Add parallel Print Page Options

Malo Atsopano a Nyumba ya Mulungu

40 Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu. Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda. Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera. Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”

Chipata Chakummawa

Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.

Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu. Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.

Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu. Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.

10 Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana. 11 Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka. 12 Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu. 13 Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka. 14 Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo. 15 Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27. 16 Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.

Bwalo la Kunja

17 Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo. 18 Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi. 19 Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.

Chipata Chakumpoto

20 Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja. 21 Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13. 22 Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde. 23 Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.

Chipata Chakummwera

24 Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija. 25 Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13. 26 Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma. 27 Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.

Zipata Zolowera ku Bwalo la Mʼkati

28 Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija. 29 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13. 30 (Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake). 31 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.

32 Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija. 33 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13. 34 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.

35 Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija. 36 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13. 37 Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.

Zipinda Zokonzeramo Nsembe

38 Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza. 39 Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula. 40 Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero. 41 Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza. 42 Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina. 43 Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.

Zipinda za Ansembe

44 Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto. 45 Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu, 46 ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”

47 Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.

Nyumba ya Mulungu

48 Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse. 49 Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.

The Temple Area Restored

40 In the twenty-fifth year of our exile, at the beginning of the year, on the tenth of the month, in the fourteenth year after the fall of the city(A)—on that very day the hand of the Lord was on me(B) and he took me there. In visions(C) of God he took me to the land of Israel and set me on a very high mountain,(D) on whose south side were some buildings that looked like a city. He took me there, and I saw a man whose appearance was like bronze;(E) he was standing in the gateway with a linen cord and a measuring rod(F) in his hand. The man said to me, “Son of man, look carefully and listen closely and pay attention to everything I am going to show you,(G) for that is why you have been brought here. Tell(H) the people of Israel everything you see.(I)

The East Gate to the Outer Court

I saw a wall completely surrounding the temple area. The length of the measuring rod in the man’s hand was six long cubits,[a] each of which was a cubit and a handbreadth. He measured(J) the wall; it was one measuring rod thick and one rod high.

Then he went to the east gate.(K) He climbed its steps and measured the threshold of the gate; it was one rod deep. The alcoves(L) for the guards were one rod long and one rod wide, and the projecting walls between the alcoves were five cubits[b] thick. And the threshold of the gate next to the portico facing the temple was one rod deep.

Then he measured the portico of the gateway; it[c] was eight cubits[d] deep and its jambs were two cubits[e] thick. The portico of the gateway faced the temple.

10 Inside the east gate were three alcoves on each side; the three had the same measurements, and the faces of the projecting walls on each side had the same measurements. 11 Then he measured the width of the entrance of the gateway; it was ten cubits and its length was thirteen cubits.[f] 12 In front of each alcove was a wall one cubit high, and the alcoves were six cubits square. 13 Then he measured the gateway from the top of the rear wall of one alcove to the top of the opposite one; the distance was twenty-five cubits[g] from one parapet opening to the opposite one. 14 He measured along the faces of the projecting walls all around the inside of the gateway—sixty cubits.[h] The measurement was up to the portico[i] facing the courtyard.[j](M) 15 The distance from the entrance of the gateway to the far end of its portico was fifty cubits.[k] 16 The alcoves and the projecting walls inside the gateway were surmounted by narrow parapet openings all around, as was the portico; the openings all around faced inward. The faces of the projecting walls were decorated with palm trees.(N)

The Outer Court

17 Then he brought me into the outer court.(O) There I saw some rooms and a pavement that had been constructed all around the court; there were thirty rooms(P) along the pavement.(Q) 18 It abutted the sides of the gateways and was as wide as they were long; this was the lower pavement. 19 Then he measured the distance from the inside of the lower gateway to the outside of the inner court;(R) it was a hundred cubits[l](S) on the east side as well as on the north.

The North Gate

20 Then he measured the length and width of the north gate, leading into the outer court. 21 Its alcoves(T)—three on each side—its projecting walls and its portico(U) had the same measurements as those of the first gateway. It was fifty cubits long and twenty-five cubits wide. 22 Its openings, its portico(V) and its palm tree decorations had the same measurements as those of the gate facing east. Seven steps led up to it, with its portico opposite them.(W) 23 There was a gate to the inner court facing the north gate, just as there was on the east. He measured from one gate to the opposite one; it was a hundred cubits.(X)

The South Gate

24 Then he led me to the south side and I saw the south gate. He measured its jambs and its portico, and they had the same measurements(Y) as the others. 25 The gateway and its portico had narrow openings all around, like the openings of the others. It was fifty cubits long and twenty-five cubits wide.(Z) 26 Seven steps led up to it, with its portico opposite them; it had palm tree decorations on the faces of the projecting walls on each side.(AA) 27 The inner court(AB) also had a gate facing south, and he measured from this gate to the outer gate on the south side; it was a hundred cubits.(AC)

The Gates to the Inner Court

28 Then he brought me into the inner court through the south gate, and he measured the south gate; it had the same measurements(AD) as the others. 29 Its alcoves,(AE) its projecting walls and its portico had the same measurements as the others. The gateway and its portico had openings all around. It was fifty cubits long and twenty-five cubits wide.(AF) 30 (The porticoes(AG) of the gateways around the inner court were twenty-five cubits wide and five cubits deep.) 31 Its portico(AH) faced the outer court; palm trees decorated its jambs, and eight steps led up to it.(AI)

32 Then he brought me to the inner court on the east side, and he measured the gateway; it had the same measurements(AJ) as the others. 33 Its alcoves,(AK) its projecting walls and its portico had the same measurements as the others. The gateway and its portico had openings all around. It was fifty cubits long and twenty-five cubits wide. 34 Its portico(AL) faced the outer court; palm trees decorated the jambs on either side, and eight steps led up to it.

35 Then he brought me to the north gate(AM) and measured it. It had the same measurements(AN) as the others, 36 as did its alcoves,(AO) its projecting walls and its portico, and it had openings all around. It was fifty cubits long and twenty-five cubits wide. 37 Its portico[m](AP) faced the outer court; palm trees decorated the jambs on either side, and eight steps led up to it.(AQ)

The Rooms for Preparing Sacrifices

38 A room with a doorway was by the portico in each of the inner gateways, where the burnt offerings(AR) were washed. 39 In the portico of the gateway were two tables on each side, on which the burnt offerings,(AS) sin offerings[n](AT) and guilt offerings(AU) were slaughtered.(AV) 40 By the outside wall of the portico of the gateway, near the steps at the entrance of the north gateway were two tables, and on the other side of the steps were two tables. 41 So there were four tables on one side of the gateway and four on the other—eight tables in all—on which the sacrifices were slaughtered. 42 There were also four tables of dressed stone(AW) for the burnt offerings, each a cubit and a half long, a cubit and a half wide and a cubit high.[o] On them were placed the utensils for slaughtering the burnt offerings and the other sacrifices.(AX) 43 And double-pronged hooks, each a handbreadth[p] long, were attached to the wall all around. The tables were for the flesh of the offerings.

The Rooms for the Priests

44 Outside the inner gate, within the inner court, were two rooms, one[q] at the side of the north gate and facing south, and another at the side of the south[r] gate and facing north. 45 He said to me, “The room facing south is for the priests who guard the temple,(AY) 46 and the room facing north(AZ) is for the priests who guard the altar.(BA) These are the sons of Zadok,(BB) who are the only Levites who may draw near to the Lord to minister before him.(BC)

47 Then he measured the court: It was square—a hundred cubits long and a hundred cubits wide. And the altar was in front of the temple.(BD)

The New Temple

48 He brought me to the portico of the temple(BE) and measured the jambs of the portico; they were five cubits wide on either side. The width of the entrance was fourteen cubits[s] and its projecting walls were[t] three cubits[u] wide on either side. 49 The portico(BF) was twenty cubits[v] wide, and twelve[w] cubits[x] from front to back. It was reached by a flight of stairs,[y] and there were pillars(BG) on each side of the jambs.

Footnotes

  1. Ezekiel 40:5 That is, about 11 feet or about 3.2 meters; also in verse 12. The long cubit of about 21 inches or about 53 centimeters is the basic unit of measurement of length throughout chapters 40–48.
  2. Ezekiel 40:7 That is, about 8 3/4 feet or about 2.7 meters; also in verse 48
  3. Ezekiel 40:9 Many Hebrew manuscripts, Septuagint, Vulgate and Syriac; most Hebrew manuscripts gateway facing the temple; it was one rod deep. Then he measured the portico of the gateway; it
  4. Ezekiel 40:9 That is, about 14 feet or about 4.2 meters
  5. Ezekiel 40:9 That is, about 3 1/2 feet or about 1 meter
  6. Ezekiel 40:11 That is, about 18 feet wide and 23 feet long or about 5.3 meters wide and 6.9 meters long
  7. Ezekiel 40:13 That is, about 44 feet or about 13 meters; also in verses 21, 25, 29, 30, 33 and 36
  8. Ezekiel 40:14 That is, about 105 feet or about 32 meters
  9. Ezekiel 40:14 Septuagint; Hebrew projecting wall
  10. Ezekiel 40:14 The meaning of the Hebrew for this verse is uncertain.
  11. Ezekiel 40:15 That is, about 88 feet or about 27 meters; also in verses 21, 25, 29, 33 and 36
  12. Ezekiel 40:19 That is, about 175 feet or about 53 meters; also in verses 23, 27 and 47
  13. Ezekiel 40:37 Septuagint (see also verses 31 and 34); Hebrew jambs
  14. Ezekiel 40:39 Or purification offerings
  15. Ezekiel 40:42 That is, about 2 2/3 feet long and wide and 21 inches high or about 80 centimeters long and wide and 53 centimeters high
  16. Ezekiel 40:43 That is, about 3 1/2 inches or about 9 centimeters
  17. Ezekiel 40:44 Septuagint; Hebrew were rooms for singers, which were
  18. Ezekiel 40:44 Septuagint; Hebrew east
  19. Ezekiel 40:48 That is, about 25 feet or about 7.4 meters
  20. Ezekiel 40:48 Septuagint; Hebrew entrance was
  21. Ezekiel 40:48 That is, about 5 1/4 feet or about 1.6 meters
  22. Ezekiel 40:49 That is, about 35 feet or about 11 meters
  23. Ezekiel 40:49 Septuagint; Hebrew eleven
  24. Ezekiel 40:49 That is, about 21 feet or about 6.4 meters
  25. Ezekiel 40:49 Hebrew; Septuagint Ten steps led up to it