Add parallel Print Page Options

Opembedza Mafano Aphedwa

Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.” Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.

Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”

Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo. Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.

Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse. Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”

Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’ 10 Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”

11 Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”

Judgment on the Idolaters

Then I heard him call out in a loud voice, “Bring near those who are appointed to execute judgment on the city, each with a weapon in his hand.” And I saw six men coming from the direction of the upper gate, which faces north, each with a deadly weapon in his hand. With them was a man clothed in linen(A) who had a writing kit at his side. They came in and stood beside the bronze altar.

Now the glory(B) of the God of Israel went up from above the cherubim,(C) where it had been, and moved to the threshold of the temple. Then the Lord called to the man clothed in linen who had the writing kit at his side and said to him, “Go throughout the city of Jerusalem(D) and put a mark(E) on the foreheads of those who grieve and lament(F) over all the detestable things that are done in it.(G)

As I listened, he said to the others, “Follow him through the city and kill, without showing pity(H) or compassion.(I) Slaughter(J) the old men, the young men and women, the mothers and children,(K) but do not touch anyone who has the mark.(L) Begin at my sanctuary.” So they began with the old men(M) who were in front of the temple.(N)

Then he said to them, “Defile the temple and fill the courts with the slain.(O) Go!” So they went out and began killing throughout the city. While they were killing and I was left alone, I fell facedown,(P) crying out, “Alas, Sovereign Lord!(Q) Are you going to destroy the entire remnant of Israel in this outpouring of your wrath(R) on Jerusalem?(S)

He answered me, “The sin of the people of Israel and Judah is exceedingly great; the land is full of bloodshed and the city is full of injustice.(T) They say, ‘The Lord has forsaken the land; the Lord does not see.’(U) 10 So I will not look on them with pity(V) or spare them, but I will bring down on their own heads what they have done.(W)

11 Then the man in linen with the writing kit at his side brought back word, saying, “I have done as you commanded.”