Add parallel Print Page Options

Yosefe ndi Mkazi wa Potifara

39 Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.

Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto. Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino. Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake. Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda. Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya.

Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola. Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”

Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga. Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?” 10 Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.

11 Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo. 12 Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.

13 Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba, 14 iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri. 15 Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”

16 Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba. 17 Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane. 18 Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”

19 Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri. 20 Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu.

Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo 21 koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe. 22 Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo. 23 Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

Joseph and Potiphar’s Wife

39 Now Joseph(A) had been taken down to Egypt. Potiphar, an Egyptian who was one of Pharaoh’s officials, the captain of the guard,(B) bought him from the Ishmaelites who had taken him there.(C)

The Lord was with Joseph(D) so that he prospered, and he lived in the house of his Egyptian master. When his master saw that the Lord was with him(E) and that the Lord gave him success in everything he did,(F) Joseph found favor in his eyes(G) and became his attendant. Potiphar put him in charge of his household,(H) and he entrusted to his care everything he owned.(I) From the time he put him in charge of his household and of all that he owned, the Lord blessed the household(J) of the Egyptian because of Joseph.(K) The blessing of the Lord was on everything Potiphar had, both in the house and in the field.(L) So Potiphar left everything he had in Joseph’s care;(M) with Joseph in charge, he did not concern himself with anything except the food he ate.

Now Joseph was well-built and handsome,(N) and after a while his master’s wife took notice of Joseph and said, “Come to bed with me!”(O)

But he refused.(P) “With me in charge,” he told her, “my master does not concern himself with anything in the house; everything he owns he has entrusted to my care.(Q) No one is greater in this house than I am.(R) My master has withheld nothing from me except you, because you are his wife. How then could I do such a wicked thing and sin against God?”(S) 10 And though she spoke to Joseph day after day, he refused(T) to go to bed with her or even be with her.

11 One day he went into the house to attend to his duties,(U) and none of the household servants(V) was inside. 12 She caught him by his cloak(W) and said, “Come to bed with me!”(X) But he left his cloak in her hand and ran out of the house.(Y)

13 When she saw that he had left his cloak in her hand and had run out of the house, 14 she called her household servants.(Z) “Look,” she said to them, “this Hebrew(AA) has been brought to us to make sport of us!(AB) He came in here to sleep with me, but I screamed.(AC) 15 When he heard me scream for help, he left his cloak beside me and ran out of the house.”(AD)

16 She kept his cloak beside her until his master came home. 17 Then she told him this story:(AE) “That Hebrew(AF) slave(AG) you brought us came to me to make sport of me. 18 But as soon as I screamed for help, he left his cloak beside me and ran out of the house.”

19 When his master heard the story his wife told him, saying, “This is how your slave treated me,” he burned with anger.(AH) 20 Joseph’s master took him and put him in prison,(AI) the place where the king’s prisoners were confined.

But while Joseph was there in the prison, 21 the Lord was with him;(AJ) he showed him kindness(AK) and granted him favor in the eyes of the prison warden.(AL) 22 So the warden put Joseph in charge of all those held in the prison, and he was made responsible for all that was done there.(AM) 23 The warden paid no attention to anything under Joseph’s(AN) care, because the Lord was with Joseph and gave him success in whatever he did.(AO)

39 And Joseph was brought down to Egypt; and Potiphar, an officer of Pharaoh, captain of the guard, an Egyptian, bought him of the hands of the Ishmeelites, which had brought him down thither.

And the Lord was with Joseph, and he was a prosperous man; and he was in the house of his master the Egyptian.

And his master saw that the Lord was with him, and that the Lord made all that he did to prosper in his hand.

And Joseph found grace in his sight, and he served him: and he made him overseer over his house, and all that he had he put into his hand.

And it came to pass from the time that he had made him overseer in his house, and over all that he had, that the Lord blessed the Egyptian's house for Joseph's sake; and the blessing of the Lord was upon all that he had in the house, and in the field.

And he left all that he had in Joseph's hand; and he knew not ought he had, save the bread which he did eat. And Joseph was a goodly person, and well favoured.

And it came to pass after these things, that his master's wife cast her eyes upon Joseph; and she said, Lie with me.

But he refused, and said unto his master's wife, Behold, my master wotteth not what is with me in the house, and he hath committed all that he hath to my hand;

There is none greater in this house than I; neither hath he kept back any thing from me but thee, because thou art his wife: how then can I do this great wickedness, and sin against God?

10 And it came to pass, as she spake to Joseph day by day, that he hearkened not unto her, to lie by her, or to be with her.

11 And it came to pass about this time, that Joseph went into the house to do his business; and there was none of the men of the house there within.

12 And she caught him by his garment, saying, Lie with me: and he left his garment in her hand, and fled, and got him out.

13 And it came to pass, when she saw that he had left his garment in her hand, and was fled forth,

14 That she called unto the men of her house, and spake unto them, saying, See, he hath brought in an Hebrew unto us to mock us; he came in unto me to lie with me, and I cried with a loud voice:

15 And it came to pass, when he heard that I lifted up my voice and cried, that he left his garment with me, and fled, and got him out.

16 And she laid up his garment by her, until his lord came home.

17 And she spake unto him according to these words, saying, The Hebrew servant, which thou hast brought unto us, came in unto me to mock me:

18 And it came to pass, as I lifted up my voice and cried, that he left his garment with me, and fled out.

19 And it came to pass, when his master heard the words of his wife, which she spake unto him, saying, After this manner did thy servant to me; that his wrath was kindled.

20 And Joseph's master took him, and put him into the prison, a place where the king's prisoners were bound: and he was there in the prison.

21 But the Lord was with Joseph, and shewed him mercy, and gave him favour in the sight of the keeper of the prison.

22 And the keeper of the prison committed to Joseph's hand all the prisoners that were in the prison; and whatsoever they did there, he was the doer of it.

23 The keeper of the prison looked not to any thing that was under his hand; because the Lord was with him, and that which he did, the Lord made it to prosper.