Add parallel Print Page Options

Kubadwa kwa Isake

21 Yehova anakomera mtima Sara monga ananenera, ndipo Yehovayo anachita monga momwe analonjezera. Sara anakhala ndi pathupi ndipo anamuberekera Abrahamu mwana wamwamuna mu ukalamba wake, pa nyengo imene Mulungu anamulonjeza. Abrahamu anapereka dzina loti Isake kwa mwana wamwamuna amene Sara anamuberekera. Isake atakwanitsa masiku asanu ndi atatu, Abrahamu anamuchita mdulidwe monga Mulungu anamulamulira. Abrahamu anali ndi 100 pamene mwana wake Isake anabadwa.

Sara anati, “Mulungu wandibweretsera mseko, ndipo aliyense amene adzamva zimenezi adzaseka nane pamodzi.” Ndipo anawonjezera kuti, “Ndani akanamuwuza Abrahamu kuti Sara nʼkudzayamwitsako ana? Chonsecho ndamubalira mwana wamwamuna kuwukalamba wake.”

Kuchotsedwa kwa Hagara ndi Ismaeli

Mwana uja anakula mpaka kumuletsa kuyamwa. Tsiku lomuletsa Isake kuyamwa, Abrahamu anakonza phwando lalikulu. Koma Sara anaona kuti mwana wamwamuna amene Hagara Mwigupto anamuberekera Abrahamu amamuseka, 10 ndipo anati kwa Abrahamu, “Muchotse mdzakazi ndi mwana wake wamwamunayu, pakuti mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wanga Isake.”

11 Nkhaniyi inamumvetsa chisoni kwambiri Abrahamu chifukwa imakhudza mwana wake. 12 Koma Mulungu anamuwuza Abrahamu kuti, “Usamve chisoni motero ndi mnyamatayu ndi mdzakazi wakoyu. Mvetsera chilichonse chomwe Sara akukuwuza, chifukwa zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake. 13 Mwana wa mdzakazi wakoyu ndidzamusandutsa mtundu wa anthu chifukwa ndi mwana wako.”

14 Mmamawa wake, Abrahamu anatenga chakudya ndi botolo la madzi nazipereka kwa Hagara. Anasenzetsa Hagara nawaperekeza pangʼono ndi mnyamatayo. Hagara ananyamuka nayendayenda mʼchipululu cha Beeriseba.

15 Madzi atatha mʼbotolo muja, anamuyika mnyamatayo pansi pa zitsamba. 16 Kenaka Hagara anachoka nakakhala pansi cha pakatalipo, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi, popeza mʼmaganizo mwake amati, “Sindingaonerere mwanayu akufa.” Ndipo anakhala pansi cha poteropo nʼkumalira.

17 Mulungu anamva mnyamatayo akulira ndipo mngelo wa Mulungu anayankhula kwa Hagara kuchokera kumwamba nati, “Chavuta nʼchiyani Hagara? Usachite mantha; Mulungu wamva kulira kwa mnyamatayo pamene wagonapo. 18 Munyamule mnyamatayo ndipo umugwire dzanja pakuti ndidzamupanga kukhala mtundu waukulu.”

19 Kenaka Mulungu anatsekula maso a Hagara ndipo anaona chitsime cha madzi. Choncho anapita nadzaza botolo lija ndi madzi ndi kumupatsa mnyamatayo kuti amwe.

20 Mulungu anali ndi mnyamatayo pamene ankakula. Anakhala ku chipululu nakhala katswiri wolasa uta. 21 Akukhala ku chipululu cha Parani, mayi ake anamupezera mkazi wochokera ku Igupto.

Pangano la ku Beeriseba

22 Pa nthawiyo, Abimeleki ndi Fikolo wamkulu wankhondo wake anati kwa Abrahamu, “Mulungu ali nawe pa chilichonse umachita. 23 Tsopano undilumbirire ine pano pamaso pa Mulungu kuti sudzachita mwa chinyengo ndi ine kapena ana anga kapena zidzukulu zanga. Undionetse ine pamodzi ndi dziko limene ukukhalamo ngati mlendo, kukoma mtima kokhala ngati kumene ndinakuonetsa ine.”

24 Abrahamu anati, “Ine ndikulumbira.”

25 Kenaka Abrahamu anadandaula kwa Abimeleki pa za chitsime chimene antchito a Abimeleki analanda. 26 Koma Abimeleki anati, “Ine sindikudziwa amene anachita zimenezi. Iwe sunandiwuze, ndipo ndazimva lero zimenezi.”

27 Choncho Abrahamu anabweretsa nkhosa ndi ngʼombe nazipereka kwa Abimeleki, ndipo anthu awiriwo anachita pangano. 28 Abrahamu anapatulako ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri kuchoka pagulu la nkhosa zina, 29 ndipo Abimeleki anafunsa Abrahamu, “Kodi tanthauzo lake la ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri amene wawapatula pawokhawa nʼchiyani?”

30 Iye anayankha kuti, “Landirani ana ankhosa aakazi kuchokera mʼdzanja langa ngati umboni kuti ndinakumba chitsime ichi.”

31 Kotero malo amenewo anatchedwa Beeriseba, chifukwa anthu awiriwo analumbirirapo malumbiro.

32 Atatha kuchita pangano pa Beeriseba, Abimeleki ndi Fikolo mkulu wankhondo wake anabwerera ku dziko la Afilisti. 33 Abrahamu anadzala mtengo wa bwemba ku Beeriseba, ndipo anapemphera pamenepo mʼdzina la Yehova, Mulungu Wamuyaya. 34 Ndipo Abrahamu anakhala mʼdziko la Afilisti kwa nthawi yayitali.

The Birth of Isaac

21 Now the Lord was gracious to Sarah(A) as he had said, and the Lord did for Sarah what he had promised.(B) Sarah became pregnant and bore a son(C) to Abraham in his old age,(D) at the very time God had promised him.(E) Abraham gave the name Isaac[a](F) to the son Sarah bore him. When his son Isaac was eight days old, Abraham circumcised him,(G) as God commanded him. Abraham was a hundred years old(H) when his son Isaac was born to him.

Sarah said, “God has brought me laughter,(I) and everyone who hears about this will laugh with me.” And she added, “Who would have said to Abraham that Sarah would nurse children? Yet I have borne him a son in his old age.”(J)

Hagar and Ishmael Sent Away

The child grew and was weaned,(K) and on the day Isaac was weaned Abraham held a great feast. But Sarah saw that the son whom Hagar the Egyptian had borne to Abraham(L) was mocking,(M) 10 and she said to Abraham, “Get rid of that slave woman(N) and her son, for that woman’s son will never share in the inheritance with my son Isaac.”(O)

11 The matter distressed Abraham greatly because it concerned his son.(P) 12 But God said to him, “Do not be so distressed about the boy and your slave woman. Listen to whatever Sarah tells you, because it is through Isaac that your offspring[b] will be reckoned.(Q) 13 I will make the son of the slave into a nation(R) also, because he is your offspring.”

14 Early the next morning Abraham took some food and a skin of water and gave them to Hagar.(S) He set them on her shoulders and then sent her off with the boy. She went on her way and wandered in the Desert of Beersheba.(T)

15 When the water in the skin was gone, she put the boy under one of the bushes. 16 Then she went off and sat down about a bowshot away, for she thought, “I cannot watch the boy die.” And as she sat there, she[c] began to sob.(U)

17 God heard the boy crying,(V) and the angel of God(W) called to Hagar from heaven(X) and said to her, “What is the matter, Hagar? Do not be afraid;(Y) God has heard the boy crying as he lies there. 18 Lift the boy up and take him by the hand, for I will make him into a great nation.(Z)

19 Then God opened her eyes(AA) and she saw a well of water.(AB) So she went and filled the skin with water and gave the boy a drink.

20 God was with the boy(AC) as he grew up. He lived in the desert and became an archer. 21 While he was living in the Desert of Paran,(AD) his mother got a wife for him(AE) from Egypt.

The Treaty at Beersheba

22 At that time Abimelek(AF) and Phicol the commander of his forces(AG) said to Abraham, “God is with you in everything you do.(AH) 23 Now swear(AI) to me here before God that you will not deal falsely with me or my children or my descendants.(AJ) Show to me and the country where you now reside as a foreigner the same kindness I have shown to you.”(AK)

24 Abraham said, “I swear it.”

25 Then Abraham complained to Abimelek about a well of water that Abimelek’s servants had seized.(AL) 26 But Abimelek said, “I don’t know who has done this. You did not tell me, and I heard about it only today.”

27 So Abraham brought sheep and cattle and gave them to Abimelek, and the two men made a treaty.(AM) 28 Abraham set apart seven ewe lambs from the flock, 29 and Abimelek asked Abraham, “What is the meaning of these seven ewe lambs you have set apart by themselves?”

30 He replied, “Accept these seven lambs from my hand as a witness(AN) that I dug this well.(AO)

31 So that place was called Beersheba,[d](AP) because the two men swore an oath(AQ) there.

32 After the treaty(AR) had been made at Beersheba,(AS) Abimelek and Phicol the commander of his forces(AT) returned to the land of the Philistines.(AU) 33 Abraham planted a tamarisk tree(AV) in Beersheba, and there he called on the name of the Lord,(AW) the Eternal God.(AX) 34 And Abraham stayed in the land of the Philistines(AY) for a long time.

Footnotes

  1. Genesis 21:3 Isaac means he laughs.
  2. Genesis 21:12 Or seed
  3. Genesis 21:16 Hebrew; Septuagint the child
  4. Genesis 21:31 Beersheba can mean well of seven and well of the oath.