Hoseya 6
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kusalapa kwa Israeli
6 “Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova.
Iye watikhadzula,
koma adzatichiritsa.
Iye wativulaza,
koma adzamanga mabala athu.
2 Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa;
pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa
kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.
3 Tiyeni timudziwe Yehova,
tiyeni tilimbike kumudziwa Iye.
Adzabwera kwa ife mosakayikira konse
ngati kutuluka kwa dzuwa;
adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe,
ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”
4 Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani?
Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda?
Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa,
ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.
5 Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga,
ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga;
chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.
6 Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe,
ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.
7 Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa,
iwo sanakhulupirike kwa Ine.
8 Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa,
okhala ndi zizindikiro za kuphana.
9 Monga momwe mbala zimadikirira anthu,
magulu a ansembe amachitanso motero;
iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu,
kupalamula milandu yochititsa manyazi.
10 Ndaona chinthu choopsa kwambiri
mʼnyumba ya Israeli.
Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere,
ndipo Israeli wadzidetsa.
11 “Kunenanso za iwe Yuda,
udzakolola chilango.
“Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”
Hosea 6
New International Version
Israel Unrepentant
6 “Come, let us return(A) to the Lord.
He has torn us to pieces(B)
but he will heal us;(C)
he has injured us
but he will bind up our wounds.(D)
2 After two days he will revive us;(E)
on the third day(F) he will restore(G) us,
that we may live in his presence.
3 Let us acknowledge the Lord;
let us press on to acknowledge him.
As surely as the sun rises,
he will appear;
he will come to us like the winter rains,(H)
like the spring rains that water the earth.(I)”
4 “What can I do with you, Ephraim?(J)
What can I do with you, Judah?
Your love is like the morning mist,
like the early dew that disappears.(K)
5 Therefore I cut you in pieces with my prophets,
I killed you with the words of my mouth(L)—
then my judgments go forth like the sun.[a](M)
6 For I desire mercy, not sacrifice,(N)
and acknowledgment(O) of God rather than burnt offerings.(P)
7 As at Adam,[b] they have broken the covenant;(Q)
they were unfaithful(R) to me there.
8 Gilead is a city of evildoers,(S)
stained with footprints of blood.
9 As marauders lie in ambush for a victim,(T)
so do bands of priests;
they murder(U) on the road to Shechem,
carrying out their wicked schemes.(V)
10 I have seen a horrible(W) thing in Israel:
There Ephraim is given to prostitution,
Israel is defiled.(X)
11 “Also for you, Judah,
a harvest(Y) is appointed.
“Whenever I would restore the fortunes(Z) of my people,
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.