Add parallel Print Page Options

22 Yehova anawuza Mose kuti, “Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.

“Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.

“Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna, kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa. Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse. Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake. Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.

“ ‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.

10 “ ‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika. 11 Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo. 12 Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo. 13 Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.

14 “ ‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho. 15 Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova 16 ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’ ”

Nsembe Zosavomerezeka

17 Yehova anawuza Mose kuti, 18 “Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, 19 ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe. 20 Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu. 21 Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe. 22 Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova. 23 Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa. 24 Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu. 25 Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’ ”

26 Yehova anawuza Mose kuti, 27 “Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova. 28 Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.

29 “Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu. 30 Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.

31 “Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova. 32 Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani 33 ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”

22 The Lord said to Moses, “Tell Aaron and his sons to treat with respect the sacred offerings(A) the Israelites consecrate to me, so they will not profane my holy name.(B) I am the Lord.(C)

“Say to them: ‘For the generations to come, if any of your descendants is ceremonially unclean and yet comes near the sacred offerings that the Israelites consecrate to the Lord,(D) that person must be cut off from my presence.(E) I am the Lord.

“‘If a descendant of Aaron has a defiling skin disease[a] or a bodily discharge,(F) he may not eat the sacred offerings until he is cleansed. He will also be unclean if he touches something defiled by a corpse(G) or by anyone who has an emission of semen, or if he touches any crawling thing(H) that makes him unclean, or any person(I) who makes him unclean, whatever the uncleanness may be. The one who touches any such thing will be unclean(J) till evening.(K) He must not eat any of the sacred offerings unless he has bathed himself with water.(L) When the sun goes down, he will be clean, and after that he may eat the sacred offerings, for they are his food.(M) He must not eat anything found dead(N) or torn by wild animals,(O) and so become unclean(P) through it. I am the Lord.(Q)

“‘The priests are to perform my service(R) in such a way that they do not become guilty(S) and die(T) for treating it with contempt. I am the Lord, who makes them holy.(U)

10 “‘No one outside a priest’s family may eat the sacred offering, nor may the guest of a priest or his hired worker eat it.(V) 11 But if a priest buys a slave with money, or if slaves are born in his household, they may eat his food.(W) 12 If a priest’s daughter marries anyone other than a priest, she may not eat any of the sacred contributions. 13 But if a priest’s daughter becomes a widow or is divorced, yet has no children, and she returns to live in her father’s household as in her youth, she may eat her father’s food. No unauthorized person, however, may eat it.

14 “‘Anyone who eats a sacred offering by mistake(X) must make restitution to the priest for the offering and add a fifth of the value(Y) to it. 15 The priests must not desecrate the sacred offerings(Z) the Israelites present to the Lord(AA) 16 by allowing them to eat(AB) the sacred offerings and so bring upon them guilt(AC) requiring payment.(AD) I am the Lord, who makes them holy.(AE)’”

Unacceptable Sacrifices

17 The Lord said to Moses, 18 “Speak to Aaron and his sons and to all the Israelites and say to them: ‘If any of you—whether an Israelite or a foreigner residing in Israel(AF)—presents a gift(AG) for a burnt offering to the Lord, either to fulfill a vow(AH) or as a freewill offering,(AI) 19 you must present a male without defect(AJ) from the cattle, sheep or goats in order that it may be accepted on your behalf.(AK) 20 Do not bring anything with a defect,(AL) because it will not be accepted on your behalf.(AM) 21 When anyone brings from the herd or flock(AN) a fellowship offering(AO) to the Lord to fulfill a special vow or as a freewill offering,(AP) it must be without defect or blemish(AQ) to be acceptable.(AR) 22 Do not offer to the Lord the blind, the injured or the maimed, or anything with warts or festering or running sores. Do not place any of these on the altar as a food offering presented to the Lord. 23 You may, however, present as a freewill offering an ox[b] or a sheep that is deformed or stunted, but it will not be accepted in fulfillment of a vow. 24 You must not offer to the Lord an animal whose testicles are bruised, crushed, torn or cut.(AS) You must not do this in your own land, 25 and you must not accept such animals from the hand of a foreigner and offer them as the food of your God.(AT) They will not be accepted on your behalf, because they are deformed and have defects.(AU)’”

26 The Lord said to Moses, 27 “When a calf, a lamb or a goat(AV) is born, it is to remain with its mother for seven days.(AW) From the eighth day(AX) on, it will be acceptable(AY) as a food offering presented to the Lord. 28 Do not slaughter a cow or a sheep and its young on the same day.(AZ)

29 “When you sacrifice a thank offering(BA) to the Lord, sacrifice it in such a way that it will be accepted on your behalf. 30 It must be eaten that same day; leave none of it till morning.(BB) I am the Lord.(BC)

31 “Keep(BD) my commands and follow them.(BE) I am the Lord. 32 Do not profane my holy name,(BF) for I must be acknowledged as holy by the Israelites.(BG) I am the Lord, who made you holy(BH) 33 and who brought you out of Egypt(BI) to be your God.(BJ) I am the Lord.”

Footnotes

  1. Leviticus 22:4 The Hebrew word for defiling skin disease, traditionally translated “leprosy,” was used for various diseases affecting the skin.
  2. Leviticus 22:23 The Hebrew word can refer to either male or female.