Add parallel Print Page Options

30 Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”

Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”

Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”

Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha, ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna. Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.

Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri. Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.

Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye. 10 Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna. 11 Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.

12 Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri. 13 Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.

14 Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”

15 Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.”

Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”

16 Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.

17 Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu. 18 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.

19 Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi. 20 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.

21 Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.

22 Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana. 23 Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.” 24 Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”

Nkhosa za Yakobo Zichuluka

25 Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu. 26 Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”

27 Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.” 28 Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”

29 Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira. 30 Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”

31 Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?”

Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira: 32 Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga. 33 Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”

34 Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.” 35 Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta. 36 Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.

37 Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera. 38 Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana. 39 Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho. 40 Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani. 41 Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija. 42 Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo. 43 Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.

30 When Rachel saw that she was not bearing Jacob any children,(A) she became jealous of her sister.(B) So she said to Jacob, “Give me children, or I’ll die!”

Jacob became angry with her and said, “Am I in the place of God,(C) who has kept you from having children?”(D)

Then she said, “Here is Bilhah,(E) my servant.(F) Sleep with her so that she can bear children for me and I too can build a family through her.”(G)

So she gave him her servant Bilhah as a wife.(H) Jacob slept with her,(I) and she became pregnant and bore him a son. Then Rachel said, “God has vindicated me;(J) he has listened to my plea and given me a son.”(K) Because of this she named him Dan.[a](L)

Rachel’s servant Bilhah(M) conceived again and bore Jacob a second son. Then Rachel said, “I have had a great struggle with my sister, and I have won.”(N) So she named him Naphtali.[b](O)

When Leah(P) saw that she had stopped having children,(Q) she took her servant Zilpah(R) and gave her to Jacob as a wife.(S) 10 Leah’s servant Zilpah(T) bore Jacob a son. 11 Then Leah said, “What good fortune!”[c] So she named him Gad.[d](U)

12 Leah’s servant Zilpah bore Jacob a second son. 13 Then Leah said, “How happy I am! The women will call me(V) happy.”(W) So she named him Asher.[e](X)

14 During wheat harvest,(Y) Reuben went out into the fields and found some mandrake plants,(Z) which he brought to his mother Leah. Rachel said to Leah, “Please give me some of your son’s mandrakes.”

15 But she said to her, “Wasn’t it enough(AA) that you took away my husband? Will you take my son’s mandrakes too?”

“Very well,” Rachel said, “he can sleep with you tonight in return for your son’s mandrakes.”(AB)

16 So when Jacob came in from the fields that evening, Leah went out to meet him. “You must sleep with me,” she said. “I have hired you with my son’s mandrakes.”(AC) So he slept with her that night.

17 God listened to Leah,(AD) and she became pregnant and bore Jacob a fifth son. 18 Then Leah said, “God has rewarded me for giving my servant to my husband.”(AE) So she named him Issachar.[f](AF)

19 Leah conceived again and bore Jacob a sixth son. 20 Then Leah said, “God has presented me with a precious gift. This time my husband will treat me with honor,(AG) because I have borne him six sons.” So she named him Zebulun.[g](AH)

21 Some time later she gave birth to a daughter and named her Dinah.(AI)

22 Then God remembered Rachel;(AJ) he listened to her(AK) and enabled her to conceive.(AL) 23 She became pregnant and gave birth to a son(AM) and said, “God has taken away my disgrace.”(AN) 24 She named him Joseph,[h](AO) and said, “May the Lord add to me another son.”(AP)

Jacob’s Flocks Increase

25 After Rachel gave birth to Joseph, Jacob said to Laban, “Send me on my way(AQ) so I can go back to my own homeland.(AR) 26 Give me my wives and children, for whom I have served you,(AS) and I will be on my way. You know how much work I’ve done for you.”

27 But Laban said to him, “If I have found favor in your eyes,(AT) please stay. I have learned by divination(AU) that the Lord has blessed me because of you.”(AV) 28 He added, “Name your wages,(AW) and I will pay them.”

29 Jacob said to him, “You know how I have worked for you(AX) and how your livestock has fared under my care.(AY) 30 The little you had before I came has increased greatly, and the Lord has blessed you wherever I have been.(AZ) But now, when may I do something for my own household?(BA)

31 “What shall I give you?” he asked.

“Don’t give me anything,” Jacob replied. “But if you will do this one thing for me, I will go on tending your flocks and watching over them: 32 Let me go through all your flocks today and remove from them every speckled or spotted sheep, every dark-colored lamb and every spotted or speckled goat.(BB) They will be my wages.(BC) 33 And my honesty will testify for me in the future, whenever you check on the wages you have paid me. Any goat in my possession that is not speckled or spotted, or any lamb that is not dark-colored,(BD) will be considered stolen.(BE)

34 “Agreed,” said Laban. “Let it be as you have said.” 35 That same day he removed all the male goats that were streaked or spotted, and all the speckled or spotted female goats (all that had white on them) and all the dark-colored lambs,(BF) and he placed them in the care of his sons.(BG) 36 Then he put a three-day journey(BH) between himself and Jacob, while Jacob continued to tend the rest of Laban’s flocks.

37 Jacob, however, took fresh-cut branches from poplar, almond(BI) and plane trees(BJ) and made white stripes on them by peeling the bark and exposing the white inner wood of the branches.(BK) 38 Then he placed the peeled branches(BL) in all the watering troughs,(BM) so that they would be directly in front of the flocks when they came to drink. When the flocks were in heat(BN) and came to drink, 39 they mated in front of the branches.(BO) And they bore young that were streaked or speckled or spotted.(BP) 40 Jacob set apart the young of the flock by themselves, but made the rest face the streaked and dark-colored animals(BQ) that belonged to Laban. Thus he made separate flocks for himself and did not put them with Laban’s animals. 41 Whenever the stronger females were in heat,(BR) Jacob would place the branches in the troughs in front of the animals so they would mate near the branches,(BS) 42 but if the animals were weak, he would not place them there. So the weak animals went to Laban and the strong ones to Jacob.(BT) 43 In this way the man grew exceedingly prosperous and came to own large flocks, and female and male servants, and camels and donkeys.(BU)

Footnotes

  1. Genesis 30:6 Dan here means he has vindicated.
  2. Genesis 30:8 Naphtali means my struggle.
  3. Genesis 30:11 Or “A troop is coming!”
  4. Genesis 30:11 Gad can mean good fortune or a troop.
  5. Genesis 30:13 Asher means happy.
  6. Genesis 30:18 Issachar sounds like the Hebrew for reward.
  7. Genesis 30:20 Zebulun probably means honor.
  8. Genesis 30:24 Joseph means may he add.