Add parallel Print Page Options

33 Ndipo Yehova anati, “Chokani pa malo ano, iwe ndi anthu amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto. Pitani ku dziko limene ine ndinalonjeza ndi lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo kuti, ‘Ine ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’ Ndipo ndidzatumiza mngelo patsogolo panu kuthamangitsa Akanaani, Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi. Pitani ku dziko loyenda mkaka ndi uchi. Koma ine sindidzapita nanu, chifukwa anthu inu ndinu nkhutukumve ndipo nditha kukuwonongani mʼnjiramo.”

Anthu atamva mawu owopsawa, anayamba kulira ndipo palibe anavala zodzikometsera. Pakuti Yehova anali atanena kwa Mose kuti, “Awuze Aisraeli kuti, ‘Inu ndinu nkhutukumve.’ Ngati ine ndipita ndi inu kwa kanthawi, nditha kukuwonongani. Tsopano vulani zodzikometsera zanu ndipo ine ndidzaganiza choti ndichite nanu.” Kotero Aisraeli anavula zodzikometsera zawo pa phiri la Horebu.

Tenti ya Msonkhano

Tsono Mose ankatenga tenti ndi kukayimanga kunja kwa msasa chapatalipo, ndipo ankayitcha “tenti ya msonkhano.” Aliyense wofuna kukafunsa kanthu kwa Yehova amapita ku tenti ya msonkhano kunja kwa msasa. Ndipo nthawi ina iliyonse imene Mose amapita ku tenti anthu onse amanyamuka ndi kuyimirira pa makomo amatenti awo, kumuyangʼana Mose mpaka atalowa mu tentimo. Mose akamalowa mu tenti, chipilala cha mtambo chimatsika ndi kukhala pa khomo pamene Yehova amayankhula ndi Mose. 10 Nthawi zonse anthu akaona chipilala cha mtambo chitayima pa khomo la tentiyo amayimirira ndi kupembedza, aliyense ali pa khomo la tenti yake. 11 Yehova amayankhula ndi Mose maso ndi maso ngati mmene munthu amayankhulira ndi bwenzi lake. Kenaka Mose amabwerera ku msasa koma womuthandiza wake, Yoswa, mwana wa Nuni samachoka pa tentiyo.

Mose ndi Ulemerero wa Yehova

12 Mose anati kwa Yehova, “Inu mwakhala mukundiwuza kuti, ‘Tsogolera anthu awa,’ koma simunandiwuze amene mudzamutuma kuti apite pamodzi nane. Inu mwanena kuti, ‘Ndikukudziwa bwino kwambiri ndipo wapeza chisomo pamaso panga.’ 13 Ngati mwakondwera nane ndiphunzitseni njira zanu kuti ndikudziweni ndi kupitiriza kupeza chisomo pamaso panu. Kumbukirani kuti mtundu uwu ndi anthu anu.”

14 Yehova anayankha kuti, “Ine ndemwe ndidzapita pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakupatsa mpumulo.”

15 Kenaka Mose anati kwa Yehova, “Ngati inu simupita nafe, musatitumize kuti tipite, kutichotsa pano. 16 Kodi wina adzadziwa bwanji kuti inu mwandikomera mtima pamodzi ndi anthu awa ngati simupita nafe? Kodi nʼchiyani chomwe chidzatisiyanitse pakati pa anthu onse amene ali pa dziko lapansi?”

17 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzachita zimene iwe wandipempha chifukwa Ine ndikukondwera nawe, ndikukudziwa bwino lomwe.”

18 Kenaka Mose anati, “Tsopano ndionetseni ulemerero wanu.”

19 Ndipo Yehova anati, “Ine ndidzakuonetsa ulemerero wanga wonse ndipo ndidzatchula dzina langa lakuti Yehova pamaso pako. Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.” 20 Iye anati, “Koma iwe sungaone nkhope yanga, pakuti palibe munthu amene amaona Ine nakhala ndi moyo.”

21 Ndipo Yehova anati, “Pali malo pafupi ndi ine pomwe ungathe kuyima pa thanthwe. 22 Pamene ulemerero wanga udutsa, ndidzakuyika mʼphanga la thanthwe ndi kukuphimba ndi dzanja langa mpaka nditadutsa. 23 Kenaka ine ndidzachotsa dzanja langa ndipo iwe udzaona msana wanga, koma nkhope yanga sidzaoneka.”

33 Then the Lord said to Moses, “Leave this place, you and the people you brought up out of Egypt, and go up to the land I promised on oath(A) to Abraham, Isaac and Jacob, saying, ‘I will give it to your descendants.’(B) I will send an angel(C) before you and drive out the Canaanites, Amorites, Hittites, Perizzites, Hivites and Jebusites.(D) Go up to the land flowing with milk and honey.(E) But I will not go with you, because you are a stiff-necked(F) people and I might destroy(G) you on the way.”

When the people heard these distressing words, they began to mourn(H) and no one put on any ornaments. For the Lord had said to Moses, “Tell the Israelites, ‘You are a stiff-necked people.(I) If I were to go with you even for a moment, I might destroy(J) you. Now take off your ornaments and I will decide what to do with you.’” So the Israelites stripped off their ornaments at Mount Horeb.(K)

The Tent of Meeting

Now Moses used to take a tent and pitch it outside the camp some distance away, calling it the “tent of meeting.”(L) Anyone inquiring(M) of the Lord would go to the tent of meeting outside the camp. And whenever Moses went out to the tent, all the people rose and stood at the entrances to their tents,(N) watching Moses until he entered the tent. As Moses went into the tent, the pillar of cloud(O) would come down and stay at the entrance, while the Lord spoke(P) with Moses. 10 Whenever the people saw the pillar of cloud standing at the entrance to the tent, they all stood and worshiped, each at the entrance to their tent.(Q) 11 The Lord would speak to Moses face to face,(R) as one speaks to a friend. Then Moses would return to the camp, but his young aide Joshua(S) son of Nun did not leave the tent.

Moses and the Glory of the Lord

12 Moses said to the Lord, “You have been telling me, ‘Lead these people,’(T) but you have not let me know whom you will send with me. You have said, ‘I know you by name(U) and you have found favor(V) with me.’ 13 If you are pleased with me, teach me your ways(W) so I may know you and continue to find favor with you. Remember that this nation is your people.”(X)

14 The Lord replied, “My Presence(Y) will go with you, and I will give you rest.”(Z)

15 Then Moses said to him, “If your Presence(AA) does not go with us, do not send us up from here. 16 How will anyone know that you are pleased with me and with your people unless you go with us?(AB) What else will distinguish me and your people from all the other people on the face of the earth?”(AC)

17 And the Lord said to Moses, “I will do the very thing you have asked,(AD) because I am pleased with you and I know you by name.”(AE)

18 Then Moses said, “Now show me your glory.”(AF)

19 And the Lord said, “I will cause all my goodness to pass(AG) in front of you, and I will proclaim my name,(AH) the Lord, in your presence. I will have mercy on whom I will have mercy, and I will have compassion on whom I will have compassion.(AI) 20 But,” he said, “you cannot see my face, for no one may see(AJ) me and live.”

21 Then the Lord said, “There is a place near me where you may stand on a rock. 22 When my glory passes by, I will put you in a cleft in the rock(AK) and cover you with my hand(AL) until I have passed by. 23 Then I will remove my hand and you will see my back; but my face must not be seen.”