Add parallel Print Page Options

Uneneri Wotsutsa Mapiri a Israeli

Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti, “Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano. Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu. Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe. Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu. Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’

“Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina. Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata. 10 Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.

11 “Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri. 12 Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo. 13 Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse. 14 Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

Doom for the Mountains of Israel

The word of the Lord came to me: “Son of man, set your face(A) against the mountains(B) of Israel; prophesy against them(C) and say: ‘You mountains of Israel, hear the word of the Sovereign Lord. This is what the Sovereign Lord says to the mountains and hills, to the ravines and valleys:(D) I am about to bring a sword against you, and I will destroy your high places.(E) Your altars will be demolished and your incense altars(F) will be smashed; and I will slay your people in front of your idols.(G) I will lay the dead bodies of the Israelites in front of their idols, and I will scatter your bones(H) around your altars.(I) Wherever you live,(J) the towns will be laid waste and the high places(K) demolished, so that your altars will be laid waste and devastated, your idols(L) smashed and ruined, your incense altars(M) broken down, and what you have made wiped out.(N) Your people will fall slain(O) among you, and you will know that I am the Lord.(P)

“‘But I will spare some, for some of you will escape(Q) the sword when you are scattered among the lands and nations.(R) Then in the nations where they have been carried captive, those who escape will remember(S) me—how I have been grieved(T) by their adulterous hearts, which have turned away from me, and by their eyes, which have lusted after their idols.(U) They will loathe themselves for the evil(V) they have done and for all their detestable practices.(W) 10 And they will know that I am the Lord;(X) I did not threaten in vain to bring this calamity on them.(Y)

11 “‘This is what the Sovereign Lord says: Strike your hands together and stamp your feet and cry out “Alas!” because of all the wicked and detestable practices of the people of Israel, for they will fall by the sword, famine and plague.(Z) 12 One who is far away will die of the plague, and one who is near will fall by the sword, and anyone who survives and is spared will die of famine. So will I pour out my wrath(AA) on them.(AB) 13 And they will know that I am the Lord, when their people lie slain among their idols(AC) around their altars, on every high hill and on all the mountaintops, under every spreading tree and every leafy oak(AD)—places where they offered fragrant incense to all their idols.(AE) 14 And I will stretch out my hand(AF) against them and make the land a desolate waste from the desert to Diblah[a]—wherever they live. Then they will know that I am the Lord.(AG)’”

Footnotes

  1. Ezekiel 6:14 Most Hebrew manuscripts; a few Hebrew manuscripts Riblah