Add parallel Print Page Options

Mndandanda wa Mitundu ya Anthu

10 Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.

Banja la Yafeti

Ana aamuna a Yafeti anali:

Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.

Ana aamuna a Gomeri anali:

Asikenazi, Rifati ndi Togarima.

Ana aamuna a Yavani anali:

Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu. (Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).

Banja la Hamu

Ana aamuna a Hamu anali:

Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.

Ana aamuna a Kusi anali:

Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka.

Ana aamuna a Raama anali:

Seba ndi Dedani.

Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi. Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.” 10 Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara. 11 Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala, 12 ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.

13 Igupto ndiye kholo la

Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu, 14 Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).

15 Kanaani anabereka mwana wake wachisamba,

Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti; 16 Ayebusi, Aamori, Agirigasi; 17 Ahivi, Aariki, Asini, 18 Aaravadi, Azemari ndi Ahamati.

Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse, 19 mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.

20 Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.

Banja la Semu

21 Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.

22 Ana aamuna a Semu anali:

Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.

23 Ana aamuna a Aramu anali:

Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.

24 Aripakisadi anabereka Sela,

ndipo Selayo anabereka Eberi.

25 A Eberi anabereka ana aamuna awiri:

Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.

26 Yokitani anabereka

Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera, 27 Hadoramu, Uzali, Dikila, 28 Obali, Abimaeli, Seba, 29 Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.

30 Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.

31 Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.

32 Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.

The Table of Nations

10 This is the account(A) of Shem, Ham and Japheth,(B) Noah’s sons,(C) who themselves had sons after the flood.

The Japhethites(D)

The sons[a] of Japheth:

Gomer,(E) Magog,(F) Madai, Javan,(G) Tubal,(H) Meshek(I) and Tiras.

The sons of Gomer:

Ashkenaz,(J) Riphath and Togarmah.(K)

The sons of Javan:

Elishah,(L) Tarshish,(M) the Kittites(N) and the Rodanites.[b] (From these the maritime peoples spread out into their territories by their clans within their nations, each with its own language.)(O)

The Hamites(P)

The sons of Ham:

Cush,(Q) Egypt, Put(R) and Canaan.(S)

The sons of Cush:

Seba,(T) Havilah,(U) Sabtah, Raamah(V) and Sabteka.

The sons of Raamah:

Sheba(W) and Dedan.(X)

Cush was the father[c] of Nimrod,(Y) who became a mighty warrior on the earth. He was a mighty(Z) hunter(AA) before the Lord; that is why it is said, “Like Nimrod, a mighty hunter before the Lord.” 10 The first centers of his kingdom were Babylon,(AB) Uruk,(AC) Akkad and Kalneh,(AD) in[d] Shinar.[e](AE) 11 From that land he went to Assyria,(AF) where he built Nineveh,(AG) Rehoboth Ir,[f] Calah 12 and Resen, which is between Nineveh and Calah—which is the great city.

13 Egypt was the father of

the Ludites, Anamites, Lehabites, Naphtuhites, 14 Pathrusites, Kasluhites (from whom the Philistines(AH) came) and Caphtorites.(AI)

15 Canaan(AJ) was the father of

Sidon(AK) his firstborn,[g](AL) and of the Hittites,(AM) 16 Jebusites,(AN) Amorites,(AO) Girgashites,(AP) 17 Hivites,(AQ) Arkites, Sinites, 18 Arvadites,(AR) Zemarites and Hamathites.(AS)

Later the Canaanite(AT) clans scattered 19 and the borders of Canaan(AU) reached from Sidon(AV) toward Gerar(AW) as far as Gaza,(AX) and then toward Sodom, Gomorrah, Admah and Zeboyim,(AY) as far as Lasha.

20 These are the sons of Ham by their clans and languages, in their territories and nations.

The Semites(AZ)

21 Sons were also born to Shem, whose older brother was[h] Japheth; Shem was the ancestor of all the sons of Eber.(BA)

22 The sons of Shem:

Elam,(BB) Ashur,(BC) Arphaxad,(BD) Lud and Aram.(BE)

23 The sons of Aram:

Uz,(BF) Hul, Gether and Meshek.[i]

24 Arphaxad was the father of[j] Shelah,

and Shelah the father of Eber.(BG)

25 Two sons were born to Eber:

One was named Peleg,[k] because in his time the earth was divided; his brother was named Joktan.

26 Joktan was the father of

Almodad, Sheleph, Hazarmaveth, Jerah, 27 Hadoram, Uzal,(BH) Diklah, 28 Obal, Abimael, Sheba,(BI) 29 Ophir,(BJ) Havilah and Jobab. All these were sons of Joktan.

30 The region where they lived stretched from Mesha toward Sephar, in the eastern hill country.

31 These are the sons of Shem by their clans and languages, in their territories and nations.

32 These are the clans of Noah’s sons,(BK) according to their lines of descent, within their nations. From these the nations spread out over the earth(BL) after the flood.

Footnotes

  1. Genesis 10:2 Sons may mean descendants or successors or nations; also in verses 3, 4, 6, 7, 20-23, 29 and 31.
  2. Genesis 10:4 Some manuscripts of the Masoretic Text and Samaritan Pentateuch (see also Septuagint and 1 Chron. 1:7); most manuscripts of the Masoretic Text Dodanites
  3. Genesis 10:8 Father may mean ancestor or predecessor or founder; also in verses 13, 15, 24 and 26.
  4. Genesis 10:10 Or Uruk and Akkad—all of them in
  5. Genesis 10:10 That is, Babylonia
  6. Genesis 10:11 Or Nineveh with its city squares
  7. Genesis 10:15 Or of the Sidonians, the foremost
  8. Genesis 10:21 Or Shem, the older brother of
  9. Genesis 10:23 See Septuagint and 1 Chron. 1:17; Hebrew Mash.
  10. Genesis 10:24 Hebrew; Septuagint father of Cainan, and Cainan was the father of
  11. Genesis 10:25 Peleg means division.