Add parallel Print Page Options

Petro Achiritsa Wolumala Miyendo

Tsiku lina Petro ndi Yohane ankapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera nthawi ya 3 koloko masana. Ndipo munthu wolumala chibadwire ankanyamulidwa tsiku ndi tsiku kukayikidwa pa khomo la Nyumbayo lotchedwa Khomo Lokongola kuti azikapempha amene amalowa ku bwalo la Nyumbayo. Ataona Petro ndi Yohane ali pafupi kulowa anawapempha ndalama. Iwo anamuyangʼanitsitsa iye. Kenaka Petro anati, “Tiyangʼane!” Munthuyo anawayangʼanitsitsa kuyembekezera kuti alandira kanthu kuchokera kwa iwo.

Petro anati kwa iye, “Ine ndilibe siliva kapena golide, koma chimene ndili nacho ndikupatsa. Mʼdzina la Yesu Khristu wa ku Nazareti, yenda.” Ndipo anamugwira dzanja lamanja, namuthandiza kuti ayimirire ndipo nthawi yomweyo mapazi ake ndi akakolo ake analimba. Iye analumpha ndi kuyamba kuyenda. Kenaka analowa nawo pamodzi mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, akuyenda ndi kulumpha ndiponso kuyamika Mulungu. Anthu onse atamuona akuyenda ndiponso kuyamika Mulungu, 10 anamuzindikira kuti ndi yemwe uja ankakhala pa khomo la Nyumbayo lotchedwa Khomo Lokongola, ndipo anazizwa ndi kudabwa ndi zimene zinamuchitikira.

Petro Ayankhula kwa Anthu

11 Wopempha uja akuyenda pamodzi ndi Petro ndi Yohane, anthu onse anadabwa ndipo anawathamangira iwo kumalo wotchedwa Khonde la Solomoni. 12 Petro ataona zimenezi anawawuza kuti, “Inu Aisraeli, chifukwa chiyani mukudabwa ndi zimene zachitikazi? Bwanji mukuyangʼana ife ngati kuti tamuyendetsa munthuyu ndi mphamvu yathu kapena chifukwa cha kupembedza kwathu? 13 Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, Mulungu wa makolo athu, wamulemekeza mtumiki wake Yesu. Amene inu munamukana pamaso pa Pilato ndi kumupereka Iye kuti aphedwe, ngakhale kuti Pilato anafuna kuti amumasule. 14 Koma inu munamukana Woyera ndi Wolungamayo ndipo munapempha kuti akumasulireni munthu wakupha anthu. 15 Inu munapha mwini moyo, koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Ife ndife mboni za zimenezi. 16 Mwachikhulupiriro mʼdzina la Yesu, munthu uyu amene mukumuona ndi kumudziwa analimbikitsidwa. Mʼdzina la Yesu ndi chikhulupiriro chimene chili mwa iye chamuchiritsa kwathunthu, monga nonse mukuona.

17 “Tsopano abale ine ndikudziwa kuti inu munachita zimenezi mosadziwa, monga momwenso anachitira atsogoleri anu. 18 Koma umu ndi mmene Mulungu anakwaniritsira zimene zinanenedwa kale ndi aneneri onse, kuti Khristu adzamva zowawa. 19 Chifukwa chake, lapani, bwererani kwa Mulungu, kuti machimo anu afafanizidwe, kuti nthawi ya kutsitsimuka ibwere kuchokera kwa Ambuye, 20 ndi kuti Iye atumize Yesu Khristu amene anasankhidwa chifukwa cha inu. 21 Iye ayenera kukhalabe kumwamba mpaka nthawi ya kukonzanso zinthu zonse monga Mulungu analonjeza kale kudzera mwa aneneri ake oyera mtima. 22 Pakuti Mose anati, ‘Ambuye Mulungu wanu adzakuukitsirani mneneri monga ine kuchokera pakati pa anthu anu; mumvere zonse zimene iye akuwuzeni. 23 Aliyense amene sadzamvera mawu a mneneriyo, adzayenera kuchotsedwa pakati pa abale ake.’

24 “Ndipo aneneri onse ambiri amene anayankhula kuyambira Samueli, ananeneratu za masiku ano. 25 Inu ndinu ana a aneneri ndiponso ana apangano limene Mulungu anachita ndi makolo anu. Iye anati kwa Abrahamu, ‘Anthu onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa zidzukulu zako.’ 26 Pamene Mulungu anaukitsa mtumiki wake, anamutuma Iye poyamba kwa inu kuti akudalitseni pobweza aliyense wa inu ku zoyipa zake.”

Peter Heals a Lame Beggar

One day Peter and John(A) were going up to the temple(B) at the time of prayer—at three in the afternoon.(C) Now a man who was lame from birth(D) was being carried to the temple gate(E) called Beautiful, where he was put every day to beg(F) from those going into the temple courts. When he saw Peter and John about to enter, he asked them for money. Peter looked straight at him, as did John. Then Peter said, “Look at us!” So the man gave them his attention, expecting to get something from them.

Then Peter said, “Silver or gold I do not have, but what I do have I give you. In the name of Jesus Christ of Nazareth,(G) walk.” Taking him by the right hand, he helped him up, and instantly the man’s feet and ankles became strong. He jumped to his feet and began to walk. Then he went with them into the temple courts, walking and jumping,(H) and praising God. When all the people(I) saw him walking and praising God, 10 they recognized him as the same man who used to sit begging at the temple gate called Beautiful,(J) and they were filled with wonder and amazement at what had happened to him.

Peter Speaks to the Onlookers

11 While the man held on to Peter and John,(K) all the people were astonished and came running to them in the place called Solomon’s Colonnade.(L) 12 When Peter saw this, he said to them: “Fellow Israelites, why does this surprise you? Why do you stare at us as if by our own power or godliness we had made this man walk? 13 The God of Abraham, Isaac and Jacob,(M) the God of our fathers,(N) has glorified his servant Jesus. You handed him over(O) to be killed, and you disowned him before Pilate,(P) though he had decided to let him go.(Q) 14 You disowned the Holy(R) and Righteous One(S) and asked that a murderer be released to you.(T) 15 You killed the author of life, but God raised him from the dead.(U) We are witnesses(V) of this. 16 By faith in the name of Jesus,(W) this man whom you see and know was made strong. It is Jesus’ name and the faith that comes through him that has completely healed him, as you can all see.

17 “Now, fellow Israelites,(X) I know that you acted in ignorance,(Y) as did your leaders.(Z) 18 But this is how God fulfilled(AA) what he had foretold(AB) through all the prophets,(AC) saying that his Messiah would suffer.(AD) 19 Repent, then, and turn to God, so that your sins may be wiped out,(AE) that times of refreshing may come from the Lord, 20 and that he may send the Messiah,(AF) who has been appointed for you—even Jesus. 21 Heaven must receive him(AG) until the time comes for God to restore everything,(AH) as he promised long ago through his holy prophets.(AI) 22 For Moses said, ‘The Lord your God will raise up for you a prophet like me from among your own people; you must listen to everything he tells you.(AJ) 23 Anyone who does not listen to him will be completely cut off from their people.’[a](AK)

24 “Indeed, beginning with Samuel, all the prophets(AL) who have spoken have foretold these days. 25 And you are heirs(AM) of the prophets and of the covenant(AN) God made with your fathers. He said to Abraham, ‘Through your offspring all peoples on earth will be blessed.’[b](AO) 26 When God raised up(AP) his servant, he sent him first(AQ) to you to bless you by turning each of you from your wicked ways.”

Footnotes

  1. Acts 3:23 Deut. 18:15,18,19
  2. Acts 3:25 Gen. 22:18; 26:4