Add parallel Print Page Options

Mawu Odzudzula Aneneri Onyenga

13 Yehova anayankhulanso nane kuti, “Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’ Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’ Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja. Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova. Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi. Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.

“Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova. Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.

10 “Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza, 11 choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho. 12 Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’

13 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu. 14 Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 15 Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza. 16 Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’

17 “Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule. 18 Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu? 19 Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.

20 “ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame. 21 Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 22 Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo, 23 choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

False Prophets Condemned

13 The word of the Lord came to me: “Son of man, prophesy against the prophets(A) of Israel who are now prophesying. Say to those who prophesy out of their own imagination:(B) ‘Hear the word of the Lord!(C) This is what the Sovereign Lord says: Woe to the foolish[a] prophets(D) who follow their own spirit and have seen nothing!(E) Your prophets, Israel, are like jackals among ruins. You have not gone up to the breaches in the wall to repair(F) it for the people of Israel so that it will stand firm in the battle on the day of the Lord.(G) Their visions are false(H) and their divinations a lie. Even though the Lord has not sent(I) them, they say, “The Lord declares,” and expect him to fulfill their words.(J) Have you not seen false visions(K) and uttered lying divinations when you say, “The Lord declares,” though I have not spoken?

“‘Therefore this is what the Sovereign Lord says: Because of your false words and lying visions, I am against you,(L) declares the Sovereign Lord. My hand will be against the prophets who see false visions and utter lying(M) divinations. They will not belong to the council of my people or be listed in the records(N) of Israel, nor will they enter the land of Israel. Then you will know that I am the Sovereign Lord.(O)

10 “‘Because they lead my people astray,(P) saying, “Peace,”(Q) when there is no peace, and because, when a flimsy wall is built, they cover it with whitewash,(R) 11 therefore tell those who cover it with whitewash that it is going to fall. Rain will come in torrents, and I will send hailstones(S) hurtling down,(T) and violent winds will burst forth.(U) 12 When the wall collapses, will people not ask you, “Where is the whitewash you covered it with?”

13 “‘Therefore this is what the Sovereign Lord says: In my wrath I will unleash a violent wind, and in my anger hailstones(V) and torrents of rain(W) will fall with destructive fury.(X) 14 I will tear down the wall(Y) you have covered with whitewash and will level it to the ground so that its foundation(Z) will be laid bare. When it[b] falls,(AA) you will be destroyed in it; and you will know that I am the Lord. 15 So I will pour out my wrath against the wall and against those who covered it with whitewash. I will say to you, “The wall is gone and so are those who whitewashed it, 16 those prophets of Israel who prophesied to Jerusalem and saw visions of peace for her when there was no peace, declares the Sovereign Lord.(AB)”’

17 “Now, son of man, set your face(AC) against the daughters(AD) of your people who prophesy out of their own imagination. Prophesy against them(AE) 18 and say, ‘This is what the Sovereign Lord says: Woe to the women who sew magic charms on all their wrists and make veils of various lengths for their heads in order to ensnare people. Will you ensnare the lives of my people but preserve your own? 19 You have profaned(AF) me among my people for a few handfuls of barley and scraps of bread.(AG) By lying to my people, who listen to lies, you have killed those who should not have died and have spared those who should not live.(AH)

20 “‘Therefore this is what the Sovereign Lord says: I am against your magic charms with which you ensnare people like birds and I will tear them from your arms; I will set free the people that you ensnare like birds.(AI) 21 I will tear off your veils and save my people from your hands, and they will no longer fall prey to your power. Then you will know that I am the Lord.(AJ) 22 Because you disheartened the righteous with your lies,(AK) when I had brought them no grief, and because you encouraged the wicked not to turn from their evil ways and so save their lives,(AL) 23 therefore you will no longer see false visions(AM) or practice divination.(AN) I will save(AO) my people from your hands. And then you will know that I am the Lord.(AP)’”

Footnotes

  1. Ezekiel 13:3 Or wicked
  2. Ezekiel 13:14 Or the city