Add parallel Print Page Options

Zipinda za Ansembe

42 Pambuyo pake munthuyo anapita nane ku bwalo lakunja chakumpoto ndipo anafika nane ku zipinda zoyangʼanana ndi bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ina yakumpoto. Nyumba yakumpotoyi mulitali mwake munali mamita makumi asanu, mulifupi mwake munali mamita 25. Panali midadada iwiri, umodzi umayangʼanana ndi bwalo lamʼkati la mamita khumi, winawo umayangʼanana ndi bwalo lakunja. Midadada iwiriyi inali ya nyumba zitatu zosanjikana ndipo imayangʼanana. Kumaso kwa zipindazo kunali njira yamʼkati, mulifupi mwake munali mamita asanu, mulitali mwake munali mamita makumi asanu. Makomo ake analoza chakumpoto. Zipinda zammwamba zinali zazifupi mʼmimbamu kupambana zipinda zamʼmunsi ndi zipinda zapakati chifukwa njira zake zinatenga malo ambiri. Popeza zipinda zinali zosanjikizana katatu ndipo zinalibe nsanamira monga za mabwalo, motero zipinda zamʼmwamba zinali zochepa kuyerekeza ndi zipinda zapansi ndi zipinda zapakati. Panali khoma lakunja lomwe limatsatana ndi zipindazo kutsogolo kwake pambali pabwalo lakunja, kutalika kwake kunali mamita 25. Zipinda za mʼmbali mwa bwalo lakunja mulitali mwake munali mamita 25. Koma zomwe zinali mʼmbali mwa Nyumba ya Mulungu, mulitali mwake munali mamita makumi asanu. Pansi pa zipinda zimenezi panali khomo chakummawa kuchokera ku bwalo lakunja kumene khoma lake linkayambira.

10 Mbali yakummwera kuyangʼanana ndi bwalo ndi nyumbayo kunali zipinda zina. 11 Kumaso kwa zipindazi kunali njira. Zipindazi mulitali mwake, mulifupi mwake ndiponso maonekedwe ake onse zinali zofanana ndi zipinda zoyangʼana zakumpoto zija. Makomo ndi zitseko zake zinalinso zofanana 12 ndi makomo a zipinda zakummwera. Kunali khomo mʼmbali ya kummawa kumene ankalowerako. Kunalinso khoma logawa zipinda.

13 Ndipo munthuyo anandiwuza kuti, “Zipinda zakumpoto ndi zakummwera zoyangʼanana ndi bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi zoyera. Mʼmenemo ansembe amene amakhala pafupi ndi Yehova amadyeramo zopereka zopatulika kwambiri. Mʼmenemo adzayikamo zopereka zopatulika kwambiri, zopereka za chakudya, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula, poti malowo ndi opatulika. 14 Pamene ansembe alowa ku malo opatulikawa, asatuluke kupita ku bwalo lakunja popanda kusiya momwemo zovala zimene anavala potumikira zija, pakuti zovalazi ndi zopatulika. Avale kaye zovala zina ndipo akhoza kufika kwa anthu.”

15 Munthuyo atamaliza kuyeza zimene zinali mʼkati mwa Nyumba ya Mulungu, anatuluka nane pa chipata chakummawa ndi kuyeza bwalo lonse. 16 Anayeza mbali yakummawa ndi ndodo yake yoyezera; kutalika kwake kunali mamita 250. 17 Anayeza mbali ya kumpoto ndi ndodo yake; kutalika kwake kunali mamita 250. 18 Munthuyo anayeza mbali yakummwera; kutalika kwake kunali mamita 250 atayeza ndi ndodo yake. 19 Kenaka anatembenukira ku mbali ya kumadzulo ndi kuyeza ndi ndodo yake; kutalika kwake kunali mamita 250 atayeza ndi ndodo yake. 20 Motero anayeza mbali zonse zinayi. Panali khoma lozungulira bwalolo mulitali mwake munali mamita 250 ndipo mulifupi mwake munalinso mamita 250. Khomalo linali lolekanitsa zinthu zoyera ndi zinthu wamba.

The Rooms for the Priests

42 Then the man led me northward into the outer court and brought me to the rooms(A) opposite the temple courtyard(B) and opposite the outer wall on the north side.(C) The building whose door faced north was a hundred cubits long and fifty cubits wide.[a] Both in the section twenty cubits[b] from the inner court and in the section opposite the pavement of the outer court, gallery(D) faced gallery at the three levels.(E) In front of the rooms was an inner passageway ten cubits wide and a hundred cubits[c] long.[d] Their doors were on the north.(F) Now the upper rooms were narrower, for the galleries took more space from them than from the rooms on the lower and middle floors of the building. The rooms on the top floor had no pillars, as the courts had; so they were smaller in floor space than those on the lower and middle floors. There was an outer wall parallel to the rooms and the outer court; it extended in front of the rooms for fifty cubits. While the row of rooms on the side next to the outer court was fifty cubits long, the row on the side nearest the sanctuary was a hundred cubits long. The lower rooms had an entrance(G) on the east side as one enters them from the outer court.

10 On the south side[e] along the length of the wall of the outer court, adjoining the temple courtyard(H) and opposite the outer wall, were rooms(I) 11 with a passageway in front of them. These were like the rooms on the north; they had the same length and width, with similar exits and dimensions. Similar to the doorways on the north 12 were the doorways of the rooms on the south. There was a doorway at the beginning of the passageway that was parallel to the corresponding wall extending eastward, by which one enters the rooms.

13 Then he said to me, “The north(J) and south rooms(K) facing the temple courtyard(L) are the priests’ rooms, where the priests who approach the Lord will eat the most holy offerings. There they will put the most holy offerings—the grain offerings,(M) the sin offerings[f](N) and the guilt offerings(O)—for the place is holy.(P) 14 Once the priests enter the holy precincts, they are not to go into the outer court until they leave behind the garments(Q) in which they minister, for these are holy. They are to put on other clothes before they go near the places that are for the people.(R)

15 When he had finished measuring what was inside the temple area, he led me out by the east gate(S) and measured the area all around: 16 He measured the east side with the measuring rod; it was five hundred cubits.[g][h] 17 He measured the north side; it was five hundred cubits[i] by the measuring rod. 18 He measured the south side; it was five hundred cubits by the measuring rod. 19 Then he turned to the west side and measured; it was five hundred cubits by the measuring rod. 20 So he measured(T) the area(U) on all four sides. It had a wall around it,(V) five hundred cubits long and five hundred cubits wide,(W) to separate the holy from the common.(X)

Footnotes

  1. Ezekiel 42:2 That is, about 175 feet long and 88 feet wide or about 53 meters long and 27 meters wide
  2. Ezekiel 42:3 That is, about 35 feet or about 11 meters
  3. Ezekiel 42:4 Septuagint and Syriac; Hebrew and one cubit
  4. Ezekiel 42:4 That is, about 18 feet wide and 175 feet long or about 5.3 meters wide and 53 meters long
  5. Ezekiel 42:10 Septuagint; Hebrew Eastward
  6. Ezekiel 42:13 Or purification offerings
  7. Ezekiel 42:16 See Septuagint of verse 17; Hebrew rods; also in verses 18 and 19.
  8. Ezekiel 42:16 Five hundred cubits equal about 875 feet or about 265 meters; also in verses 17, 18 and 19.
  9. Ezekiel 42:17 Septuagint; Hebrew rods