Add parallel Print Page Options

Asankha Atumiki Asanu ndi Awiri

Mʼmasiku amenewo pamene chiwerengero cha ophunzira chinkachuluka, Ayuda a Chihelene pakati pawo anadandaula chifukwa cha Ayuda a Chihebri chifukwa amasiye awo samawagawira chakudya cha tsiku ndi tsiku. Tsono Atumwi khumi ndi awiriwo anasonkhanitsa ophunzira onse pamodzi ndipo anati, “Nʼkosayenera kuti ife tisiye kulalikira Mawu a Mulungu ndi kuyangʼanira za chakudya. Choncho abale, sankhani pakati panu anthu asanu ndi awiri a mbiri yabwino, odzazidwa ndi Mzimu Woyera ndi anzeru. Ife tidzawapatsa udindo oyangʼanira. Koma ife tidzadzipereka kuti tizipemphera ndi kulalikira mawu.”

Mawu amenewa anakondweretsa gulu lonse la anthu. Iwo anasankha, Stefano, munthu wodzazidwa ndi chikhulupiriro ndiponso Mzimu Woyera; anasankhanso Filipo, Prokoro, Nikanora, Timo, Parmena ndi Nikolao amene anatembenuka mtima ndi kulowa Chiyuda kuchokera kwa Antiokeya. Iwo anapereka anthuwa kwa atumwi amene anawapempherera ndi kuwasanjika manja.

Ndipo Mawu a Mulungu anapitirira kufalikira. Chiwerengero cha ophunzira mu Yerusalemu chinakula mofulumira ndipo ansembe ochuluka anakhulupirira.

Ayuda Agwira Stefano

Stefano, munthu wodzazidwa ndi chisomo cha Mulungu ndi mphamvu anachita zodabwitsa ndiponso zizindikiro zazikulu pakati pa anthu. Panauka mtsutso kuchokera kwa anthu a ku Kurene ndi a ku Alekisandriya komanso a ku dera la Silisiya ndi Asiya, otchedwa a Sunagoge ya Mfulu. Anthu amenewa anayamba kutsutsana ndi Stefano. 10 Koma iwo sanathe kumugonjetsa chifukwa iye ankayankhula ndi nzeru zimene Mzimu Woyera anamupatsa.

11 Iwo ananyengerera anthu ena mwamseri kuti anene kuti, “Ife tinamva Stefano akuchitira chipongwe Mose ndiponso Mulungu.”

12 Motero anawutsa mitima ya anthu, akulu ndi aphunzitsi amalamulo. Anamugwira Stefano ndi kumubweretsa ku Bwalo Lalikulu. 13 Iwo anabweretsa mboni zonama zimene zinati, “Munthu uyu akupitirirabe kuyankhula mawu onyoza malo oyera ndi malamulo. 14 Pakuti tinamumva akunena kuti Yesu uja wa ku Nazareti adzawononga malo ano ndiponso kusintha miyambo imene Mose anatipatsa.”

15 Onse amene anakhala pansi Mʼbwalo Lalikulu anamuyangʼanitsitsa Stefano, ndipo anaona kuti nkhope yake ikuwala ngati ya mngelo.

The Choosing of the Seven

In those days when the number of disciples was increasing,(A) the Hellenistic Jews[a](B) among them complained against the Hebraic Jews because their widows(C) were being overlooked in the daily distribution of food.(D) So the Twelve gathered all the disciples(E) together and said, “It would not be right for us to neglect the ministry of the word of God(F) in order to wait on tables. Brothers and sisters,(G) choose seven men from among you who are known to be full of the Spirit(H) and wisdom. We will turn this responsibility over to them(I) and will give our attention to prayer(J) and the ministry of the word.”

This proposal pleased the whole group. They chose Stephen,(K) a man full of faith and of the Holy Spirit;(L) also Philip,(M) Procorus, Nicanor, Timon, Parmenas, and Nicolas from Antioch, a convert to Judaism. They presented these men to the apostles, who prayed(N) and laid their hands on them.(O)

So the word of God spread.(P) The number of disciples in Jerusalem increased rapidly,(Q) and a large number of priests became obedient to the faith.

Stephen Seized

Now Stephen, a man full of God’s grace and power, performed great wonders and signs(R) among the people. Opposition arose, however, from members of the Synagogue of the Freedmen (as it was called)—Jews of Cyrene(S) and Alexandria as well as the provinces of Cilicia(T) and Asia(U)—who began to argue with Stephen. 10 But they could not stand up against the wisdom the Spirit gave him as he spoke.(V)

11 Then they secretly(W) persuaded some men to say, “We have heard Stephen speak blasphemous words against Moses and against God.”(X)

12 So they stirred up the people and the elders and the teachers of the law. They seized Stephen and brought him before the Sanhedrin.(Y) 13 They produced false witnesses,(Z) who testified, “This fellow never stops speaking against this holy place(AA) and against the law. 14 For we have heard him say that this Jesus of Nazareth will destroy this place(AB) and change the customs Moses handed down to us.”(AC)

15 All who were sitting in the Sanhedrin(AD) looked intently at Stephen, and they saw that his face was like the face of an angel.

Footnotes

  1. Acts 6:1 That is, Jews who had adopted the Greek language and culture