Add parallel Print Page Options

Zilango za Tchimo

20 Yehova anawuza Mose kuti, “Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala. Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera. Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha, Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”

“ ‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.

“ ‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu. Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.

“ ‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.

10 “ ‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.

11 “ ‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.

12 “ ‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.

13 “ ‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.

14 “ ‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.

15 “ ‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.

16 “ ‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.

17 “ ‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.

18 “ ‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.

19 “ ‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.

20 “ ‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.

21 “ ‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.

22 “ ‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni. 23 Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo. 24 Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.

25 “ ‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu. 26 Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.

27 “ ‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’ ”

Punishments for Sin

20 The Lord said to Moses, “Say to the Israelites: ‘Any Israelite or any foreigner residing in Israel who sacrifices any of his children to Molek is to be put to death.(A) The members of the community are to stone him.(B) I myself will set my face against him and will cut him off from his people;(C) for by sacrificing his children to Molek, he has defiled(D) my sanctuary(E) and profaned my holy name.(F) If the members of the community close their eyes when that man sacrifices one of his children to Molek and if they fail to put him to death,(G) I myself will set my face against him and his family and will cut them off from their people together with all who follow him in prostituting themselves to Molek.

“‘I will set my face against anyone who turns to mediums and spiritists to prostitute themselves by following them, and I will cut them off from their people.(H)

“‘Consecrate yourselves(I) and be holy,(J) because I am the Lord your God.(K) Keep my decrees(L) and follow them. I am the Lord, who makes you holy.(M)

“‘Anyone who curses their father(N) or mother(O) is to be put to death.(P) Because they have cursed their father or mother, their blood will be on their own head.(Q)

10 “‘If a man commits adultery with another man’s wife(R)—with the wife of his neighbor—both the adulterer and the adulteress are to be put to death.(S)

11 “‘If a man has sexual relations with his father’s wife, he has dishonored his father.(T) Both the man and the woman are to be put to death; their blood will be on their own heads.(U)

12 “‘If a man has sexual relations with his daughter-in-law,(V) both of them are to be put to death. What they have done is a perversion; their blood will be on their own heads.

13 “‘If a man has sexual relations with a man as one does with a woman, both of them have done what is detestable.(W) They are to be put to death; their blood will be on their own heads.

14 “‘If a man marries both a woman and her mother,(X) it is wicked. Both he and they must be burned in the fire,(Y) so that no wickedness will be among you.(Z)

15 “‘If a man has sexual relations with an animal,(AA) he is to be put to death,(AB) and you must kill the animal.

16 “‘If a woman approaches an animal to have sexual relations with it, kill both the woman and the animal. They are to be put to death; their blood will be on their own heads.

17 “‘If a man marries his sister(AC), the daughter of either his father or his mother, and they have sexual relations, it is a disgrace. They are to be publicly removed(AD) from their people. He has dishonored his sister and will be held responsible.(AE)

18 “‘If a man has sexual relations with a woman during her monthly period,(AF) he has exposed the source of her flow, and she has also uncovered it. Both of them are to be cut off from their people.(AG)

19 “‘Do not have sexual relations with the sister of either your mother or your father,(AH) for that would dishonor a close relative; both of you would be held responsible.

20 “‘If a man has sexual relations with his aunt,(AI) he has dishonored his uncle. They will be held responsible; they will die childless.(AJ)

21 “‘If a man marries his brother’s wife,(AK) it is an act of impurity; he has dishonored his brother. They will be childless.(AL)

22 “‘Keep all my decrees and laws(AM) and follow them, so that the land(AN) where I am bringing you to live may not vomit you out. 23 You must not live according to the customs of the nations(AO) I am going to drive out before you.(AP) Because they did all these things, I abhorred them.(AQ) 24 But I said to you, “You will possess their land; I will give it to you as an inheritance, a land flowing with milk and honey.”(AR) I am the Lord your God, who has set you apart from the nations.(AS)

25 “‘You must therefore make a distinction between clean and unclean animals and between unclean and clean birds.(AT) Do not defile yourselves by any animal or bird or anything that moves along the ground—those that I have set apart as unclean for you. 26 You are to be holy to me(AU) because I, the Lord, am holy,(AV) and I have set you apart from the nations(AW) to be my own.

27 “‘A man or woman who is a medium(AX) or spiritist among you must be put to death.(AY) You are to stone them;(AZ) their blood will be on their own heads.’”