Add parallel Print Page Options

Guwa Lansembe Yopsereza

38 Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229. Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa. Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto. Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo. Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira. Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa. Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.

Beseni Losambira

Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.

Bwalo la Chihema

Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino. 10 Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo. 11 Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.

12 Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo. 13 Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23. 14 Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu, 15 polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu. 16 Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino. 17 Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.

18 Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229, 19 pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva. 20 Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.

Zipangizo Zachitsulo za ku Malo Opatulika

21 Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi: 22 Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose, 23 pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala. 24 Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.

25 Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika. 26 Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550. 27 Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi. 28 Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.

29 Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425. 30 Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse, 31 matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.

The Altar of Burnt Offering(A)

38 They[a] built the altar of burnt offering of acacia wood, three cubits[b] high; it was square, five cubits long and five cubits wide.[c] They made a horn at each of the four corners, so that the horns and the altar were of one piece, and they overlaid the altar with bronze.(B) They made all its utensils(C) of bronze—its pots, shovels, sprinkling bowls, meat forks and firepans. They made a grating for the altar, a bronze network, to be under its ledge, halfway up the altar. They cast bronze rings to hold the poles for the four corners of the bronze grating. They made the poles of acacia wood and overlaid them with bronze. They inserted the poles into the rings so they would be on the sides of the altar for carrying it. They made it hollow, out of boards.

The Basin for Washing

They made the bronze basin(D) and its bronze stand from the mirrors of the women(E) who served at the entrance to the tent of meeting.

The Courtyard(F)

Next they made the courtyard. The south side was a hundred cubits[d] long and had curtains of finely twisted linen, 10 with twenty posts and twenty bronze bases, and with silver hooks and bands on the posts. 11 The north side was also a hundred cubits long and had twenty posts and twenty bronze bases, with silver hooks and bands on the posts.

12 The west end was fifty cubits[e] wide and had curtains, with ten posts and ten bases, with silver hooks and bands on the posts. 13 The east end, toward the sunrise, was also fifty cubits wide. 14 Curtains fifteen cubits[f] long were on one side of the entrance, with three posts and three bases, 15 and curtains fifteen cubits long were on the other side of the entrance to the courtyard, with three posts and three bases. 16 All the curtains around the courtyard were of finely twisted linen. 17 The bases for the posts were bronze. The hooks and bands on the posts were silver, and their tops were overlaid with silver; so all the posts of the courtyard had silver bands.

18 The curtain for the entrance to the courtyard was made of blue, purple and scarlet yarn and finely twisted linen—the work of an embroiderer. It was twenty cubits[g] long and, like the curtains of the courtyard, five cubits[h] high, 19 with four posts and four bronze bases. Their hooks and bands were silver, and their tops were overlaid with silver. 20 All the tent pegs(G) of the tabernacle and of the surrounding courtyard were bronze.

The Materials Used

21 These are the amounts of the materials used for the tabernacle, the tabernacle of the covenant law,(H) which were recorded at Moses’ command by the Levites under the direction of Ithamar(I) son of Aaron, the priest. 22 (Bezalel(J) son of Uri, the son of Hur, of the tribe of Judah, made everything the Lord commanded Moses; 23 with him was Oholiab(K) son of Ahisamak, of the tribe of Dan—an engraver and designer, and an embroiderer in blue, purple and scarlet yarn and fine linen.) 24 The total amount of the gold from the wave offering used for all the work on the sanctuary(L) was 29 talents and 730 shekels,[i] according to the sanctuary shekel.(M)

25 The silver obtained from those of the community who were counted in the census(N) was 100 talents[j] and 1,775 shekels,[k] according to the sanctuary shekel— 26 one beka per person,(O) that is, half a shekel,[l] according to the sanctuary shekel,(P) from everyone who had crossed over to those counted, twenty years old or more,(Q) a total of 603,550 men.(R) 27 The 100 talents of silver were used to cast the bases(S) for the sanctuary and for the curtain—100 bases from the 100 talents, one talent for each base. 28 They used the 1,775 shekels to make the hooks for the posts, to overlay the tops of the posts, and to make their bands.

29 The bronze from the wave offering was 70 talents and 2,400 shekels.[m] 30 They used it to make the bases for the entrance to the tent of meeting, the bronze altar with its bronze grating and all its utensils, 31 the bases for the surrounding courtyard and those for its entrance and all the tent pegs for the tabernacle and those for the surrounding courtyard.

Footnotes

  1. Exodus 38:1 Or He; also in verses 2-9
  2. Exodus 38:1 That is, about 4 1/2 feet or about 1.4 meters
  3. Exodus 38:1 That is, about 7 1/2 feet or about 2.3 meters long and wide
  4. Exodus 38:9 That is, about 150 feet or about 45 meters
  5. Exodus 38:12 That is, about 75 feet or about 23 meters
  6. Exodus 38:14 That is, about 22 feet or about 6.8 meters
  7. Exodus 38:18 That is, about 30 feet or about 9 meters
  8. Exodus 38:18 That is, about 7 1/2 feet or about 2.3 meters
  9. Exodus 38:24 The weight of the gold was a little over a ton or about 1 metric ton.
  10. Exodus 38:25 That is, about 3 3/4 tons or about 3.4 metric tons; also in verse 27
  11. Exodus 38:25 That is, about 44 pounds or about 20 kilograms; also in verse 28
  12. Exodus 38:26 That is, about 1/5 ounce or about 5.7 grams
  13. Exodus 38:29 The weight of the bronze was about 2 1/2 tons or about 2.4 metric tons.