Add parallel Print Page Options

Kusakhulupirika kwa Yerusalemu

16 Yehova anayankhula nane kuti, “Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa. Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti. Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu. Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.

“ ‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’ ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.

“ ‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.

“ ‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta. 10 Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta. 11 Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako, 12 ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako. 13 Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi. 14 Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.

15 “ ‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake. 16 Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso. 17 Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama. 18 Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo. 19 Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.

20 “ ‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire 21 kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo? 22 Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.

23 “ ‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse, 24 wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse. 25 Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo. 26 Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako. 27 Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa. 28 Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe. 29 Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.

30 “ ‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi. 31 Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.

32 “ ‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako! 33 Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe. 34 Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.

35 “ ‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova! 36 Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano, 37 nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse. 38 Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri. 39 Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa. 40 Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo. 41 Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako. 42 Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.

43 “ ‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.

44 “ ‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’ 45 Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori. 46 Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi. 47 Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo. 48 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.

49 “ ‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi. 50 Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu. 51 Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye. 52 Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.

53 “ ‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu. 54 Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa. 55 Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja. 56 Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu 57 kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza. 58 Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.

59 “ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa. 60 Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe. 61 Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe. 62 Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 63 Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Jerusalem as an Adulterous Wife

16 The word of the Lord came to me: “Son of man, confront(A) Jerusalem with her detestable practices(B) and say, ‘This is what the Sovereign Lord says to Jerusalem: Your ancestry(C) and birth were in the land of the Canaanites; your father(D) was an Amorite(E) and your mother a Hittite.(F) On the day you were born(G) your cord was not cut, nor were you washed with water to make you clean, nor were you rubbed with salt or wrapped in cloths. No one looked on you with pity or had compassion enough to do any of these things for you. Rather, you were thrown out into the open field, for on the day you were born you were despised.

“‘Then I passed by and saw you kicking about in your blood, and as you lay there in your blood I said to you, “Live!”[a](H) I made you grow(I) like a plant of the field. You grew and developed and entered puberty. Your breasts had formed and your hair had grown, yet you were stark naked.(J)

“‘Later I passed by, and when I looked at you and saw that you were old enough for love, I spread the corner of my garment(K) over you and covered your naked body. I gave you my solemn oath and entered into a covenant(L) with you, declares the Sovereign Lord, and you became mine.(M)

“‘I bathed you with water and washed(N) the blood from you and put ointments on you. 10 I clothed you with an embroidered(O) dress and put sandals of fine leather on you. I dressed you in fine linen(P) and covered you with costly garments.(Q) 11 I adorned you with jewelry:(R) I put bracelets(S) on your arms and a necklace(T) around your neck, 12 and I put a ring on your nose,(U) earrings(V) on your ears and a beautiful crown(W) on your head.(X) 13 So you were adorned with gold and silver; your clothes(Y) were of fine linen and costly fabric and embroidered cloth. Your food was honey, olive oil(Z) and the finest flour. You became very beautiful and rose to be a queen.(AA) 14 And your fame(AB) spread among the nations on account of your beauty,(AC) because the splendor I had given you made your beauty perfect, declares the Sovereign Lord.(AD)

15 “‘But you trusted in your beauty and used your fame to become a prostitute. You lavished your favors on anyone who passed by(AE) and your beauty became his.(AF) 16 You took some of your garments to make gaudy high places,(AG) where you carried on your prostitution.(AH) You went to him, and he possessed your beauty.[b] 17 You also took the fine jewelry I gave you, the jewelry made of my gold and silver, and you made for yourself male idols and engaged in prostitution with them.(AI) 18 And you took your embroidered clothes to put on them, and you offered my oil and incense(AJ) before them. 19 Also the food I provided for you—the flour, olive oil and honey I gave you to eat—you offered as fragrant incense before them. That is what happened, declares the Sovereign Lord.(AK)

20 “‘And you took your sons and daughters(AL) whom you bore to me(AM) and sacrificed them as food to the idols. Was your prostitution not enough?(AN) 21 You slaughtered my children and sacrificed them to the idols.(AO) 22 In all your detestable practices and your prostitution you did not remember the days of your youth,(AP) when you were naked and bare,(AQ) kicking about in your blood.(AR)

23 “‘Woe!(AS) Woe to you, declares the Sovereign Lord. In addition to all your other wickedness, 24 you built a mound for yourself and made a lofty shrine(AT) in every public square.(AU) 25 At every street corner(AV) you built your lofty shrines and degraded your beauty, spreading your legs with increasing promiscuity to anyone who passed by.(AW) 26 You engaged in prostitution(AX) with the Egyptians,(AY) your neighbors with large genitals, and aroused my anger(AZ) with your increasing promiscuity.(BA) 27 So I stretched out my hand(BB) against you and reduced your territory; I gave you over(BC) to the greed of your enemies, the daughters of the Philistines,(BD) who were shocked by your lewd conduct. 28 You engaged in prostitution with the Assyrians(BE) too, because you were insatiable; and even after that, you still were not satisfied.(BF) 29 Then you increased your promiscuity to include Babylonia,[c](BG) a land of merchants, but even with this you were not satisfied.(BH)

30 “‘I am filled with fury against you,[d] declares the Sovereign Lord, when you do all these things, acting like a brazen prostitute!(BI) 31 When you built your mounds at every street corner and made your lofty shrines(BJ) in every public square, you were unlike a prostitute, because you scorned payment.

32 “‘You adulterous wife! You prefer strangers to your own husband! 33 All prostitutes receive gifts,(BK) but you give gifts(BL) to all your lovers, bribing them to come to you from everywhere for your illicit favors.(BM) 34 So in your prostitution you are the opposite of others; no one runs after you for your favors. You are the very opposite, for you give payment and none is given to you.

35 “‘Therefore, you prostitute, hear the word of the Lord! 36 This is what the Sovereign Lord says: Because you poured out your lust and exposed your naked body in your promiscuity with your lovers, and because of all your detestable idols, and because you gave them your children’s blood,(BN) 37 therefore I am going to gather all your lovers, with whom you found pleasure, those you loved as well as those you hated. I will gather them against you from all around and will strip(BO) you in front of them, and they will see you stark naked.(BP) 38 I will sentence you to the punishment of women who commit adultery and who shed blood;(BQ) I will bring on you the blood vengeance of my wrath and jealous anger.(BR) 39 Then I will deliver you into the hands(BS) of your lovers, and they will tear down your mounds and destroy your lofty shrines. They will strip you of your clothes and take your fine jewelry and leave you stark naked.(BT) 40 They will bring a mob against you, who will stone(BU) you and hack you to pieces with their swords. 41 They will burn down(BV) your houses and inflict punishment on you in the sight of many women.(BW) I will put a stop(BX) to your prostitution, and you will no longer pay your lovers. 42 Then my wrath against you will subside and my jealous anger will turn away from you; I will be calm and no longer angry.(BY)

43 “‘Because you did not remember(BZ) the days of your youth but enraged me with all these things, I will surely bring down(CA) on your head what you have done, declares the Sovereign Lord. Did you not add lewdness to all your other detestable practices?(CB)

44 “‘Everyone who quotes proverbs(CC) will quote this proverb about you: “Like mother, like daughter.” 45 You are a true daughter of your mother, who despised(CD) her husband(CE) and her children; and you are a true sister of your sisters, who despised their husbands and their children. Your mother was a Hittite and your father an Amorite.(CF) 46 Your older sister(CG) was Samaria, who lived to the north of you with her daughters; and your younger sister, who lived to the south of you with her daughters, was Sodom.(CH) 47 You not only followed their ways and copied their detestable practices, but in all your ways you soon became more depraved than they.(CI) 48 As surely as I live, declares the Sovereign(CJ) Lord, your sister Sodom(CK) and her daughters never did what you and your daughters have done.(CL)

49 “‘Now this was the sin of your sister Sodom:(CM) She and her daughters were arrogant,(CN) overfed and unconcerned;(CO) they did not help the poor and needy.(CP) 50 They were haughty(CQ) and did detestable things before me. Therefore I did away with them as you have seen.(CR) 51 Samaria did not commit half the sins you did. You have done more detestable things than they, and have made your sisters seem righteous by all these things you have done.(CS) 52 Bear your disgrace, for you have furnished some justification for your sisters. Because your sins were more vile than theirs, they appear more righteous(CT) than you. So then, be ashamed and bear(CU) your disgrace, for you have made your sisters appear righteous.

53 “‘However, I will restore(CV) the fortunes of Sodom and her daughters and of Samaria and her daughters, and your fortunes along with them,(CW) 54 so that you may bear your disgrace(CX) and be ashamed of all you have done in giving them comfort. 55 And your sisters, Sodom with her daughters and Samaria with her daughters, will return to what they were before; and you and your daughters will return to what you were before.(CY) 56 You would not even mention your sister Sodom in the day of your pride, 57 before your wickedness was uncovered. Even so, you are now scorned(CZ) by the daughters of Edom[e](DA) and all her neighbors and the daughters of the Philistines—all those around you who despise you. 58 You will bear the consequences of your lewdness and your detestable practices, declares the Lord.(DB)

59 “‘This is what the Sovereign Lord says: I will deal with you as you deserve, because you have despised my oath by breaking the covenant.(DC) 60 Yet I will remember the covenant(DD) I made with you in the days of your youth,(DE) and I will establish an everlasting covenant(DF) with you. 61 Then you will remember your ways and be ashamed(DG) when you receive your sisters, both those who are older than you and those who are younger. I will give them to you as daughters,(DH) but not on the basis of my covenant with you. 62 So I will establish my covenant(DI) with you, and you will know that I am the Lord.(DJ) 63 Then, when I make atonement(DK) for you for all you have done, you will remember and be ashamed(DL) and never again open your mouth(DM) because of your humiliation, declares the Sovereign Lord.(DN)’”

Footnotes

  1. Ezekiel 16:6 A few Hebrew manuscripts, Septuagint and Syriac; most Hebrew manuscripts repeat and as you lay there in your blood I said to you, “Live!”
  2. Ezekiel 16:16 The meaning of the Hebrew for this sentence is uncertain.
  3. Ezekiel 16:29 Or Chaldea
  4. Ezekiel 16:30 Or How feverish is your heart,
  5. Ezekiel 16:57 Many Hebrew manuscripts and Syriac; most Hebrew manuscripts, Septuagint and Vulgate Aram