Add parallel Print Page Options

Nyimbo ya Maliro a Farao

32 Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti: “Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti,

“Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu.
    Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja.
Umakhuvula mʼmitsinje yako,
    kuvundula madzi ndi mapazi ako
    ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.

“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri,
    ndidzakuponyera khoka langa
    ndi kukugwira mu ukonde wanga.
Ndidzakuponya ku mtunda
    ndi kukutayira pansi.
Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe,
    ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.
Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri
    ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.
Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako,
    mpaka kumapiri komwe,
    ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.
Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba
    ndikudetsa nyenyezi zake.
Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo,
    ndipo mwezi sudzawala.
Zowala zonse zamumlengalenga
    ndidzazizimitsa;
    ndidzachititsa mdima pa dziko lako,
            akutero Ambuye Yehova.
Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri
    pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,
    ku mayiko amene iwe sunawadziwe.
10 Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe,
    ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe
    pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo.
Pa nthawi ya kugwa kwako,
    aliyense wa iwo adzanjenjemera
    moyo wake wonse.

11 “ ‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti,

“ ‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni
    lidzabwera kudzalimbana nawe.
12 Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe
    ndi lupanga la anthu amphamvu,
    anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Adzathetsa kunyada kwa Igupto,
    ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.
13 Ndidzawononga ziweto zake zonse
    zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri.
Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu
    kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.
14 Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake
    ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta,
            akutero Ambuye Yehova.
15 Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja;
    ndikadzawononga dziko lonse
ndi kukantha onse okhala kumeneko,
    adzadziwa kuti ndine Yehova.’

16 “Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”

17 Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti: 18 “Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa. 19 Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’ 20 Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo. 21 Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’

22 “Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo. 23 Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.

24 “Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. 25 Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.

26 “Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. 27 Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo.

28 “Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.

29 “Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.

30 “Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.

31 “Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 32 Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

A Lament Over Pharaoh

32 In the twelfth year, in the twelfth month on the first day, the word of the Lord came to me:(A) “Son of man, take up a lament(B) concerning Pharaoh king of Egypt and say to him:

“‘You are like a lion(C) among the nations;
    you are like a monster(D) in the seas(E)
thrashing about in your streams,
    churning the water with your feet
    and muddying the streams.(F)

“‘This is what the Sovereign Lord says:

“‘With a great throng of people
    I will cast my net over you,
    and they will haul you up in my net.(G)
I will throw you on the land
    and hurl you on the open field.
I will let all the birds of the sky settle on you
    and all the animals of the wild gorge themselves on you.(H)
I will spread your flesh on the mountains
    and fill the valleys(I) with your remains.
I will drench the land with your flowing blood(J)
    all the way to the mountains,
    and the ravines will be filled with your flesh.(K)
When I snuff you out, I will cover the heavens
    and darken their stars;
I will cover the sun with a cloud,
    and the moon will not give its light.(L)
All the shining lights in the heavens
    I will darken(M) over you;
    I will bring darkness over your land,(N)
declares the Sovereign Lord.
I will trouble the hearts of many peoples
    when I bring about your destruction among the nations,
    among[a] lands you have not known.
10 I will cause many peoples to be appalled at you,
    and their kings will shudder with horror because of you
    when I brandish my sword(O) before them.
On the day(P) of your downfall
    each of them will tremble
    every moment for his life.(Q)

11 “‘For this is what the Sovereign Lord says:

“‘The sword(R) of the king of Babylon(S)
    will come against you.(T)
12 I will cause your hordes to fall
    by the swords of mighty men—
    the most ruthless of all nations.(U)
They will shatter the pride of Egypt,
    and all her hordes will be overthrown.(V)
13 I will destroy all her cattle
    from beside abundant waters
no longer to be stirred by the foot of man
    or muddied by the hooves of cattle.(W)
14 Then I will let her waters settle
    and make her streams flow like oil,
declares the Sovereign Lord.
15 When I make Egypt desolate
    and strip the land of everything in it,
when I strike down all who live there,
    then they will know that I am the Lord.(X)

16 “This is the lament(Y) they will chant for her. The daughters of the nations will chant it; for Egypt and all her hordes they will chant it, declares the Sovereign Lord.”

Egypt’s Descent Into the Realm of the Dead

17 In the twelfth year, on the fifteenth day of the month, the word of the Lord came to me:(Z) 18 “Son of man, wail for the hordes of Egypt and consign(AA) to the earth below both her and the daughters of mighty nations, along with those who go down to the pit.(AB) 19 Say to them, ‘Are you more favored than others? Go down and be laid among the uncircumcised.’(AC) 20 They will fall among those killed by the sword. The sword is drawn; let her be dragged(AD) off with all her hordes.(AE) 21 From within the realm of the dead(AF) the mighty leaders will say of Egypt and her allies, ‘They have come down and they lie with the uncircumcised,(AG) with those killed by the sword.’

22 “Assyria is there with her whole army; she is surrounded by the graves of all her slain, all who have fallen by the sword. 23 Their graves are in the depths of the pit(AH) and her army lies around her grave.(AI) All who had spread terror in the land of the living are slain, fallen by the sword.

24 “Elam(AJ) is there, with all her hordes around her grave. All of them are slain, fallen by the sword.(AK) All who had spread terror in the land of the living(AL) went down uncircumcised to the earth below. They bear their shame with those who go down to the pit.(AM) 25 A bed is made for her among the slain, with all her hordes around her grave. All of them are uncircumcised,(AN) killed by the sword. Because their terror had spread in the land of the living, they bear their shame with those who go down to the pit; they are laid among the slain.

26 “Meshek and Tubal(AO) are there, with all their hordes around their graves. All of them are uncircumcised, killed by the sword because they spread their terror in the land of the living. 27 But they do not lie with the fallen warriors of old,[b](AP) who went down to the realm of the dead with their weapons of war—their swords placed under their heads and their shields[c] resting on their bones—though these warriors also had terrorized the land of the living.

28 “You too, Pharaoh, will be broken and will lie among the uncircumcised, with those killed by the sword.

29 “Edom(AQ) is there, her kings and all her princes; despite their power, they are laid with those killed by the sword. They lie with the uncircumcised, with those who go down to the pit.(AR)

30 “All the princes of the north(AS) and all the Sidonians(AT) are there; they went down with the slain in disgrace despite the terror caused by their power. They lie uncircumcised(AU) with those killed by the sword and bear their shame with those who go down to the pit.(AV)

31 “Pharaoh—he and all his army—will see them and he will be consoled(AW) for all his hordes that were killed by the sword, declares the Sovereign Lord. 32 Although I had him spread terror in the land of the living, Pharaoh(AX) and all his hordes will be laid among the uncircumcised, with those killed by the sword, declares the Sovereign Lord.”(AY)

Footnotes

  1. Ezekiel 32:9 Hebrew; Septuagint bring you into captivity among the nations, / to
  2. Ezekiel 32:27 Septuagint; Hebrew warriors who were uncircumcised
  3. Ezekiel 32:27 Probable reading of the original Hebrew text; Masoretic Text punishment