Add parallel Print Page Options

Chiyambi cha Chilengedwe

Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi. Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.

Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi. Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima. Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.

Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.” Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi. Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.

Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi. 10 Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.

11 Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi. 12 Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino. 13 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.

14 Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka; 15 zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.” 16 Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi. 17 Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi, 18 kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino. 19 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.

20 Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.” 21 Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino. 22 Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.” 23 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.

24 Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi. 25 Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.

26 Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”

27 Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.
    Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu;
    analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.

28 Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”

29 Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu. 30 Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.

31 Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.

The Beginning

In the beginning(A) God created(B) the heavens(C) and the earth.(D) Now the earth was formless(E) and empty,(F) darkness was over the surface of the deep,(G) and the Spirit of God(H) was hovering(I) over the waters.

And God said,(J) “Let there be light,” and there was light.(K) God saw that the light was good,(L) and he separated the light from the darkness.(M) God called(N) the light “day,” and the darkness he called “night.”(O) And there was evening, and there was morning(P)—the first day.

And God said,(Q) “Let there be a vault(R) between the waters(S) to separate water from water.” So God made the vault and separated the water under the vault from the water above it.(T) And it was so.(U) God called(V) the vault “sky.”(W) And there was evening, and there was morning(X)—the second day.

And God said, “Let the water under the sky be gathered to one place,(Y) and let dry ground(Z) appear.” And it was so.(AA) 10 God called(AB) the dry ground “land,” and the gathered waters(AC) he called “seas.”(AD) And God saw that it was good.(AE)

11 Then God said, “Let the land produce vegetation:(AF) seed-bearing plants and trees on the land that bear fruit with seed in it, according to their various kinds.(AG)” And it was so.(AH) 12 The land produced vegetation: plants bearing seed according to their kinds(AI) and trees bearing fruit with seed in it according to their kinds. And God saw that it was good.(AJ) 13 And there was evening, and there was morning(AK)—the third day.

14 And God said, “Let there be lights(AL) in the vault of the sky to separate the day from the night,(AM) and let them serve as signs(AN) to mark sacred times,(AO) and days and years,(AP) 15 and let them be lights in the vault of the sky to give light on the earth.” And it was so.(AQ) 16 God made two great lights—the greater light(AR) to govern(AS) the day and the lesser light to govern(AT) the night.(AU) He also made the stars.(AV) 17 God set them in the vault of the sky to give light on the earth, 18 to govern the day and the night,(AW) and to separate light from darkness. And God saw that it was good.(AX) 19 And there was evening, and there was morning(AY)—the fourth day.

20 And God said, “Let the water teem with living creatures,(AZ) and let birds fly above the earth across the vault of the sky.”(BA) 21 So God created(BB) the great creatures of the sea(BC) and every living thing with which the water teems and that moves about in it,(BD) according to their kinds, and every winged bird according to its kind.(BE) And God saw that it was good.(BF) 22 God blessed them and said, “Be fruitful and increase in number and fill the water in the seas, and let the birds increase on the earth.”(BG) 23 And there was evening, and there was morning(BH)—the fifth day.

24 And God said, “Let the land produce living creatures(BI) according to their kinds:(BJ) the livestock, the creatures that move along the ground, and the wild animals, each according to its kind.” And it was so.(BK) 25 God made the wild animals(BL) according to their kinds, the livestock according to their kinds, and all the creatures that move along the ground according to their kinds.(BM) And God saw that it was good.(BN)

26 Then God said, “Let us(BO) make mankind(BP) in our image,(BQ) in our likeness,(BR) so that they may rule(BS) over the fish in the sea and the birds in the sky,(BT) over the livestock and all the wild animals,[a] and over all the creatures that move along the ground.”

27 So God created(BU) mankind(BV) in his own image,(BW)
    in the image of God(BX) he created them;
    male and female(BY) he created them.(BZ)

28 God blessed them and said to them,(CA) “Be fruitful and increase in number;(CB) fill the earth(CC) and subdue it. Rule over(CD) the fish in the sea and the birds in the sky and over every living creature that moves on the ground.(CE)

29 Then God said, “I give you every seed-bearing plant on the face of the whole earth and every tree that has fruit with seed in it. They will be yours for food.(CF) 30 And to all the beasts of the earth and all the birds in the sky and all the creatures that move along the ground—everything that has the breath of life(CG) in it—I give every green plant for food.(CH)” And it was so.

31 God saw all that he had made,(CI) and it was very good.(CJ) And there was evening, and there was morning(CK)—the sixth day.

Footnotes

  1. Genesis 1:26 Probable reading of the original Hebrew text (see Syriac); Masoretic Text the earth