Add parallel Print Page Options

Yakobo Abwerera ku Beteli

35 Tsono Mulungu anati kwa Yakobo, “Nyamuka uchoke kuno kupita ku Beteli. Kumeneko ukamange guwa lansembe la Mulungu amene anadza kwa iwe pamene umathawa Esau, mʼbale wako.”

Choncho Yakobo anawuza a pa banja pake ndi onse amene anali naye kuti, “Chotsani milungu yachilendo imene muli nayo, ndipo mudziyeretse nokha ndi kusintha zovala zanu. Tiyeni tinyamuke kuchoka kuno kupita ku Beteli. Kumeneko ndikamumangira guwa lansembe Mulungu amene anandithandiza pa nthawi za masautso anga, komanso amene wakhala nane mʼmayendedwe anga onse.” Choncho anamupatsa Yakobo milungu yachilendo yonse imene anali nayo pamodzi ndi ndolo. Iye anazikwirira pansi pa mtengo wa thundu ku Sekemu. Pamenepo ananyamuka, ndipo mtima woopa Mulungu unagwera anthu onse a mʼmizinda yozungulira, kotero kuti palibe aliyense amene anatsatira banja la Yakobo.

Yakobo ndi anthu onse anali naye aja anafika ku Luzi (ku Beteli) mu dziko la Kanaani. Kumeneko anamanga guwa lansembe nalitcha Eli Beteli, chifukwa kunali kumeneko kumene Mulungu anadziwulula yekha kwa Yakobo pamene ankathawa mʼbale wake.

Debora mlezi wa Rakele anamwalira komweko nayikidwa mʼmanda pansi pa mtengo wa thundu cha kumunsi kwa Beteli. Choncho panatchedwa Aloni-Bakuti (mtengo wamaliro).

Yakobo atabwera kuchokera ku Padanaramu, Mulungu anabweranso kwa iye namudalitsa. 10 Mulungu anati kwa iye, “Dzina lako ndiwe Yakobo, koma sudzatchedwanso Yakobo; koma udzatchedwa Israeli.” Choncho anamutcha iye Israeli.

11 Ndipo Mulungu anati kwa iye, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse; berekanani ndi kuchulukana. Mtundu wa anthu, inde, mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe, ndipo ena mwa zidzukulu zako adzakhala mafumu. 12 Dziko limene ndinapereka kwa Abrahamu ndi Isake ndiliperekanso kwa iwe. Lidzakhala lako ndi la zidzukulu zako.” 13 Kenaka Mulungu anamusiya Yakobo.

14 Yakobo anayika mwala wachikumbutso pa malo pamene Mulungu anayankhula naye paja. Iye anathirapo nsembe yachakumwa ndi yamafuta. 15 Yakobo anawatcha malo amene Mulungu anayankhula naye aja kuti Beteli.

Imfa ya Isake ndi Rakele

16 Kenaka anachoka ku Beteli. Koma ali pafupi kufika ku Efurata nthawi yakuti Rakele aone mwana inakwana. Iye anavutika pobereka. 17 Akanali chivutikire choncho, mzamba anamulimbikitsa nati, “Usaope pakuti ubala mwana wina wamwamuna.” 18 Tsono pamene Rakele ankapuma wefuwefu (popeza ankamwalira) iye anatcha mwana uja kuti Beni-Oni. Koma abambo ake anamutcha kuti Benjamini.

19 Choncho Rakele anamwalira ndipo anayikidwa pa njira yopita ku Efurata (Kumeneko ndiye ku Betelehemu). 20 Pa manda ake, Yakobo anayimika mwala wachikumbutso wa pa manda ndipo ulipobe mpaka lero.

21 Israeli (Yakobo) anasunthanso nakamanga tenti yake kupitirira nsanja ya Ederi. 22 Israeli akanali mʼderali, Rubeni anapita nakagonana ndi Biliha, mdzakazi wa abambo ake. Yakobo uja anazimva zimenezi.

Yakobo anali ndi ana aamuna khumi ndi awiri:

23 Ana a Leya ndi awa:

Rubeni anali mwana woyamba wa Yakobo,

Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, ndi Zebuloni.

24 Ana a Rakele ndi awa:

Yosefe ndi Benjamini.

25 Ana a Biliha, wantchito wa Rakele ndi awa:

Dani ndi Nafutali.

26 Ana a Zilipa wantchito wa Leya ndi awa:

Gadi ndi Aseri.

Awa ndiwo ana a Yakobo amene anabadwira ku Padanaramu.

27 Yakobo anafika ku mudzi kwa abambo ake Isake ku Mamre, (kumene kunkatchedwa ku Kiriyati-Ariba kapenanso Hebroni) kumene Abrahamu ndi Isake anakhalako kale. 28 Isake anakhala ndi moyo zaka 180. 29 Anamwalira ali wokalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. Ndipo ana ake Esau ndi Yakobo anamuyika mʼmanda.

Jacob Returns to Bethel

35 Then God said to Jacob, “Go up to Bethel(A) and settle there, and build an altar(B) there to God,(C) who appeared to you(D) when you were fleeing from your brother Esau.”(E)

So Jacob said to his household(F) and to all who were with him, “Get rid of the foreign gods(G) you have with you, and purify yourselves and change your clothes.(H) Then come, let us go up to Bethel, where I will build an altar to God,(I) who answered me in the day of my distress(J) and who has been with me wherever I have gone.(K) So they gave Jacob all the foreign gods they had and the rings in their ears,(L) and Jacob buried them under the oak(M) at Shechem.(N) Then they set out, and the terror of God(O) fell on the towns all around them so that no one pursued them.(P)

Jacob and all the people with him came to Luz(Q) (that is, Bethel) in the land of Canaan.(R) There he built an altar,(S) and he called the place El Bethel,[a](T) because it was there that God revealed himself to him(U) when he was fleeing from his brother.(V)

Now Deborah, Rebekah’s nurse,(W) died and was buried under the oak(X) outside Bethel.(Y) So it was named Allon Bakuth.[b]

After Jacob returned from Paddan Aram,[c](Z) God appeared to him again and blessed him.(AA) 10 God said to him, “Your name is Jacob,[d] but you will no longer be called Jacob; your name will be Israel.[e](AB) So he named him Israel.

11 And God said to him, “I am God Almighty[f];(AC) be fruitful and increase in number.(AD) A nation(AE) and a community of nations will come from you, and kings will be among your descendants.(AF) 12 The land I gave to Abraham and Isaac I also give to you, and I will give this land to your descendants after you.(AG)(AH) 13 Then God went up from him(AI) at the place where he had talked with him.

14 Jacob set up a stone pillar(AJ) at the place where God had talked with him, and he poured out a drink offering(AK) on it; he also poured oil on it.(AL) 15 Jacob called the place where God had talked with him Bethel.[g](AM)

The Deaths of Rachel and Isaac(AN)

16 Then they moved on from Bethel. While they were still some distance from Ephrath,(AO) Rachel(AP) began to give birth and had great difficulty. 17 And as she was having great difficulty in childbirth, the midwife(AQ) said to her, “Don’t despair, for you have another son.”(AR) 18 As she breathed her last—for she was dying—she named her son Ben-Oni.[h](AS) But his father named him Benjamin.[i](AT)

19 So Rachel died and was buried on the way to Ephrath(AU) (that is, Bethlehem(AV)). 20 Over her tomb Jacob set up a pillar, and to this day(AW) that pillar marks Rachel’s tomb.(AX)

21 Israel moved on again and pitched his tent beyond Migdal Eder.(AY) 22 While Israel was living in that region, Reuben went in and slept with his father’s concubine(AZ) Bilhah,(BA) and Israel heard of it.

Jacob had twelve sons:

23 The sons of Leah:(BB)

Reuben the firstborn(BC) of Jacob,

Simeon, Levi, Judah,(BD) Issachar and Zebulun.(BE)

24 The sons of Rachel:

Joseph(BF) and Benjamin.(BG)

25 The sons of Rachel’s servant Bilhah:(BH)

Dan and Naphtali.(BI)

26 The sons of Leah’s servant Zilpah:(BJ)

Gad(BK) and Asher.(BL)

These were the sons of Jacob,(BM) who were born to him in Paddan Aram.(BN)

27 Jacob came home to his father Isaac(BO) in Mamre,(BP) near Kiriath Arba(BQ) (that is, Hebron),(BR) where Abraham and Isaac had stayed.(BS) 28 Isaac lived a hundred and eighty years.(BT) 29 Then he breathed his last and died and was gathered to his people,(BU) old and full of years.(BV) And his sons Esau and Jacob buried him.(BW)

Footnotes

  1. Genesis 35:7 El Bethel means God of Bethel.
  2. Genesis 35:8 Allon Bakuth means oak of weeping.
  3. Genesis 35:9 That is, Northwest Mesopotamia; also in verse 26
  4. Genesis 35:10 Jacob means he grasps the heel, a Hebrew idiom for he deceives.
  5. Genesis 35:10 Israel probably means he struggles with God.
  6. Genesis 35:11 Hebrew El-Shaddai
  7. Genesis 35:15 Bethel means house of God.
  8. Genesis 35:18 Ben-Oni means son of my trouble.
  9. Genesis 35:18 Benjamin means son of my right hand.