Add parallel Print Page Options

Yuda ndi Tamara

38 Pa nthawi imeneyi, Yuda anasiyana ndi abale ake napita kukakhala ndi munthu wina wa ku Adulamu wotchedwa Hira. Kumeneko, Yuda anaona mwana wamkazi wa munthu wina wa Chikanaani wotchedwa Suwa. Anamukwatira nagona naye malo amodzi. Iye anatenga pathupi, nabala mwana wamwamuna amene anamutcha Eri. Anatenganso pathupi nabala mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Onani. Anaberekanso mwana wina wamwamuna ndipo anamutcha Sela. Ameneyu anabadwa Yuda ali ku Kezibi.

Yuda anamupezera mkazi mwana wake woyamba uja Eri, ndipo dzina la mkaziyo linali Tamara. Koma ntchito zoyipa za Eri, mwana wachisamba wa Yuda zinayipira Yehova. Choncho Mulungu anamulanga ndi imfa.

Pamenepo Yuda anati kwa Onani, “Kwatira mkazi wamasiye wa mʼbale wako. Ulowe chokolo kuti mʼbale wako akhale ndi mwana.” Koma Onani anadziwa kuti mwanayo sadzakhala wake. Choncho nthawi zonse pamene amagona naye mkaziyo, ankatayira umuna pansi kuti asamuberekere mwana mʼbale wake. 10 Zimene ankachitazi zinayipira Yehova. Choncho anamulanganso ndi imfa.

11 Kenaka Yuda anati kwa mpongozi wake Tamara, “Bwererani ku nyumba ya abambo anu ndi kukhala kumeneko ngati wamasiye mpaka mwana wanga Sela atakula.” Ananena izi chifukwa ankaopa kuti Sela angafenso ngati abale ake aja. Choncho Tamara anapita kukakhala ku nyumba ya abambo ake.

12 Patapita nthawi yayitali, Batishua, mkazi wa Yuda anamwalira. Yuda atatha kulira maliro a mkazi wake, anapita, iyeyu pamodzi ndi bwenzi lake Hira, Mwadulamu uja, ku Timna kumene ankameta nkhosa zawo.

13 Tamara atamva kuti apongozi ake akupita ku Timna kukameta nkhosa, 14 iye anavula zovala zake za umasiye, nadziphimba nkhope ndi nsalu kuti asadziwike, ndipo anakhala pansi pa chipata cha ku Enaimu popita ku Timna. Tamara anachita izi chifukwa anaona kuti ngakhale Selayo anali atakula tsopano, iye sanaperekedwe kuti amulowe chokolo.

15 Yuda atamuona anangomuyesa mkazi wadama chabe, chifukwa anadziphimba nkhope. 16 Tsono anapita kwa mkaziyo pamphepete pa msewu paja nati, “Tabwera ndigone nawe.” Apa Yuda sankadziwa kuti mkazi uja anali mpongozi wake.

Ndiye mkazi uja anamufunsa Yuda nati, “Mudzandipatsa chiyani kuti ndigone nanu?”

17 Iye anati, “Ndidzakutumizira kamwana kambuzi ka mʼkhola mwanga.”

Mkaziyo anayankha kuti, “Chabwino, ndavomera, koma mungandipatse chikole mpaka mutanditumizira mbuziyo?”

18 Iye anati, “Ndikupatse chikole chanji?”

Mkaziyo anayankha, “Mundipatse mphete yanuyo, chingwe chanucho pamodzi ndi ndodo imene ili mʼdzanja lanulo.” Choncho anazipereka kwa iye nagona naye ndipo anatenga pathupi. 19 Kenaka Tamara anachoka, navula nsalu anadziphimba nayo ija, navalanso zovala zake za umasiye zija.

20 Tsono Yuda anatuma bwenzi lake Mwadulamu uja ndi kamwana kambuzi kaja kuti akapereke kwa mkazi wadama uja, ndi kuti akatero amubwezere chikole chake chija. Koma atafika sanamupezepo. 21 Anawafunsa anthu a komweko, “Kodi mkazi wadama uja amene ankakhala pambali pa msewu wa ku Enaimu, ali kuti?”

Iwo anayankha, “Sipanakhalepo mkazi wa dama aliyense pano.”

22 Choncho anabwerera kwa Yuda nati, “Sindinamupeze mkazi uja. Kuwonjeza apo, anthu a kumeneko amati, ‘Sipanakhalepo mkazi wadama pano.’ ”

23 Pamenepo Yuda anati, “Mulekeni atenge zinthuzo zikhale zake, kuopa kuti anthu angatiseke. Ine sindinalakwe, ndinamutumizira kamwana kambuzika, koma simunamupeze.”

24 Patapita miyezi itatu, Yuda anawuzidwa kuti, “Mpongozi wanu Tamara anachita zadama, ndipo zotsatira zake nʼzakuti ali ndi pathupi.”

Yuda anati, “Kamutulutseni ndipo mukamutenthe kuti afe!”

25 Akumutulutsa, iye anatuma mawu kwa apongozi ake. Anati, “Ndili ndi pathupi pa munthu amene ndi mwini wake wa zinthu izi. Taziyangʼanitsitsani, kodi mwini wa khoza, chingwe ndi ndodo yoyenderayi ndi yani?”

26 Yuda anazizindikira zinthuzo ndipo anati, “Uyu ndi wolungama kuposa ine, chifukwa sindinamupereke kwa mwana wanga Sela.” Ndipo Yuda sanagone nayenso.

27 Pamene Tamara nthawi inamukwanira yoti abeleke, mʼmimbamo munali mapasa. 28 Pamene ankabereka, mmodzi wa iwo anatulutsa dzanja lake. Choncho mzamba anatenga kawulusi kofiira nakamangirira pa mkono pa mwanayo nati, “Uyu ndiye anayamba kubadwa.” 29 Koma pamene anabweza mkonowo, mʼbale wake anabadwa ndipo mzamba anati, “Wachita kudziphotcholera wekha njira chonchi!” Ndipo anamutcha Perezi. 30 Pambuyo pake mʼbale wake amene anali ndi ulusi wofiira pa mkono wake uja anabadwa ndipo anapatsidwa dzina lakuti Zera.

Judah and Tamar

38 At that time, Judah(A) left his brothers and went down to stay with a man of Adullam(B) named Hirah.(C) There Judah met the daughter of a Canaanite man named Shua.(D) He married her and made love to her; she became pregnant and gave birth to a son, who was named Er.(E) She conceived again and gave birth to a son and named him Onan.(F) She gave birth to still another son and named him Shelah.(G) It was at Kezib that she gave birth to him.

Judah got a wife for Er, his firstborn, and her name was Tamar.(H) But Er, Judah’s firstborn, was wicked in the Lord’s sight;(I) so the Lord put him to death.(J)

Then Judah said to Onan, “Sleep with your brother’s wife and fulfill your duty to her as a brother-in-law to raise up offspring for your brother.”(K) But Onan knew that the child would not be his; so whenever he slept with his brother’s wife, he spilled his semen on the ground to keep from providing offspring for his brother. 10 What he did was wicked in the Lord’s sight; so the Lord put him to death also.(L)

11 Judah then said to his daughter-in-law(M) Tamar,(N) “Live as a widow in your father’s household(O) until my son Shelah(P) grows up.”(Q) For he thought, “He may die too, just like his brothers.” So Tamar went to live in her father’s household.

12 After a long time Judah’s wife, the daughter of Shua,(R) died. When Judah had recovered from his grief, he went up to Timnah,(S) to the men who were shearing his sheep,(T) and his friend Hirah the Adullamite(U) went with him.

13 When Tamar(V) was told, “Your father-in-law is on his way to Timnah to shear his sheep,”(W) 14 she took off her widow’s clothes,(X) covered herself with a veil(Y) to disguise herself, and then sat down(Z) at the entrance to Enaim, which is on the road to Timnah.(AA) For she saw that, though Shelah(AB) had now grown up, she had not been given to him as his wife.

15 When Judah saw her, he thought she was a prostitute,(AC) for she had covered her face. 16 Not realizing(AD) that she was his daughter-in-law,(AE) he went over to her by the roadside and said, “Come now, let me sleep with you.”(AF)

“And what will you give me to sleep with you?”(AG) she asked.

17 “I’ll send you a young goat(AH) from my flock,” he said.

“Will you give me something as a pledge(AI) until you send it?” she asked.

18 He said, “What pledge should I give you?”

“Your seal(AJ) and its cord, and the staff(AK) in your hand,” she answered. So he gave them to her and slept with her, and she became pregnant by him.(AL) 19 After she left, she took off her veil and put on her widow’s clothes(AM) again.

20 Meanwhile Judah sent the young goat by his friend the Adullamite(AN) in order to get his pledge(AO) back from the woman, but he did not find her. 21 He asked the men who lived there, “Where is the shrine prostitute(AP) who was beside the road at Enaim?”

“There hasn’t been any shrine prostitute here,” they said.

22 So he went back to Judah and said, “I didn’t find her. Besides, the men who lived there said, ‘There hasn’t been any shrine prostitute here.’”

23 Then Judah said, “Let her keep what she has,(AQ) or we will become a laughingstock.(AR) After all, I did send her this young goat, but you didn’t find her.”

24 About three months later Judah was told, “Your daughter-in-law Tamar is guilty of prostitution, and as a result she is now pregnant.”

Judah said, “Bring her out and have her burned to death!”(AS)

25 As she was being brought out, she sent a message to her father-in-law. “I am pregnant by the man who owns these,” she said. And she added, “See if you recognize whose seal and cord and staff these are.”(AT)

26 Judah recognized them and said, “She is more righteous than I,(AU) since I wouldn’t give her to my son Shelah.(AV)” And he did not sleep with her again.

27 When the time came for her to give birth, there were twin boys in her womb.(AW) 28 As she was giving birth, one of them put out his hand; so the midwife(AX) took a scarlet thread and tied it on his wrist(AY) and said, “This one came out first.” 29 But when he drew back his hand, his brother came out,(AZ) and she said, “So this is how you have broken out!” And he was named Perez.[a](BA) 30 Then his brother, who had the scarlet thread on his wrist,(BB) came out. And he was named Zerah.[b](BC)

Footnotes

  1. Genesis 38:29 Perez means breaking out.
  2. Genesis 38:30 Zerah can mean scarlet or brightness.