Add parallel Print Page Options

Yohane Mʼbatizi Akonza Njira

Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu, monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya:

“Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu,
    amene adzakonza njira yanu,”
“Mawu a wofuwula mʼchipululu,
‘Konzani njira ya Ambuye,
    wongolani njira zake.’ ”

Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo. Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani. Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo. Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake. Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”

Kubatizidwa ndi Kuyesedwa kwa Yesu

Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani. 10 Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda. 11 Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”

12 Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu, 13 ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.

Yesu Alengeza za Uthenga Wabwino

14 Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati, 15 “Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”

Yesu Ayitana Ophunzira ake Oyamba

16 Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi. 17 Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.” 18 Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.

19 Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo. 20 Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.

Yesu Atulutsa Mzimu Woyipa

21 Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa. 22 Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo. 23 Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti, 24 “Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”

25 Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!” 26 Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.

27 Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.” 28 Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.

Yesu Achiritsa Anthu Ambiri

29 Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya. 30 Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye. 31 Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.

32 Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda. 33 Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo, 34 Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.

Yesu Apemphera Kumalo a Yekha

35 Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera. 36 Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye, 37 ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”

38 Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.” 39 Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.

Yesu Achiritsa Wakhate

40 Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”

41 Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!” 42 Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.

43 Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti, 44 “Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.” 45 Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.

John the Baptist Prepares the Way(A)

The beginning of the good news about Jesus the Messiah,[a] the Son of God,[b](B) as it is written in Isaiah the prophet:

“I will send my messenger ahead of you,
    who will prepare your way”[c](C)
“a voice of one calling in the wilderness,
‘Prepare the way for the Lord,
    make straight paths for him.’”[d](D)

And so John the Baptist(E) appeared in the wilderness, preaching a baptism of repentance(F) for the forgiveness of sins.(G) The whole Judean countryside and all the people of Jerusalem went out to him. Confessing their sins, they were baptized by him in the Jordan River. John wore clothing made of camel’s hair, with a leather belt around his waist,(H) and he ate locusts(I) and wild honey. And this was his message: “After me comes the one more powerful than I, the straps of whose sandals I am not worthy to stoop down and untie.(J) I baptize you with[e] water, but he will baptize you with[f] the Holy Spirit.”(K)

The Baptism and Testing of Jesus(L)(M)

At that time Jesus came from Nazareth(N) in Galilee and was baptized by John(O) in the Jordan. 10 Just as Jesus was coming up out of the water, he saw heaven being torn open and the Spirit descending on him like a dove.(P) 11 And a voice came from heaven: “You are my Son,(Q) whom I love; with you I am well pleased.”(R)

12 At once the Spirit sent him out into the wilderness, 13 and he was in the wilderness forty days,(S) being tempted[g] by Satan.(T) He was with the wild animals, and angels attended him.

Jesus Announces the Good News(U)

14 After John(V) was put in prison, Jesus went into Galilee,(W) proclaiming the good news of God.(X) 15 “The time has come,”(Y) he said. “The kingdom of God has come near. Repent and believe(Z) the good news!”(AA)

Jesus Calls His First Disciples

16 As Jesus walked beside the Sea of Galilee, he saw Simon and his brother Andrew casting a net into the lake, for they were fishermen. 17 “Come, follow me,” Jesus said, “and I will send you out to fish for people.” 18 At once they left their nets and followed him.(AB)

19 When he had gone a little farther, he saw James son of Zebedee and his brother John in a boat, preparing their nets. 20 Without delay he called them, and they left their father Zebedee in the boat with the hired men and followed him.

Jesus Drives Out an Impure Spirit(AC)

21 They went to Capernaum, and when the Sabbath came, Jesus went into the synagogue and began to teach.(AD) 22 The people were amazed at his teaching, because he taught them as one who had authority, not as the teachers of the law.(AE) 23 Just then a man in their synagogue who was possessed by an impure spirit cried out, 24 “What do you want with us,(AF) Jesus of Nazareth?(AG) Have you come to destroy us? I know who you are—the Holy One of God!”(AH)

25 “Be quiet!” said Jesus sternly. “Come out of him!”(AI) 26 The impure spirit shook the man violently and came out of him with a shriek.(AJ)

27 The people were all so amazed(AK) that they asked each other, “What is this? A new teaching—and with authority! He even gives orders to impure spirits and they obey him.” 28 News about him spread quickly over the whole region(AL) of Galilee.

Jesus Heals Many(AM)(AN)

29 As soon as they left the synagogue,(AO) they went with James and John to the home of Simon and Andrew. 30 Simon’s mother-in-law was in bed with a fever, and they immediately told Jesus about her. 31 So he went to her, took her hand and helped her up.(AP) The fever left her and she began to wait on them.

32 That evening after sunset the people brought to Jesus all the sick and demon-possessed.(AQ) 33 The whole town gathered at the door, 34 and Jesus healed many who had various diseases.(AR) He also drove out many demons, but he would not let the demons speak because they knew who he was.(AS)

Jesus Prays in a Solitary Place(AT)

35 Very early in the morning, while it was still dark, Jesus got up, left the house and went off to a solitary place, where he prayed.(AU) 36 Simon and his companions went to look for him, 37 and when they found him, they exclaimed: “Everyone is looking for you!”

38 Jesus replied, “Let us go somewhere else—to the nearby villages—so I can preach there also. That is why I have come.”(AV) 39 So he traveled throughout Galilee, preaching in their synagogues(AW) and driving out demons.(AX)

Jesus Heals a Man With Leprosy(AY)

40 A man with leprosy[h] came to him and begged him on his knees,(AZ) “If you are willing, you can make me clean.”

41 Jesus was indignant.[i] He reached out his hand and touched the man. “I am willing,” he said. “Be clean!” 42 Immediately the leprosy left him and he was cleansed.

43 Jesus sent him away at once with a strong warning: 44 “See that you don’t tell this to anyone.(BA) But go, show yourself to the priest(BB) and offer the sacrifices that Moses commanded for your cleansing,(BC) as a testimony to them.” 45 Instead he went out and began to talk freely, spreading the news. As a result, Jesus could no longer enter a town openly but stayed outside in lonely places.(BD) Yet the people still came to him from everywhere.(BE)

Footnotes

  1. Mark 1:1 Or Jesus Christ. Messiah (Hebrew) and Christ (Greek) both mean Anointed One.
  2. Mark 1:1 Some manuscripts do not have the Son of God.
  3. Mark 1:2 Mal. 3:1
  4. Mark 1:3 Isaiah 40:3
  5. Mark 1:8 Or in
  6. Mark 1:8 Or in
  7. Mark 1:13 The Greek for tempted can also mean tested.
  8. Mark 1:40 The Greek word traditionally translated leprosy was used for various diseases affecting the skin.
  9. Mark 1:41 Many manuscripts Jesus was filled with compassion