Add parallel Print Page Options

Nsembe Yachiyanjano

“ ‘Ngati munthu apereka nsembe ya chiyanjano kwa Yehova, ndipo choperekacho nʼkukhala ngʼombe yayimuna kapena yayikazi, ikhale yopanda chilema. Munthuyo asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo, ndipo ayiphere pa khomo la tenti ya msonkhano. Ndipo ansembe, ana a Aaroni, awaze magazi mbali zonse za guwalo. Pa nsembe yachiyanjanopo, ayenera kupatula zamʼkati mwa nyamayo ndi mafuta onse amene amakuta zamʼkati kupereka nsembe ya chakudya kwa Yehova. Apatulenso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake omwe ndiponso mafuta okuta chiwindi amene achotsedwa pamodzi ndi impsyo zija. Ndipo ana a Aaroni atenthe zimenezi pa guwa, pamwamba pa chopereka chopsereza chimene chili pa nkhuni zoyakazo. Imeneyi ndi nsembe yotentha pa moto, ya fungo lokomera Yehova.

“ ‘Ngati munthu apereka nsembe ya chiyanjano kwa Yehova, choperekacho chikhale nkhosa yayimuna kapena yayikazi yopanda chilema. Ngati apereka nsembe ya mwana wankhosa, abwere naye pamaso pa Yehova. Asanjike dzanja lake pamutu pa nkhosayo ndipo ayiphere pa khomo la tenti ya msonkhano. Ndipo ana a Aaroni awaze magaziwo mbali zonse za guwalo. Pa nsembe yachiyanjanopo ayenera kuchotsa ndi kubweretsa: mafuta a nkhosayo, mchira wake wonse wonona atawudulira mʼtsinde pafupi ndi fupa la msana, zamʼkati zonse ndi mafuta onse amene akuta ziwalo zamʼkatimo, 10 impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta amene akuta impsyozo, msonga ya chiwindi imene idzachotsedwere limodzi ndi impsyozo. 11 Wansembe awotche zonsezi pa guwa. Ichi ndi chakudya chotentha pa moto choperekedwa kwa Yehova.

12 “ ‘Ngati munthuyo apereka mbuzi ngati nsembe, abwere nayo kwa Yehova. 13 Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphere pa khomo la tenti ya msonkhano. Ndipo ana a Aaroni awaze magazi ake mbali zonse za guwa. 14 Tsono pa nsembe yoti iwotchedwe kukhala nsembe chakudya ya Yehova, achotse ndi kubweretsa: mafuta onse amene amaphimba zamʼkati kapena mafuta onse a mʼkatimo, 15 impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse omwe akuta impsyozo ndi msonga ya chiwindi imene adzachotsera pamodzi ndi impsyo zija. 16 Wansembe awotche zonsezi pa guwa. Ichi ndi chakudya cha Yehova, chowotcha pa moto ndiponso cha fungo lokomera Yehova. Mafuta onse ndi a Yehova.

17 “ ‘Limeneli likhale lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse kuti musadzadye mafuta kapena magazi kulikonse kumene mudzakhale.’ ”

The Fellowship Offering

“‘If your offering is a fellowship offering,(A) and you offer an animal from the herd, whether male or female, you are to present before the Lord an animal without defect.(B) You are to lay your hand on the head(C) of your offering and slaughter it(D) at the entrance to the tent of meeting.(E) Then Aaron’s sons the priests shall splash(F) the blood against the sides(G) of the altar.(H) From the fellowship offering you are to bring a food offering to the Lord: the internal organs(I) and all the fat(J) that is connected to them, both kidneys(K) with the fat on them near the loins, and the long lobe of the liver, which you will remove with the kidneys. Then Aaron’s sons(L) are to burn it on the altar(M) on top of the burnt offering(N) that is lying on the burning wood;(O) it is a food offering, an aroma pleasing to the Lord.(P)

“‘If you offer an animal from the flock as a fellowship offering(Q) to the Lord, you are to offer a male or female without defect. If you offer a lamb,(R) you are to present it before the Lord,(S) lay your hand on its head and slaughter it(T) in front of the tent of meeting. Then Aaron’s sons shall splash its blood against the sides of the altar. From the fellowship offering you are to bring a food offering(U) to the Lord: its fat, the entire fat tail cut off close to the backbone, the internal organs and all the fat that is connected to them, 10 both kidneys with the fat on them near the loins, and the long lobe of the liver, which you will remove with the kidneys. 11 The priest shall burn them on the altar(V) as a food offering(W) presented to the Lord.(X)

12 “‘If your offering is a goat,(Y) you are to present it before the Lord, 13 lay your hand on its head and slaughter it in front of the tent of meeting. Then Aaron’s sons shall splash(Z) its blood against the sides of the altar.(AA) 14 From what you offer you are to present this food offering to the Lord: the internal organs and all the fat that is connected to them, 15 both kidneys with the fat on them near the loins, and the long lobe of the liver, which you will remove with the kidneys.(AB) 16 The priest shall burn them on the altar(AC) as a food offering,(AD) a pleasing aroma.(AE) All the fat(AF) is the Lord’s.(AG)

17 “‘This is a lasting ordinance(AH) for the generations to come,(AI) wherever you live:(AJ) You must not eat any fat or any blood.(AK)’”