Add parallel Print Page Options

Yosefe ndi Mkazi wa Potifara

39 Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.

Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto. Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino. Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake. Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda. Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya.

Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola. Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”

Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga. Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?” 10 Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.

11 Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo. 12 Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.

13 Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba, 14 iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri. 15 Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”

16 Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba. 17 Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane. 18 Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”

19 Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri. 20 Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu.

Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo 21 koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe. 22 Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo. 23 Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

Joseph and Potiphar’s Wife

39 Now Joseph(A) had been taken down to Egypt. Potiphar, an Egyptian who was one of Pharaoh’s officials, the captain of the guard,(B) bought him from the Ishmaelites who had taken him there.(C)

The Lord was with Joseph(D) so that he prospered, and he lived in the house of his Egyptian master. When his master saw that the Lord was with him(E) and that the Lord gave him success in everything he did,(F) Joseph found favor in his eyes(G) and became his attendant. Potiphar put him in charge of his household,(H) and he entrusted to his care everything he owned.(I) From the time he put him in charge of his household and of all that he owned, the Lord blessed the household(J) of the Egyptian because of Joseph.(K) The blessing of the Lord was on everything Potiphar had, both in the house and in the field.(L) So Potiphar left everything he had in Joseph’s care;(M) with Joseph in charge, he did not concern himself with anything except the food he ate.

Now Joseph was well-built and handsome,(N) and after a while his master’s wife took notice of Joseph and said, “Come to bed with me!”(O)

But he refused.(P) “With me in charge,” he told her, “my master does not concern himself with anything in the house; everything he owns he has entrusted to my care.(Q) No one is greater in this house than I am.(R) My master has withheld nothing from me except you, because you are his wife. How then could I do such a wicked thing and sin against God?”(S) 10 And though she spoke to Joseph day after day, he refused(T) to go to bed with her or even be with her.

11 One day he went into the house to attend to his duties,(U) and none of the household servants(V) was inside. 12 She caught him by his cloak(W) and said, “Come to bed with me!”(X) But he left his cloak in her hand and ran out of the house.(Y)

13 When she saw that he had left his cloak in her hand and had run out of the house, 14 she called her household servants.(Z) “Look,” she said to them, “this Hebrew(AA) has been brought to us to make sport of us!(AB) He came in here to sleep with me, but I screamed.(AC) 15 When he heard me scream for help, he left his cloak beside me and ran out of the house.”(AD)

16 She kept his cloak beside her until his master came home. 17 Then she told him this story:(AE) “That Hebrew(AF) slave(AG) you brought us came to me to make sport of me. 18 But as soon as I screamed for help, he left his cloak beside me and ran out of the house.”

19 When his master heard the story his wife told him, saying, “This is how your slave treated me,” he burned with anger.(AH) 20 Joseph’s master took him and put him in prison,(AI) the place where the king’s prisoners were confined.

But while Joseph was there in the prison, 21 the Lord was with him;(AJ) he showed him kindness(AK) and granted him favor in the eyes of the prison warden.(AL) 22 So the warden put Joseph in charge of all those held in the prison, and he was made responsible for all that was done there.(AM) 23 The warden paid no attention to anything under Joseph’s(AN) care, because the Lord was with Joseph and gave him success in whatever he did.(AO)