Add parallel Print Page Options

Chilango cha Israeli

Iwe Israeli, usakondwere;
    monga imachitira mitundu ina.
Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako;
    umakonda malipiro a chiwerewere
    pa malo aliwonse opunthira tirigu.
Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu;
    adzasowa vinyo watsopano.
Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova.
    Efereimu adzabwerera ku Igupto
    ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova,
    kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo.
Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa;
    onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa.
Chakudya ichi chidzakhala chodya okha,
    sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.

Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika;
    pa masiku a zikondwerero za Yehova?
Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko,
    Igupto adzawasonkhanitsa,
    ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda.
Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva,
    ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
Masiku achilango akubwera,
    masiku obwezera ali pafupi.
    Israeli adziwe zimenezi.
Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri
    ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri.
Mneneri amamuyesa chitsiru,
    munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga
    ndiwo alonda a Efereimu,
koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse,
    ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
Iwo azama mu zachinyengo
    monga masiku a Gibeya.
Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo
    ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.

10 “Pamene ndinamupeza Israeli
    zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu.
Nditaona makolo anu,
    zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa.
Koma atafika ku Baala Peori,
    anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi
    ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
11 Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame.
    Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
12 Ngakhale atalera ana
    ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire.
Tsoka kwa anthuwo
    pamene Ine ndidzawafulatira!
13 Ndaona Efereimu ngati Turo,
    atadzalidwa pa nthaka ya chonde.
Koma Efereimu adzatsogolera
    ana ake kuti akaphedwe.”

14 Inu Yehova, muwapatse.
    Kodi mudzawapatsa chiyani?
Apatseni mimba yomangopita padera
    ndi mawere owuma.

15 “Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala,
    Ine ndinawada kumeneko.
Chifukwa cha machitidwe awo auchimo,
    ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga.
Sindidzawakondanso;
    atsogoleri awo onse ndi owukira.
16 Efereimu wathedwa,
    mizu yake yauma
    sakubalanso zipatso.
Ngakhale atabereka ana,
    Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”

17 Mulungu wanga adzawakana
    chifukwa sanamumvere Iye;
    adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.

Punishment for Israel

Do not rejoice, Israel;
    do not be jubilant(A) like the other nations.
For you have been unfaithful(B) to your God;
    you love the wages of a prostitute(C)
    at every threshing floor.
Threshing floors and winepresses will not feed the people;
    the new wine(D) will fail them.
They will not remain(E) in the Lord’s land;
    Ephraim will return to Egypt(F)
    and eat unclean food in Assyria.(G)
They will not pour out wine offerings(H) to the Lord,
    nor will their sacrifices please(I) him.
Such sacrifices will be to them like the bread of mourners;(J)
    all who eat them will be unclean.(K)
This food will be for themselves;
    it will not come into the temple of the Lord.(L)

What will you do(M) on the day of your appointed festivals,(N)
    on the feast days of the Lord?
Even if they escape from destruction,
    Egypt will gather them,(O)
    and Memphis(P) will bury them.(Q)
Their treasures of silver(R) will be taken over by briers,
    and thorns(S) will overrun their tents.
The days of punishment(T) are coming,
    the days of reckoning(U) are at hand.
    Let Israel know this.
Because your sins(V) are so many
    and your hostility so great,
the prophet is considered a fool,(W)
    the inspired person a maniac.(X)
The prophet, along with my God,
    is the watchman over Ephraim,[a]
yet snares(Y) await him on all his paths,
    and hostility in the house of his God.(Z)
They have sunk deep into corruption,(AA)
    as in the days of Gibeah.(AB)
God will remember(AC) their wickedness
    and punish them for their sins.(AD)

10 “When I found Israel,
    it was like finding grapes in the desert;
when I saw your ancestors,
    it was like seeing the early fruit(AE) on the fig(AF) tree.
But when they came to Baal Peor,(AG)
    they consecrated themselves to that shameful idol(AH)
    and became as vile as the thing they loved.
11 Ephraim’s glory(AI) will fly away like a bird(AJ)
    no birth, no pregnancy, no conception.(AK)
12 Even if they rear children,
    I will bereave(AL) them of every one.
Woe(AM) to them
    when I turn away from them!(AN)
13 I have seen Ephraim,(AO) like Tyre,
    planted in a pleasant place.(AP)
But Ephraim will bring out
    their children to the slayer.”(AQ)

14 Give them, Lord
    what will you give them?
Give them wombs that miscarry
    and breasts that are dry.(AR)

15 “Because of all their wickedness in Gilgal,(AS)
    I hated them there.
Because of their sinful deeds,(AT)
    I will drive them out of my house.
I will no longer love them;(AU)
    all their leaders are rebellious.(AV)
16 Ephraim(AW) is blighted,
    their root is withered,
    they yield no fruit.(AX)
Even if they bear children,
    I will slay(AY) their cherished offspring.”

17 My God will reject(AZ) them
    because they have not obeyed(BA) him;
    they will be wanderers among the nations.(BB)

Footnotes

  1. Hosea 9:8 Or The prophet is the watchman over Ephraim, / the people of my God