Add parallel Print Page Options

Chimaliziro Chafika

Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti, “Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti:

“Chimaliziro! Chimaliziro chafika
    ku ngodya zinayi za dziko.
Chimaliziro chili pa iwe tsopano.
    Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe.
Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako
    ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
Ine sindidzakumvera chisoni
    kapena kukuleka.
Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa
    komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako.

Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

“Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi:

“Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo!
    Taona chikubwera!
Chimaliziro chafika!
    Chimaliziro chafika!
Chiwonongeko chakugwera.
    Taona chafika!
Inu anthu okhala mʼdziko,
    chiwonongeko chakugwerani.
Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
Ine ndili pafupi kukukwiyirani,
    ndipo ukali wanga udzathera pa iwe;
Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako
    ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
Ine sindidzakumvera chisoni
    kapena kukuleka.
Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako
ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.

‘Pamenepo udzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndimakantha.’

10 “Taona, tsikulo!
    Taona, lafika!
Chiwonongeko chako chabwera.
    Ndodo yaphuka mphundu za maluwa.
    Kudzitama kwaphuka.
11 Chiwawa chasanduka ndodo
    yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo.
Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale.
    Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo.
Palibiretu ndipo sipadzapezeka
    munthu wowalira maliro.
12 Nthawi yafika!
    Tsiku layandikira!
Munthu wogula asakondwere
    ndipo wogulitsa asamve chisoni,
    popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
13 Wogulitsa sadzazipezanso zinthu
    zimene anagulitsa kwa wina
    chinkana onse awiri akanali ndi moyo,
pakuti chilango chidzagwera onsewo
    ndipo sichingasinthike.
Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense
    amene adzapulumutsa moyo wake.

14 “Lipenga lalira,
    ndipo zonse zakonzeka.
Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo,
    pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
15 Ku bwalo kuli kumenyana
    ndipo mʼkati muli mliri ndi njala.
Anthu okhala ku midzi
    adzafa ndi nkhondo.
Iwo okhala ku mizinda
    adzafa ndi mliri ndi njala.
16 Onse amene adzapulumuka
    ndi kumakakhala ku mapiri,
azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa.
    Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
17 Dzanja lililonse lidzalefuka,
    ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
18 Iwo adzavala ziguduli
    ndipo adzagwidwa ndi mantha.
Adzakhala ndi nkhope zamanyazi
    ndipo mitu yawo adzameta mpala.

19 “Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu
    ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa.
Siliva ndi golide wawo
    sizidzatha kuwapulumutsa
    pa tsiku la ukali wa Yehova.
Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala,
    kapena kukhala okhuta,
    pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
20 Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka
    ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa
    kukhala zowanyansa.
21 Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe.
    Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda
    ndi kudziyipitsa.
22 Ine ndidzawalekerera anthuwo
    ndipo adzayipitsa malo anga apamtima.
Adzalowamo ngati mbala
    ndi kuyipitsamo.

23 “Konzani maunyolo,

    chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo
    ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
24 Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa
    kuti idzalande nyumba zawo.
Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu
    pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
25 Nkhawa ikadzawafikira
    adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
26 Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake,
    ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake.
Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri.
    Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo,
    ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
27 Mfumu idzalira,
    kalonga adzagwidwa ndi mantha.
    Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha.
Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo,
    ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.

Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”