Add parallel Print Page Options

12 Efereimu amadya mpweya;
    tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa
    ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa.
Amachita mgwirizano ndi Asiriya
    ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
Yehova akuyimba mlandu Yuda;
    Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake,
    adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake;
    iye atakula analimbana ndi Mulungu.
Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana;
    analira napempha kuti amukomere mtima.
Mulungu anakumana naye ku Beteli
    ndipo anayankhula naye kumeneko,
Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,
    Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu;
    pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama,
    ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.

Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo;
    iyeyo amakonda kubera anthu.
Efereimu amadzitama ponena kuti,
    “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri.
Palibe amene angandiloze chala
    chifukwa cha kulemera kwanga.”

“Ine ndine Yehova Mulungu wako
    amene ndinakutulutsa mu Igupto.
Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti,
    monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
10 Ndinayankhula ndi aneneri,
    ndinawaonetsa masomphenya ambiri,
    ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”

11 Kodi Giliyadi ndi woyipa?
    Anthu ake ndi achabechabe!
Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala?
    Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala
    mʼmunda molimidwa.
12 Yakobo anathawira ku dziko la Aramu,
    Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi,
    ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
13 Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto;
    kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
14 Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri.
    Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa.
    Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.

12 [a]Ephraim(A) feeds on the wind;(B)
    he pursues the east wind all day
    and multiplies lies and violence.(C)
He makes a treaty with Assyria(D)
    and sends olive oil to Egypt.(E)
The Lord has a charge(F) to bring against Judah;(G)
    he will punish(H) Jacob[b] according to his ways
    and repay him according to his deeds.(I)
In the womb he grasped his brother’s heel;(J)
    as a man he struggled(K) with God.
He struggled with the angel and overcame him;
    he wept and begged for his favor.
He found him at Bethel(L)
    and talked with him there—
the Lord God Almighty,
    the Lord is his name!(M)
But you must return(N) to your God;
    maintain love and justice,(O)
    and wait for your God always.(P)

The merchant uses dishonest scales(Q)
    and loves to defraud.
Ephraim boasts,(R)
    “I am very rich; I have become wealthy.(S)
With all my wealth they will not find in me
    any iniquity or sin.”

“I have been the Lord your God
    ever since you came out of Egypt;(T)
I will make you live in tents(U) again,
    as in the days of your appointed festivals.
10 I spoke to the prophets,
    gave them many visions
    and told parables(V) through them.”(W)

11 Is Gilead wicked?(X)
    Its people are worthless!
Do they sacrifice bulls in Gilgal?(Y)
    Their altars will be like piles of stones
    on a plowed field.(Z)
12 Jacob fled to the country of Aram[c];(AA)
    Israel served to get a wife,
    and to pay for her he tended sheep.(AB)
13 The Lord used a prophet to bring Israel up from Egypt,(AC)
    by a prophet he cared for him.(AD)
14 But Ephraim has aroused his bitter anger;
    his Lord will leave on him the guilt of his bloodshed(AE)
    and will repay him for his contempt.(AF)

Footnotes

  1. Hosea 12:1 In Hebrew texts 12:1-14 is numbered 12:2-15.
  2. Hosea 12:2 Jacob means he grasps the heel, a Hebrew idiom for he takes advantage of or he deceives.
  3. Hosea 12:12 That is, Northwest Mesopotamia