Add parallel Print Page Options

Pangano la Mulungu ndi Nowa

Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi. Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire. Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.

“Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda. Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.

“Aliyense wopha munthu,
    adzaphedwanso ndi munthu;
pakuti Mulungu analenga munthu
    mʼchifanizo chake.

Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”

Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti, “Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo, 10 pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe. 11 Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”

12 Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo. 13 Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi. 14 Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka, 15 ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi. 16 Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”

17 Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”

Ana Aamuna a Nowa

18 Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani. 19 Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.

20 Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa. 21 Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche. 22 Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja. 23 Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.

24 Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira, 25 anati,

“Atembereredwe Kanaani!
    Adzakhala kapolo
    wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”

26 Anatinso,

“Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu!
    Kanaani akhale kapolo wa Semu.
27 Mulungu akulitse dziko la Yafeti;
    Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu,
    ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”

28 Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350. 29 Anamwalira ali ndi zaka 950.

God’s Covenant With Noah

Then God blessed Noah and his sons, saying to them, “Be fruitful and increase in number and fill the earth.(A) The fear and dread of you will fall on all the beasts of the earth, and on all the birds in the sky, on every creature that moves along the ground, and on all the fish in the sea; they are given into your hands.(B) Everything that lives and moves about will be food for you.(C) Just as I gave you the green plants, I now give you everything.(D)

“But you must not eat meat that has its lifeblood still in it.(E) And for your lifeblood I will surely demand an accounting.(F) I will demand an accounting from every animal.(G) And from each human being, too, I will demand an accounting for the life of another human being.(H)

“Whoever sheds human blood,
    by humans shall their blood be shed;(I)
for in the image of God(J)
    has God made mankind.

As for you, be fruitful and increase in number; multiply on the earth and increase upon it.”(K)

Then God said to Noah and to his sons with him: “I now establish my covenant with you(L) and with your descendants after you 10 and with every living creature that was with you—the birds, the livestock and all the wild animals, all those that came out of the ark with you—every living creature on earth. 11 I establish my covenant(M) with you:(N) Never again will all life be destroyed by the waters of a flood; never again will there be a flood to destroy the earth.(O)

12 And God said, “This is the sign of the covenant(P) I am making between me and you and every living creature with you, a covenant for all generations to come:(Q) 13 I have set my rainbow(R) in the clouds, and it will be the sign of the covenant between me and the earth. 14 Whenever I bring clouds over the earth and the rainbow(S) appears in the clouds, 15 I will remember my covenant(T) between me and you and all living creatures of every kind. Never again will the waters become a flood to destroy all life.(U) 16 Whenever the rainbow(V) appears in the clouds, I will see it and remember the everlasting covenant(W) between God and all living creatures of every kind on the earth.”

17 So God said to Noah, “This is the sign of the covenant(X) I have established between me and all life on the earth.”

The Sons of Noah

18 The sons of Noah who came out of the ark were Shem, Ham and Japheth.(Y) (Ham was the father of Canaan.)(Z) 19 These were the three sons of Noah,(AA) and from them came the people who were scattered over the whole earth.(AB)

20 Noah, a man of the soil, proceeded[a] to plant a vineyard. 21 When he drank some of its wine,(AC) he became drunk and lay uncovered inside his tent. 22 Ham, the father of Canaan, saw his father naked(AD) and told his two brothers outside. 23 But Shem and Japheth took a garment and laid it across their shoulders; then they walked in backward and covered their father’s naked body. Their faces were turned the other way so that they would not see their father naked.

24 When Noah awoke from his wine and found out what his youngest son had done to him, 25 he said,

“Cursed(AE) be Canaan!(AF)
    The lowest of slaves
    will he be to his brothers.(AG)

26 He also said,

“Praise be to the Lord, the God of Shem!(AH)
    May Canaan be the slave(AI) of Shem.
27 May God extend Japheth’s[b] territory;(AJ)
    may Japheth live in the tents of Shem,(AK)
    and may Canaan be the slave of Japheth.”

28 After the flood Noah lived 350 years. 29 Noah lived a total of 950 years, and then he died.(AL)

Footnotes

  1. Genesis 9:20 Or soil, was the first
  2. Genesis 9:27 Japheth sounds like the Hebrew for extend.