Add parallel Print Page Options

Manase ndi Efereimu

48 Patapita kanthawi Yosefe anawuzidwa kuti, “Abambo ako akudwala.” Choncho anatenga ana ake awiri aja Manase ndi Efereimu ndi kupita nawo kwa Yakobo. Yakobo atawuzidwa kuti, “Mwana wanu Yosefe wabwera,” Israeli anadzilimbitsa nadzuka kukhala tsonga pa bedi pake.

Yakobo anati kwa Yosefe, “Mulungu Wamphamvuzonse anandionekera ku Luzi mʼdziko la Kanaani, ndipo anandidalitsa, nati kwa ine, ‘Ndidzakupatsa ana ambiri ndipo zidzukulu zako zidzasanduka mitundu yambiri ya anthu. Ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako zobwera pambuyo pako kuti likhale lawo mpaka muyaya.’

“Tsopano ana ako aamuna awiri amene anabadwa ine ndisanabwere kuno adzakhala ana anga. Efereimu ndi Manase adzakhala anga monga mmene alili Rubeni ndi Simeoni. Koma amene ati adzabadwe pambuyo pa iwowa adzakhala ako ndipo cholowa chawo chidzadziwika ndi mayina a abale awo. Pamene ndimabwerera kuchoka ku Parani, mwachisoni Rakele, amayi ako anamwalira mʼdziko la Kanaani, tikanali mʼnjira, mtunda wokafika ku Efurata ukanalipo. Ndipo ndinawayika kumeneko mʼmphepete mwa msewu wa ku Efurata” (amene ndi Betelehemu).

Israeli ataona ana a Yosefe anafunsa kuti, “Anyamatawa ndi a yani?”

Yosefe anati kwa abambo ake, “Awa ndi ana anga amene Mulungu wandipatsa kuno.”

Ndipo Israeli anati, “Bwera nawo kuno kuti ndiwadalitse.”

10 Koma maso a Israeli anali ofowoka chifukwa cha kukalamba moti sankaona nʼkomwe. Tsono Yosefe anabwera nawo ana ake aja pafupi ndi abambo ake ndipo abambo ake anawapsompsona nawakumbatira.

11 Israeli anati kwa Yosefe, “Ine sindinali kuyembekeza kuti nʼkudzaonanso nkhope yako, ndipo tsopano Mulungu wandilola kuti ndionenso ngakhale ana ako.”

12 Tsono Yosefe anawachotsa ana aja pa mawondo a Israeli ndipo anamuweramira nkhope pansi. 13 Yosefe anawagwira ana onse awiri padzanja, Efereimu ku dzanja lake lamanja kulunjika dzanja lamanzere la Israeli ndipo Manase ku dzanja lamanzere kulunjikitsa dzanja lamanja la Israeli, ndipo anawayandikiza kwa Yakobo. 14 Koma Israeli anapinganitsa mikono motero kuti anayika dzanja lake lamanja pamutu pa Efereimu ngakhale kuti iyeyo anali wamngʼono ndi dzanja lake lakumanzere analisanjika pamutu pa Manase ngakhale kuti iyeyu ndiye anali mwana woyamba.

15 Kenaka anadalitsa Yosefe nati,

“Mulungu amene makolo anga
    Abrahamu ndi Isake anamutumikira,
Mulungu amene wakhala ali mʼbusa wanga
    moyo wanga wonse kufikira lero,
16 mngelo amene wandipulumutsa ine ku zovuta zonse,
    ameneyo adalitse anyamata awa.
Kudzera mwa iwowa
    dzina langa ndi mayina a makolo anga, Abrahamu ndi Isake, adzamveka.
Iwowa adzakhala ndi ana ambiri nadzasanduka mtundu waukulu
    pa dziko lapansi.”

17 Yosefe ataona kuti abambo ake ayika dzanja lamanja pa Efereimu, sanakondwere. Choncho anagwira dzanja la abambo ake kuti alichotse pamutu pa Efereimu ndi kuliyika pamutu pa Manase, 18 nati kwa abambo ake, “Ayi, abambo anga, uyu ndiye woyamba kubadwa, ikani dzanja lanu lamanja pamutu pake.”

19 Koma abambo ake anakana nati, “Ndikudziwa, mwana wanga, ndikudziwa. Adzukulu a iyeyunso adzakhala mtundu waukulu. Komabe mʼbale wake wamngʼonoyu adzakhala wamkulu kuposa iye, ndipo zidzukulu zake zidzakhala mitundu yayikulu ya anthu.” 20 Tsono iye anawadalitsa tsiku limenelo nati,

“Aisraeli adzagwiritsa ntchito dzina lanu podalitsa nadzati:
    Mulungu akudalitseni monga Efereimu ndi Manase.”

Choncho anayika Efereimu patsogolo pa Manase.

21 Kenaka Israeli anati kwa Yosefe, “Ine ndatsala pangʼono kufa, koma Mulungu adzakhala ndipo adzakutenganinso kubwerera nanu ku dziko la makolo anu. 22 Ndiponso iwe wekha ndikupatsa moposera abale ako, malo woonjezera, Sekemu, malo amene ndinalanda kwa Aamori ndi lupanga ndi uta wanga.”

Manasseh and Ephraim

48 Some time later Joseph was told, “Your father is ill.” So he took his two sons Manasseh and Ephraim(A) along with him. When Jacob was told, “Your son Joseph has come to you,” Israel(B) rallied his strength and sat up on the bed.

Jacob said to Joseph, “God Almighty[a](C) appeared to me at Luz(D) in the land of Canaan, and there he blessed me(E) and said to me, ‘I am going to make you fruitful and increase your numbers.(F) I will make you a community of peoples, and I will give this land(G) as an everlasting possession to your descendants after you.’(H)

“Now then, your two sons born to you in Egypt(I) before I came to you here will be reckoned as mine; Ephraim and Manasseh will be mine,(J) just as Reuben(K) and Simeon(L) are mine. Any children born to you after them will be yours; in the territory they inherit they will be reckoned under the names of their brothers. As I was returning from Paddan,[b](M) to my sorrow(N) Rachel died in the land of Canaan while we were still on the way, a little distance from Ephrath. So I buried her there beside the road to Ephrath” (that is, Bethlehem).(O)

When Israel(P) saw the sons of Joseph,(Q) he asked, “Who are these?”

“They are the sons God has given me here,”(R) Joseph said to his father.

Then Israel said, “Bring them to me so I may bless(S) them.”

10 Now Israel’s eyes were failing because of old age, and he could hardly see.(T) So Joseph brought his sons close to him, and his father kissed them(U) and embraced them.(V)

11 Israel(W) said to Joseph, “I never expected to see your face again,(X) and now God has allowed me to see your children too.”(Y)

12 Then Joseph removed them from Israel’s knees(Z) and bowed down with his face to the ground.(AA) 13 And Joseph took both of them, Ephraim on his right toward Israel’s left hand and Manasseh on his left toward Israel’s right hand,(AB) and brought them close to him. 14 But Israel(AC) reached out his right hand and put it on Ephraim’s head,(AD) though he was the younger,(AE) and crossing his arms, he put his left hand on Manasseh’s head, even though Manasseh was the firstborn.(AF)

15 Then he blessed(AG) Joseph and said,

“May the God before whom my fathers
    Abraham and Isaac walked faithfully,(AH)
the God who has been my shepherd(AI)
    all my life to this day,
16 the Angel(AJ) who has delivered me from all harm(AK)
    —may he bless(AL) these boys.(AM)
May they be called by my name
    and the names of my fathers Abraham and Isaac,(AN)
and may they increase greatly
    on the earth.”(AO)

17 When Joseph saw his father placing his right hand(AP) on Ephraim’s head(AQ) he was displeased; so he took hold of his father’s hand to move it from Ephraim’s head to Manasseh’s head. 18 Joseph said to him, “No, my father, this one is the firstborn; put your right hand on his head.”(AR)

19 But his father refused and said, “I know, my son, I know. He too will become a people, and he too will become great.(AS) Nevertheless, his younger brother will be greater than he,(AT) and his descendants will become a group of nations.(AU) 20 He blessed(AV) them that day(AW) and said,

“In your[c] name will Israel(AX) pronounce this blessing:(AY)
    ‘May God make you like Ephraim(AZ) and Manasseh.(BA)’”

So he put Ephraim ahead of Manasseh.

21 Then Israel said to Joseph, “I am about to die, but God will be with you[d](BB) and take you[e] back to the land of your[f] fathers.(BC) 22 And to you I give one more ridge of land[g](BD) than to your brothers,(BE) the ridge I took from the Amorites with my sword(BF) and my bow.”

Footnotes

  1. Genesis 48:3 Hebrew El-Shaddai
  2. Genesis 48:7 That is, Northwest Mesopotamia
  3. Genesis 48:20 The Hebrew is singular.
  4. Genesis 48:21 The Hebrew is plural.
  5. Genesis 48:21 The Hebrew is plural.
  6. Genesis 48:21 The Hebrew is plural.
  7. Genesis 48:22 The Hebrew for ridge of land is identical with the place name Shechem.