Add parallel Print Page Options

Chiweruzo pa Atsogoleri a Israeli

11 Pamenepo Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kubwera nane ku chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Kumeneko pa khomo la chipata panali anthu 25, ndipo ndinaona pakati pawo atsogoleri awa: Yaazaniya mwana wa Azuri ndi Pelatiya mwana wa Benaya. Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi anthu amene akukonza zoyipa ndi kupereka malangizo oyipa mu mzindamo. Iwo amawuza anthu kuti, ‘Nthawi sinafike yoti timange Nyumba? Mzindawu uli ngati mʼphika umene uli pa moto ndipo ife tili ngati nyama mu mʼphikamo. Choncho iwe mwana wa munthu, unenere mowadzudzula. Nenera ndithu.’ ”

Ndipo Mzimu wa Yehova unandigwera ndipo unandiwuza kuti, “Unene kuti zimene akunena Yehova ndi izi. Iye akuti. ‘Izi ndi zimene mukunena, Inu Aisraeli, koma Ine ndikudziwa zimene zili mu mtima mwanu.’ Mwapha anthu ambiri mu mzinda muno ndipo mwadzaza misewu yake ndi mitembo.

“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mitembo imene mwayiponya mʼmisewuyo ndiyo nyama ndipo mzinda uno ndiwo mʼphika, koma Ine ndidzakuthamangitsanimo. Inu mumaopa lupanga, koma lupangalo ndi limene ndidzakubweretsereni, akutero Ambuye. Ine ndidzakuthamangitsani mu mzinda ndipo ndidzakuperekani mʼdzanja la alendo kuti akulangeni. 10 Mudzaphedwa ndi lupanga ndipo ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 11 Mzinda uno sudzakhala ngati mʼphika wokutetezani ndipo simudzakhalanso ngati nyama ya mʼmenemo. Ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli. 12 Ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. Inu simunatsatire malangizo anga kapena kusunga malamulo anga koma mwakhala mukutsata zochita za mitundu ina ya anthu imene yakuzungulirani.’ ”

13 Tsono pamene ndinkanenera, Pelatiya mwana wa Benaya anafa. Pomwepo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba ndipo ndinafuwula ndi mawu aakulu kuti “Mayo, Ambuye Yehova! Kodi mudzawatheratu Aisraeli onse otsala?”

14 Yehova anayankhula nane kuti, 15 “Anthu okhala ku Yerusalemu akuwanena abale ako, anthu a ku ukapolo, onse a banja la Israeli, kuti, ‘Anthu onse amene anatengedwa ukapolo ali kutali ndi Yehova. Dziko lanu Yehova anatipatsa kuti likhale lathulathu.’ ”

Mulungu Alonjeza za Kubwerera kwa Israeli

16 “Nʼchifukwa chake nena kwa anzako a ku ukapolo kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Ine ndinawatumiza kutali pakati pa anthu a mitundu ina. Ndinawabalalitsa ku mayiko ambiri. Komabe ndakhala ndikuwasunga ku mayiko kumene anapitako!’

17 “Nʼchifukwa chake uwawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kuti, Ndidzawasonkhanitsa kuchokera kwa anthu a mitundu inayo ndi kuwasonkhanitsira pamodzi kuchokera ku mayiko kumene ndinawabalalitsirako. Pambuyo pake ndidzawapatsa dziko la Israeli.

18 “Akadzalowa mʼdzikomo adzachotsa mafano awo onse oyipa ndi onyansa. 19 Ndidzawapatsa mtima watsopano ndipo ndidzayika mzimu watsopano mwa iwo. Ndidzachotsa mtima wowuma ngati mwala mwa iwo, ndipo ndidzawapatsa mtima wofewa ngati mnofu. 20 Motero adzatsata malamulo anga ndipo adzasunga mosamala malamulo anga. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo. 21 Koma kunena za amene akupembedza mafano oyipa ndi onyansa, ndidzawalanga chifukwa cha zimene achita. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

22 Tsono akerubi aja anatambasula mapiko awo kuyamba kuwuluka, mikombero ili mʼmbali mwawo. Ulemerero wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo. 23 Ulemerero wa Yehova unakwera ndi kusiya mzindawo ndipo unakayima pa phiri cha kummawa kwake kwa mzindawo. 24 Pambuyo pake Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kukandifikitsa. Zimenezi zinkachitika mʼmasomphenya monga mmene Mzimu wa Mulungu unkandionetsera.

Kenaka masomphenya amene ndinkawaonawo anayamba kuzimirira. 25 Ndipo ndinafotokozera akapolowo zonse zimene Yehova anandionetsa.

God’s Sure Judgment on Jerusalem

11 Then the Spirit lifted me up and brought me to the gate of the house of the Lord that faces east. There at the entrance of the gate were twenty-five men, and I saw among them Jaazaniah son of Azzur and Pelatiah(A) son of Benaiah, leaders(B) of the people.(C) The Lord said to me, “Son of man, these are the men who are plotting evil(D) and giving wicked advice in this city.(E) They say, ‘Haven’t our houses been recently rebuilt? This city is a pot,(F) and we are the meat in it.’(G) Therefore prophesy(H) against them; prophesy, son of man.”

Then the Spirit of the Lord came on me, and he told me to say: “This is what the Lord says: That is what you are saying, you leaders in Israel, but I know what is going through your mind.(I) You have killed many people in this city and filled its streets with the dead.(J)

“Therefore this is what the Sovereign Lord says: The bodies you have thrown there are the meat and this city is the pot,(K) but I will drive you out of it.(L) You fear the sword,(M) and the sword is what I will bring against you, declares the Sovereign Lord.(N) I will drive you out of the city and deliver you into the hands(O) of foreigners and inflict punishment on you.(P) 10 You will fall by the sword, and I will execute judgment on you at the borders of Israel.(Q) Then you will know that I am the Lord. 11 This city will not be a pot(R) for you, nor will you be the meat in it; I will execute judgment on you at the borders of Israel. 12 And you will know that I am the Lord,(S) for you have not followed my decrees(T) or kept my laws but have conformed to the standards of the nations around you.(U)

13 Now as I was prophesying, Pelatiah(V) son of Benaiah died. Then I fell facedown and cried out in a loud voice, “Alas, Sovereign Lord! Will you completely destroy the remnant of Israel?(W)

The Promise of Israel’s Return

14 The word of the Lord came to me: 15 “Son of man, the people of Jerusalem have said of your fellow exiles and all the other Israelites, ‘They are far away from the Lord; this land was given to us as our possession.’(X)

16 “Therefore say: ‘This is what the Sovereign Lord says: Although I sent them far away among the nations and scattered them among the countries, yet for a little while I have been a sanctuary(Y) for them in the countries where they have gone.’

17 “Therefore say: ‘This is what the Sovereign Lord says: I will gather you from the nations and bring you back from the countries where you have been scattered, and I will give you back the land of Israel again.’(Z)

18 “They will return to it and remove all its vile images(AA) and detestable idols.(AB) 19 I will give them an undivided heart(AC) and put a new spirit in them; I will remove from them their heart of stone(AD) and give them a heart of flesh.(AE) 20 Then they will follow my decrees and be careful to keep my laws.(AF) They will be my people,(AG) and I will be their God.(AH) 21 But as for those whose hearts are devoted to their vile images and detestable idols,(AI) I will bring down on their own heads what they have done, declares the Sovereign Lord.(AJ)

22 Then the cherubim, with the wheels beside them, spread their wings, and the glory(AK) of the God of Israel was above them.(AL) 23 The glory(AM) of the Lord went up from within the city and stopped above the mountain(AN) east of it. 24 The Spirit(AO) lifted me up and brought me to the exiles in Babylonia[a] in the vision(AP) given by the Spirit of God.

Then the vision I had seen went up from me, 25 and I told the exiles everything the Lord had shown me.(AQ)

Footnotes

  1. Ezekiel 11:24 Or Chaldea