Add parallel Print Page Options

Abrahamu Amwalira

25 Abrahamu anakwatira mkazi wina dzina lake Ketura. Iyeyu anamubalira Zimurani, Yokisani, Medani, Midiyani, Isibaki ndi Suwa. Yokisani anabereka Seba ndi Dedani ndipo zidzukulu za Dedani ndiwo Aasuri, Aletusi, ndi Aleumi. Ana aamuna a Midiyani anali, Efai, Eferi, Hanoki, Abida ndi Elida. Onsewa anali zidzukulu za Ketura.

Abrahamu anasiyira Isake chilichonse anali nacho. Koma pamene anali ndi moyo, Abrahamu anapereka mphatso kwa ana aakazi ake ena onse. Kenaka anawatumiza ku dziko la kummawa kuti akhale kutali ndi mwana wake Isake.

Abrahamu anakhala ndi moyo zaka 175. Abrahamu anamwalira atakalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. Ana ake, Isake ndi Ismaeli anamuyika mʼphanga la Makipela pafupi ndi Mamre, mʼmunda umene kale unali wa Efroni mwana wa Zohari Mhiti, 10 uwu ndi munda umene Abrahamu anagula kwa Ahiti. Kumeneko Abrahamu anakayikidwa pamodzi ndi mkazi wake Sara. 11 Atamwalira Abrahamu, Mulungu anadalitsa mwana wake Isake, amene ankakhala pafupi ndi Beeri-lahai-roi (chitsime cha Wamoyo Wondipenya).

Ana Aamuna a Ismaeli

12 Nazi zidzukulu za Ismaeli, mwana wa Abrahamu amene wantchito wa Sara, Hagara Mwigupto uja, anaberekera Abrahamu.

13 Awa ndi mayina a ana a Ismaeli monga mwa mndandanda wa mabadwidwe awo: Nebayoti ndiye anali mwana woyamba wa Ismaeli; kenaka Kedara, Adibeeli, Mibisamu, 14 Misima, Duma, Masa, 15 Hadadi, Tema, Yeturi, Nafisi ndi Kedema; 16 Amenewa ndi ana a Ismaeli ndi mayina awo monga mwa midzi ndi misasa yawo. Anali olamulira mafuko khumi ndi awiri. 17 Ismaeli anakhala ndi moyo zaka 137. Iye anamwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. 18 Zidzukulu za Ismaeli zinkakhala mʼdera la pakati pa Havila ndi Suri, kummwera kwa Igupto, mukamapita cha ku Asuri. Choncho anakhala kummawa kwa abale awo.

Yakobo ndi Esau

19 Iyi ndi mbiri ya Isake mwana wa Abrahamu.

Abrahamu anabereka Isake 20 ndipo Isake anali ndi zaka makumi anayi pamene anakwatira Rebeka mwana wa Betueli Mwaramu wa ku Padanaramu mlongo wa Labani Mwaramu.

21 Isake anapempherera mkazi wake kwa Yehova popeza iye anali wosabereka. Yehova anayankha pemphero lake ndipo mkazi wake Rebeka anatenga pathupi. 22 Koma pamene anawo amalimbana mʼmimba mwake, iye anati, “Bwanji zikundichitikira zoterezi?” Choncho anapita kukafunsa kwa Yehova.

23 Yehova anati kwa iye,

“Udzabala mafuko awiri a anthu olimbana,
    ndipo magulu awiri a anthu ochokera mwa iwe adzasiyana;
fuko limodzi lidzakhala la mphamvu kuposa linzake,
    ndipo wamkulu adzatumikira wamngʼono.”

24 Pamene nthawi inakwana yakuti abeleke, Rebeka anaberekadi mapasa. 25 Woyamba kubadwa anali wofiira, ndipo thupi lake lonse linali ngati chovala cha ubweya; choncho anamutcha Esau. 26 Kenaka mʼbale wake anabadwa atagwira chidendene cha Esau; choncho anamutcha Yakobo. Isake anali ndi zaka 60 pamene Rebeka anabereka mapasawa.

27 Anyamatawo anakula ndipo Esau anakhala katswiri wosaka, munthu wamʼthengo, pamene Yakobo anali munthu wofatsa, wokonda kukhala pa nyumba. 28 Isake ankakonda Esau chifukwa cha nyama za kutchire zomwe ankakonda kudya, koma Rebeka ankakonda Yakobo.

29 Tsiku lina pamene Yakobo ankaphika chakudya, Esau anabwera kuchokera kuthengo ali wolefuka ndi njala. 30 Iye anati kwa Yakobo, “Tandipatsako phala lofiiralo, ndimwe! Ndalefuka ndi njala.” (Nʼchifukwa chake amatchedwanso Edomu).

31 Yakobo anayankha, “Choyamba undigulitse ukulu wako.”

32 Esau anati, “Chabwino, ine ndatsala pangʼono kufa, ukulu undithandiza chiyani?”

33 Koma Yakobo anati, “Lumbira kwa ine choyamba.” Kotero Esau analumbiradi, ndipo anagulitsa ukulu wake kwa Yakobo.

34 Choncho Yakobo anamupatsa Esau buledi ndi phala lofiira lija. Iye anadya ndi kumwa, nanyamuka kumapita.

Motero Esau anapeputsa ukulu wake wachisamba uja.

The Death of Abraham(A)

25 Abraham had taken another wife, whose name was Keturah. She bore him Zimran,(B) Jokshan, Medan, Midian,(C) Ishbak and Shuah.(D) Jokshan was the father of Sheba(E) and Dedan;(F) the descendants of Dedan were the Ashurites, the Letushites and the Leummites. The sons of Midian were Ephah,(G) Epher, Hanok, Abida and Eldaah. All these were descendants of Keturah.

Abraham left everything he owned to Isaac.(H) But while he was still living, he gave gifts to the sons of his concubines(I) and sent them away from his son Isaac(J) to the land of the east.(K)

Abraham lived a hundred and seventy-five years.(L) Then Abraham breathed his last and died at a good old age,(M) an old man and full of years; and he was gathered to his people.(N) His sons Isaac and Ishmael buried him(O) in the cave of Machpelah(P) near Mamre,(Q) in the field of Ephron(R) son of Zohar the Hittite,(S) 10 the field Abraham had bought from the Hittites.[a](T) There Abraham was buried with his wife Sarah. 11 After Abraham’s death, God blessed his son Isaac,(U) who then lived near Beer Lahai Roi.(V)

Ishmael’s Sons(W)

12 This is the account(X) of the family line of Abraham’s son Ishmael, whom Sarah’s slave, Hagar(Y) the Egyptian, bore to Abraham.(Z)

13 These are the names of the sons of Ishmael, listed in the order of their birth: Nebaioth(AA) the firstborn of Ishmael, Kedar,(AB) Adbeel, Mibsam, 14 Mishma, Dumah,(AC) Massa, 15 Hadad, Tema,(AD) Jetur,(AE) Naphish and Kedemah. 16 These were the sons of Ishmael, and these are the names of the twelve tribal rulers(AF) according to their settlements and camps.(AG) 17 Ishmael lived a hundred and thirty-seven years. He breathed his last and died, and he was gathered to his people.(AH) 18 His descendants(AI) settled in the area from Havilah to Shur,(AJ) near the eastern border of Egypt, as you go toward Ashur. And they lived in hostility toward[b] all the tribes related to them.(AK)

Jacob and Esau

19 This is the account(AL) of the family line of Abraham’s son Isaac.

Abraham became the father of Isaac, 20 and Isaac was forty years old(AM) when he married Rebekah(AN) daughter of Bethuel(AO) the Aramean from Paddan Aram[c](AP) and sister of Laban(AQ) the Aramean.(AR)

21 Isaac prayed to the Lord on behalf of his wife, because she was childless.(AS) The Lord answered his prayer,(AT) and his wife Rebekah became pregnant. 22 The babies jostled each other within her, and she said, “Why is this happening to me?” So she went to inquire of the Lord.(AU)

23 The Lord said to her,

“Two nations(AV) are in your womb,
    and two peoples from within you will be separated;
one people will be stronger than the other,
    and the older will serve the younger.(AW)

24 When the time came for her to give birth,(AX) there were twin boys in her womb.(AY) 25 The first to come out was red,(AZ) and his whole body was like a hairy garment;(BA) so they named him Esau.[d](BB) 26 After this, his brother came out,(BC) with his hand grasping Esau’s heel;(BD) so he was named Jacob.[e](BE) Isaac was sixty years old(BF) when Rebekah gave birth to them.

27 The boys grew up, and Esau became a skillful hunter,(BG) a man of the open country,(BH) while Jacob was content to stay at home among the tents. 28 Isaac, who had a taste for wild game,(BI) loved Esau, but Rebekah loved Jacob.(BJ)

29 Once when Jacob was cooking some stew,(BK) Esau came in from the open country,(BL) famished. 30 He said to Jacob, “Quick, let me have some of that red stew!(BM) I’m famished!” (That is why he was also called Edom.[f])(BN)

31 Jacob replied, “First sell me your birthright.(BO)

32 “Look, I am about to die,” Esau said. “What good is the birthright to me?”

33 But Jacob said, “Swear(BP) to me first.” So he swore an oath to him, selling his birthright(BQ) to Jacob.

34 Then Jacob gave Esau some bread and some lentil stew.(BR) He ate and drank, and then got up and left.

So Esau despised his birthright.

Footnotes

  1. Genesis 25:10 Or the descendants of Heth
  2. Genesis 25:18 Or lived to the east of
  3. Genesis 25:20 That is, Northwest Mesopotamia
  4. Genesis 25:25 Esau may mean hairy.
  5. Genesis 25:26 Jacob means he grasps the heel, a Hebrew idiom for he deceives.
  6. Genesis 25:30 Edom means red.