Maliro 4
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
4 Haa! Golide wathimbirira,
golide wosalala wasinthikiratu!
Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika
pamphambano ponse pa mzinda.
2 Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali
amene kale anali ngati golide,
tsopano ali ngati miphika ya dothi,
ntchito ya owumba mbiya!
3 Ngakhale nkhandwe zimapereka bere
kuyamwitsa ana ake,
koma anthu anga asanduka ankhanza
ngati nthiwatiwa mʼchipululu.
4 Lilime la mwana lakangamira kukhosi
chifukwa cha ludzu,
ana akupempha chakudya,
koma palibe amene akuwapatsa.
5 Iwo amene kale ankadya zonona
akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda.
Iwo amene kale ankavala zokongola
tsopano akugona pa phulusa.
6 Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu
kuposa anthu a ku Sodomu,
amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa
popanda owathandiza.
7 Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana
ndi oyera kuposa mkaka.
Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi,
maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.
8 Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye;
palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda.
Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo;
lawuma gwaa ngati nkhuni.
9 Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa
amene anafa ndi njala;
chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda
iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.
10 Amayi achifundo afika
pophika ana awo enieni,
ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu
anga anali kuwonongeka.
11 Yehova wakwaniritsa ukali wake;
wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa.
Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni
kuti uwononge maziko ake.
12 Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire,
kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse,
kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa
pa zipata za Yerusalemu.
13 Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake
ndi mphulupulu za ansembe ake,
amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.
14 Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda
ngati anthu osaona.
Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi
palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.
15 Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!”
“Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!”
Akamathawa ndi kumangoyendayenda,
pakati pa anthu a mitundu yonse amati,
“Asakhalenso ndi ife.”
16 Yehova mwini wake wawabalalitsa;
Iye sakuwalabadiranso.
Ansembe sakulandira ulemu,
akuluakulu sakuwachitira chifundo.
17 Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana,
chithandizo chosabwera nʼkomwe,
kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu
wa anthu umene sukanatipulumutsa.
18 Anthu ankalondola mapazi athu,
choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda.
Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka,
chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.
19 Otilondola akuthamanga kwambiri
kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga;
anatithamangitsa mpaka ku mapiri
ndi kutibisalira mʼchipululu.
20 Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo,
anakodwa mʼmisampha yawo.
Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake
pakati pa mitundu ya anthu.
21 Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu.
Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi.
Koma iwenso chikho chidzakupeza;
udzaledzera mpaka kukhala maliseche.
22 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha;
Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo.
Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu,
ndi kuyika poyera mphulupulu zako.
Lamentations 4
New International Version
4 [a]How the gold has lost its luster,
the fine gold become dull!
The sacred gems are scattered
at every street corner.(A)
2 How the precious children of Zion,(B)
once worth their weight in gold,
are now considered as pots of clay,
the work of a potter’s hands!
3 Even jackals offer their breasts
to nurse their young,
but my people have become heartless
like ostriches in the desert.(C)
4 Because of thirst(D) the infant’s tongue
sticks to the roof of its mouth;(E)
the children beg for bread,
but no one gives it to them.(F)
5 Those who once ate delicacies
are destitute in the streets.
Those brought up in royal purple(G)
now lie on ash heaps.(H)
6 The punishment of my people
is greater than that of Sodom,(I)
which was overthrown in a moment
without a hand turned to help her.
7 Their princes were brighter than snow
and whiter than milk,
their bodies more ruddy than rubies,
their appearance like lapis lazuli.
8 But now they are blacker(J) than soot;
they are not recognized in the streets.
Their skin has shriveled on their bones;(K)
it has become as dry as a stick.
9 Those killed by the sword are better off
than those who die of famine;(L)
racked with hunger, they waste away
for lack of food from the field.(M)
10 With their own hands compassionate women
have cooked their own children,(N)
who became their food
when my people were destroyed.
11 The Lord has given full vent to his wrath;(O)
he has poured out(P) his fierce anger.(Q)
He kindled a fire(R) in Zion
that consumed her foundations.(S)
12 The kings of the earth did not believe,
nor did any of the peoples of the world,
that enemies and foes could enter
the gates of Jerusalem.(T)
13 But it happened because of the sins of her prophets
and the iniquities of her priests,(U)
who shed within her
the blood(V) of the righteous.
14 Now they grope through the streets
as if they were blind.(W)
They are so defiled with blood(X)
that no one dares to touch their garments.
15 “Go away! You are unclean!” people cry to them.
“Away! Away! Don’t touch us!”
When they flee and wander(Y) about,
people among the nations say,
“They can stay here no longer.”(Z)
16 The Lord himself has scattered them;
he no longer watches over them.(AA)
The priests are shown no honor,
the elders(AB) no favor.(AC)
17 Moreover, our eyes failed,
looking in vain(AD) for help;(AE)
from our towers we watched
for a nation(AF) that could not save us.
18 People stalked us at every step,
so we could not walk in our streets.
Our end was near, our days were numbered,
for our end had come.(AG)
19 Our pursuers were swifter
than eagles(AH) in the sky;
they chased us(AI) over the mountains
and lay in wait for us in the desert.(AJ)
20 The Lord’s anointed,(AK) our very life breath,
was caught in their traps.(AL)
We thought that under his shadow(AM)
we would live among the nations.
Footnotes
- Lamentations 4:1 This chapter is an acrostic poem, the verses of which begin with the successive letters of the Hebrew alphabet.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.