Add parallel Print Page Options

Za Kulangidwa kwa Igupto

30 Yehova anandiyankhula kuti: “Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.

“ ‘Ufuwule mawu awa akuti,
    ‘Kalanga, tsiku lafika!’
Pakuti tsiku layandikira,
    tsiku la Yehova lili pafupi,
tsiku la mitambo yakuda,
    tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto
    ndipo mavuto adzafika pa Kusi.
Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto,
    chuma chake chidzatengedwa
    ndipo maziko ake adzagumuka.

Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.

“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“ ‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa
    ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu.
Adzaphedwa ndi lupanga
    kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’ ”
            ndikutero Ine Ambuye Yehova.
“ ‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja
    kupambana mabwinja ena onse opasuka,
ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka
    kupambana mizinda ina yonse.
Nditatha kutentha Igupto
    ndi kupha onse omuthandiza,
    pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

“ ‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.

10 “ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni
    kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
11 Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja
    adzabwera kudzawononga dzikolo.
Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto
    ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
12 Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo
    ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa.
Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo
    pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.

Ine Yehova ndayankhula.

13 “ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzawononga mafano
    ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi.
Simudzakhalanso mfumu mu Igupto,
    ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
14 Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi,
    ndi kutentha mzinda wa Zowani.
    Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
15 Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu,
    linga lolimba la Igupto,
    ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
16 Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto;
    Peluziumu adzazunzika ndi ululu.
Malinga a Thebesi adzagumuka,
    ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
17 Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti
    adzaphedwa ndi lupanga
    ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
18 Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima
    pamene ndidzathyola goli la Igupto;
    motero kunyada kwake kudzatha.
Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda,
    ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
19 Kotero ndidzalanga dziko la Igupto,
    ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

Farao Watha Mphamvu

20 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 21 “Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga. 22 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake. 23 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. 24 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo. 25 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto. 26 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

A Lament Over Egypt

30 The word of the Lord came to me: “Son of man, prophesy and say: ‘This is what the Sovereign Lord says:

“‘Wail(A) and say,
    “Alas for that day!”
For the day is near,(B)
    the day of the Lord(C) is near—
a day of clouds,
    a time of doom for the nations.
A sword will come against Egypt,(D)
    and anguish will come upon Cush.[a](E)
When the slain fall in Egypt,
    her wealth will be carried away
    and her foundations torn down.(F)

Cush and Libya,(G) Lydia and all Arabia,(H) Kub and the people(I) of the covenant land will fall by the sword along with Egypt.(J)

“‘This is what the Lord says:

“‘The allies of Egypt will fall
    and her proud strength will fail.
From Migdol to Aswan(K)
    they will fall by the sword within her,
declares the Sovereign Lord.
“‘They will be desolate
    among desolate lands,
and their cities will lie
    among ruined cities.(L)
Then they will know that I am the Lord,
    when I set fire(M) to Egypt
    and all her helpers are crushed.(N)

“‘On that day messengers will go out from me in ships to frighten Cush(O) out of her complacency. Anguish(P) will take hold of them on the day of Egypt’s doom, for it is sure to come.(Q)

10 “‘This is what the Sovereign Lord says:

“‘I will put an end to the hordes of Egypt
    by the hand of Nebuchadnezzar(R) king of Babylon.(S)
11 He and his army—the most ruthless of nations(T)
    will be brought in to destroy the land.
They will draw their swords against Egypt
    and fill the land with the slain.(U)
12 I will dry up(V) the waters of the Nile(W)
    and sell the land to an evil nation;
by the hand of foreigners
    I will lay waste(X) the land and everything in it.

I the Lord have spoken.

13 “‘This is what the Sovereign Lord says:

“‘I will destroy the idols(Y)
    and put an end to the images in Memphis.(Z)
No longer will there be a prince in Egypt,(AA)
    and I will spread fear throughout the land.
14 I will lay(AB) waste Upper Egypt,
    set fire to Zoan(AC)
    and inflict punishment on Thebes.(AD)
15 I will pour out my wrath on Pelusium,
    the stronghold of Egypt,
    and wipe out the hordes of Thebes.
16 I will set fire(AE) to Egypt;
    Pelusium will writhe in agony.
Thebes will be taken by storm;
    Memphis(AF) will be in constant distress.
17 The young men of Heliopolis(AG) and Bubastis
    will fall by the sword,
    and the cities themselves will go into captivity.
18 Dark will be the day at Tahpanhes(AH)
    when I break the yoke of Egypt;(AI)
    there her proud strength will come to an end.
She will be covered with clouds,
    and her villages will go into captivity.(AJ)
19 So I will inflict punishment(AK) on Egypt,
    and they will know that I am the Lord.’”

Pharaoh’s Arms Are Broken

20 In the eleventh year, in the first month on the seventh day, the word of the Lord came to me:(AL) 21 “Son of man, I have broken the arm(AM) of Pharaoh(AN) king of Egypt. It has not been bound up to be healed(AO) or put in a splint so that it may become strong enough to hold a sword. 22 Therefore this is what the Sovereign Lord says: I am against Pharaoh king of Egypt.(AP) I will break both his arms, the good arm as well as the broken one, and make the sword fall from his hand.(AQ) 23 I will disperse the Egyptians among the nations and scatter them through the countries.(AR) 24 I will strengthen(AS) the arms of the king of Babylon and put my sword(AT) in his hand, but I will break the arms of Pharaoh, and he will groan(AU) before him like a mortally wounded man. 25 I will strengthen the arms of the king of Babylon, but the arms of Pharaoh will fall limp. Then they will know that I am the Lord, when I put my sword(AV) into the hand of the king of Babylon and he brandishes it against Egypt.(AW) 26 I will disperse the Egyptians among the nations and scatter them through the countries. Then they will know that I am the Lord.(AX)

Footnotes

  1. Ezekiel 30:4 That is, the upper Nile region; also in verses 5 and 9