Ezekieli 19
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Nyimbo ya Maliro a Akalonga a Israeli
19 “Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli. 2 Uzinena kuti,
“ ‘Amayi ako anali ndani?
Anali ngati mkango waukazi!
Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna;
unkalera ana ake pakati pa misona.
3 Unalera mmodzi mwa ana ake,
ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu.
Unaphunzira kugwira nyama,
ndipo unayamba kudya anthu.
4 Anthu amitundu anamva za mkangowo,
ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo.
Iwo anawukoka ndi ngowe
kupita nawo ku dziko la Igupto.
5 “ ‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera,
amayiwo anatenganso mwana wina
namusandutsa mkango wamphamvu.
6 Unkayendayenda pakati pa mikango inzake,
pakuti tsopano unali mkango wamphamvu.
Unaphunzira kugwira nyama
ndipo unayamba kudya anthu.
7 Unagwetsa malinga awo,
ndikuwononga mizinda yawo.
Onse a mʼdzikomo
anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
8 Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira,
inabwera kudzalimbana nawo.
Anawutchera ukonde wawo,
ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
9 Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga.
Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni
ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende
ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso
ku mapiri a Israeli.
10 “ ‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa
wodzalidwa mʼmbali mwa madzi.
Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri
chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
11 Nthambi zake zinali zolimba,
zoyenera kupangira ndodo yaufumu.
Unatalika nusomphoka pakati pa
zomera zina.
Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake,
ndi nthambi zake zambiri.
12 Koma unazulidwa mwaukali
ndipo unagwetsedwa pansi.
Unawuma ndi mphepo ya kummawa,
zipatso zake zinayoyoka;
nthambi zake zolimba zinafota
ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
13 Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu,
dziko lowuma ndi lopanda madzi.
14 Moto unatulukanso mu mtengomo
ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake.
Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo
yoyenera kupangira ndodo yaufumu.
Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’ ”
Ezekiel 19
New International Version
A Lament Over Israel’s Princes
19 “Take up a lament(A) concerning the princes(B) of Israel 2 and say:
“‘What a lioness(C) was your mother
among the lions!
She lay down among them
and reared her cubs.(D)
3 She brought up one of her cubs,
and he became a strong lion.
He learned to tear the prey
and he became a man-eater.
4 The nations heard about him,
and he was trapped in their pit.
They led him with hooks(E)
to the land of Egypt.(F)
5 “‘When she saw her hope unfulfilled,
her expectation gone,
she took another of her cubs(G)
and made him a strong lion.(H)
6 He prowled among the lions,
for he was now a strong lion.
He learned to tear the prey
and he became a man-eater.(I)
7 He broke down[a] their strongholds
and devastated(J) their towns.
The land and all who were in it
were terrified by his roaring.
8 Then the nations(K) came against him,
those from regions round about.
They spread their net(L) for him,
and he was trapped in their pit.(M)
9 With hooks(N) they pulled him into a cage
and brought him to the king of Babylon.(O)
They put him in prison,
so his roar(P) was heard no longer
on the mountains of Israel.(Q)
10 “‘Your mother was like a vine in your vineyard[b](R)
planted by the water;(S)
it was fruitful and full of branches
because of abundant water.(T)
11 Its branches were strong,
fit for a ruler’s scepter.
It towered high
above the thick foliage,
conspicuous for its height
and for its many branches.(U)
12 But it was uprooted(V) in fury
and thrown to the ground.
The east wind(W) made it shrivel,
it was stripped of its fruit;
its strong branches withered
and fire consumed them.(X)
13 Now it is planted in the desert,(Y)
in a dry and thirsty land.(Z)
14 Fire spread from one of its main[c] branches
and consumed(AA) its fruit.
No strong branch is left on it
fit for a ruler’s scepter.’(AB)
“This is a lament(AC) and is to be used as a lament.”
Footnotes
- Ezekiel 19:7 Targum (see Septuagint); Hebrew He knew
- Ezekiel 19:10 Two Hebrew manuscripts; most Hebrew manuscripts your blood
- Ezekiel 19:14 Or from under its
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.