D) acacia wood;(E) olive oil(F) for the light; spices for the anointing oil and for the fragrant incense;(G) and onyx stones and other gems to be mounted on the ephod(H) and breastpiece.(I)

“Then have them make a sanctuary(J) for me, and I will dwell(K) among them. Make this tabernacle and all its furnishings exactly like the pattern(L) I will show you.

The Ark(M)

10 “Have them make an ark[b](N) of acacia wood—two and a half cubits long, a cubit and a half wide, and a cubit and a half high.[c] 11 Overlay(O) it with pure gold, both inside and out, and make a gold molding around it. 12 Cast four gold rings for it and fasten them to its four feet, with two rings(P) on one side and two rings on the other. 13 Then make poles of acacia wood and overlay them with gold.(Q) 14 Insert the poles(R) into the rings on the sides of the ark to carry it. 15 The poles are to remain in the rings of this ark; they are not to be removed.(S) 16 Then put in the ark the tablets of the covenant law,(T) which I will give you.

17 “Make an atonement cover(U) of pure gold—two and a half cubits long and a cubit and a half wide. 18 And make two cherubim(V) out of hammered gold at the ends of the cover. 19 Make one cherub on one end and the second cherub on the other; make the cherubim of one piece with the cover, at the two ends. 20 The cherubim(W) are to have their wings spread upward, overshadowing(X) the cover with them. The cherubim are to face each other, looking toward the cover. 21 Place the cover on top of the ark(Y) and put in the ark the tablets of the covenant law(Z) that I will give you. 22 There, above the cover between the two cherubim(AA) that are over the ark of the covenant law, I will meet(AB) with you and give you all my commands for the Israelites.(AC)

The Table(AD)

23 “Make a table(AE) of acacia wood—two cubits long, a cubit wide and a cubit and a half high.[d] 24 Overlay it with pure gold and make a gold molding around it. 25 Also make around it a rim a handbreadth[e] wide and put a gold molding on the rim. 26 Make four gold rings for the table and fasten them to the four corners, where the four legs are. 27 The rings are to be close to the rim to hold the poles used in carrying the table. 28 Make the poles of acacia wood, overlay them with gold(AF) and carry the table with them. 29 And make its plates and dishes of pure gold, as well as its pitchers and bowls for the pouring out of offerings.(AG) 30 Put the bread of the Presence(AH) on this table to be before me at all times.

The Lampstand(AI)

31 “Make a lampstand(AJ) of pure gold. Hammer out its base and shaft, and make its flowerlike cups, buds and blossoms of one piece with them. 32 Six branches are to extend from the sides of the lampstand—three on one side and three on the other. 33 Three cups shaped like almond flowers with buds and blossoms are to be on one branch, three on the next branch, and the same for all six branches extending from the lampstand. 34 And on the lampstand there are to be four cups shaped like almond flowers with buds and blossoms. 35 One bud shall be under the first pair of branches extending from the lampstand, a second bud under the second pair, and a third bud under the third pair—six branches in all. 36 The buds and branches shall all be of one piece with the lampstand, hammered out of pure gold.(AK)

37 “Then make its seven lamps(AL) and set them up on it so that they light the space in front of it. 38 Its wick trimmers and trays(AM) are to be of pure gold. 39 A talent[f] of pure gold is to be used for the lampstand and all these accessories. 40 See that you make them according to the pattern(AN) shown you on the mountain.

Footnotes

  1. Exodus 25:5 Possibly the hides of large aquatic mammals
  2. Exodus 25:10 That is, a chest
  3. Exodus 25:10 That is, about 3 3/4 feet long and 2 1/4 feet wide and high or about 1.1 meters long and 68 centimeters wide and high; similarly in verse 17
  4. Exodus 25:23 That is, about 3 feet long, 1 1/2 feet wide and 2 1/4 feet high or about 90 centimeters long, 45 centimeters wide and 68 centimeters high
  5. Exodus 25:25 That is, about 3 inches or about 7.5 centimeters
  6. Exodus 25:39 That is, about 75 pounds or about 34 kilograms