Add parallel Print Page Options

Yakobo Adalitsa Ana ake Aamuna

49 Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.

“Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo;
    mverani abambo anu Israeli.

“Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa;
    mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga,
    wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana,
    iwe unagona pa bedi la abambo ako,
    ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.

“Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo,
    anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri,
    kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo,
pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo
    ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi
    ndi ukali wawo wankhanza choterewu!
Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo
    ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.

“Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda;
    dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako;
    abale ako adzakugwadira iwe.
Yuda ali ngati mwana wa mkango;
    umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga.
Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi,
    ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
10 Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda,
    udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse,
mpaka mwini wake weniweni atabwera
    ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
11 Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa,
    ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino.
Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo;
    ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
12 Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo,
    mano ake woyera chifukwa cha mkaka.

13 “Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja;
    adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi;
    malire ake adzafika ku Sidoni.

14 “Isakara ali ngati bulu wamphamvu
    wogona pansi pakati pa makola.
15 Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira
    ndi kukongola kwa dziko lake,
iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake
    ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.

16 “Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake
    monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
17 Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu,
    songo yokhala mʼnjira
imene imaluma chidendene cha kavalo
    kuti wokwerapoyo agwe chagada.

18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.

19 “Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo,
    koma iye adzawathamangitsa.

20 “Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma,
    ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.

21 “Nafutali ali ngati mbawala yayikazi
    yokhala ndi ana okongola kwambiri.

22 “Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso,
    mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe,
    nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
23 Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza;
    anamuthamangitsa ndi mauta awo.
24 Koma uta wake sunagwedezeke,
    ndi manja ake amphamvu aja analimbika,
chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo,
    chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
25 Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza;
    chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa
ndi mvula yochokera kumwamba,
    ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka,
    ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
26 Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa
    madalitso a mapiri akale
    oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona.
Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe,
    pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.

27 “Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa;
    umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha,
    ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”

28 Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.

Kumwalira kwa Yakobo

29 Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti. 30 Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda. 31 Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya. 32 Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”

33 Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.

Jacob Blesses His Sons(A)

49 Then Jacob called for his sons and said: “Gather around so I can tell you what will happen to you in days to come.(B)

“Assemble(C) and listen, sons of Jacob;
    listen to your father Israel.(D)

“Reuben, you are my firstborn,(E)
    my might, the first sign of my strength,(F)
    excelling in honor,(G) excelling in power.
Turbulent as the waters,(H) you will no longer excel,
    for you went up onto your father’s bed,
    onto my couch and defiled it.(I)

“Simeon(J) and Levi(K) are brothers—
    their swords[a] are weapons of violence.(L)
Let me not enter their council,
    let me not join their assembly,(M)
for they have killed men in their anger(N)
    and hamstrung(O) oxen as they pleased.
Cursed be their anger, so fierce,
    and their fury,(P) so cruel!(Q)
I will scatter them in Jacob
    and disperse them in Israel.(R)

“Judah,[b](S) your brothers will praise you;
    your hand will be on the neck(T) of your enemies;
    your father’s sons will bow down to you.(U)
You are a lion’s(V) cub,(W) Judah;(X)
    you return from the prey,(Y) my son.
Like a lion he crouches and lies down,
    like a lioness—who dares to rouse him?
10 The scepter will not depart from Judah,(Z)
    nor the ruler’s staff from between his feet,[c]
until he to whom it belongs[d] shall come(AA)
    and the obedience of the nations shall be his.(AB)
11 He will tether his donkey(AC) to a vine,
    his colt to the choicest branch;(AD)
he will wash his garments in wine,
    his robes in the blood of grapes.(AE)
12 His eyes will be darker than wine,
    his teeth whiter than milk.[e](AF)

13 “Zebulun(AG) will live by the seashore
    and become a haven for ships;
    his border will extend toward Sidon.(AH)

14 “Issachar(AI) is a rawboned[f] donkey
    lying down among the sheep pens.[g](AJ)
15 When he sees how good is his resting place
    and how pleasant is his land,(AK)
he will bend his shoulder to the burden(AL)
    and submit to forced labor.(AM)

16 “Dan[h](AN) will provide justice for his people
    as one of the tribes of Israel.(AO)
17 Dan(AP) will be a snake by the roadside,
    a viper along the path,(AQ)
that bites the horse’s heels(AR)
    so that its rider tumbles backward.

18 “I look for your deliverance,(AS) Lord.(AT)

19 “Gad[i](AU) will be attacked by a band of raiders,
    but he will attack them at their heels.(AV)

20 “Asher’s(AW) food will be rich;(AX)
    he will provide delicacies fit for a king.(AY)

21 “Naphtali(AZ) is a doe set free
    that bears beautiful fawns.[j](BA)

22 “Joseph(BB) is a fruitful vine,(BC)
    a fruitful vine near a spring,
    whose branches(BD) climb over a wall.[k]
23 With bitterness archers attacked him;(BE)
    they shot at him with hostility.(BF)
24 But his bow remained steady,(BG)
    his strong arms(BH) stayed[l] limber,
because of the hand of the Mighty One of Jacob,(BI)
    because of the Shepherd,(BJ) the Rock of Israel,(BK)
25 because of your father’s God,(BL) who helps(BM) you,
    because of the Almighty,[m](BN) who blesses you
with blessings of the skies above,
    blessings of the deep springs below,(BO)
    blessings of the breast(BP) and womb.(BQ)
26 Your father’s blessings are greater
    than the blessings of the ancient mountains,
    than[n] the bounty of the age-old hills.(BR)
Let all these rest on the head of Joseph,(BS)
    on the brow of the prince among[o] his brothers.(BT)

27 “Benjamin(BU) is a ravenous wolf;(BV)
    in the morning he devours the prey,(BW)
    in the evening he divides the plunder.”(BX)

28 All these are the twelve tribes of Israel,(BY) and this is what their father said to them when he blessed them, giving each the blessing(BZ) appropriate to him.

The Death of Jacob

29 Then he gave them these instructions:(CA) “I am about to be gathered to my people.(CB) Bury me with my fathers(CC) in the cave in the field of Ephron the Hittite,(CD) 30 the cave in the field of Machpelah,(CE) near Mamre(CF) in Canaan, which Abraham bought along with the field(CG) as a burial place(CH) from Ephron the Hittite. 31 There Abraham(CI) and his wife Sarah(CJ) were buried, there Isaac and his wife Rebekah(CK) were buried, and there I buried Leah.(CL) 32 The field and the cave in it were bought from the Hittites.[p](CM)

33 When Jacob had finished giving instructions to his sons, he drew his feet up into the bed, breathed his last and was gathered to his people.(CN)

Footnotes

  1. Genesis 49:5 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  2. Genesis 49:8 Judah sounds like and may be derived from the Hebrew for praise.
  3. Genesis 49:10 Or from his descendants
  4. Genesis 49:10 Or to whom tribute belongs; the meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.
  5. Genesis 49:12 Or will be dull from wine, / his teeth white from milk
  6. Genesis 49:14 Or strong
  7. Genesis 49:14 Or the campfires; or the saddlebags
  8. Genesis 49:16 Dan here means he provides justice.
  9. Genesis 49:19 Gad sounds like the Hebrew for attack and also for band of raiders.
  10. Genesis 49:21 Or free; / he utters beautiful words
  11. Genesis 49:22 Or Joseph is a wild colt, / a wild colt near a spring, / a wild donkey on a terraced hill
  12. Genesis 49:24 Or archers will attack … will shoot … will remain … will stay
  13. Genesis 49:25 Hebrew Shaddai
  14. Genesis 49:26 Or of my progenitors, / as great as
  15. Genesis 49:26 Or of the one separated from
  16. Genesis 49:32 Or the descendants of Heth