Add parallel Print Page Options

Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko.

102 Yehova imvani pemphero langa;
    kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
Musandibisire nkhope yanu
    pamene ndili pa msautso.
Munditcherere khutu;
    pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.

Pakuti masiku anga akupita ngati utsi;
    mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu;
    ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula
    ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu,
    monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala
    ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe;
    iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa
    ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu,
    popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo;
    Ine ndikufota ngati udzu.

12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya;
    kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni
    pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo;
    nthawi yoyikika yafika.
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu;
    fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova,
    mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni
    ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika;
    sadzanyoza kupempha kwawo.

18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo,
    kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba,
    kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende,
    kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni
    ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu
    adzasonkhana kuti alambire Yehova.

23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga;
    Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Choncho Ine ndinati:
    “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga;
    zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi
    ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo;
    zidzatha ngati chovala.
Mudzazisintha ngati chovala
    ndipo zidzatayidwa.
27 Koma Inu simusintha,
    ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu;
    zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

Psalm 102[a]

A prayer of an afflicted person who has grown weak and pours out a lament before the Lord.

Hear my prayer,(A) Lord;
    let my cry for help(B) come to you.
Do not hide your face(C) from me
    when I am in distress.
Turn your ear(D) to me;
    when I call, answer me quickly.

For my days vanish like smoke;(E)
    my bones(F) burn like glowing embers.
My heart is blighted and withered like grass;(G)
    I forget to eat my food.(H)
In my distress I groan aloud(I)
    and am reduced to skin and bones.
I am like a desert owl,(J)
    like an owl among the ruins.
I lie awake;(K) I have become
    like a bird alone(L) on a roof.
All day long my enemies(M) taunt me;(N)
    those who rail against me use my name as a curse.(O)
For I eat ashes(P) as my food
    and mingle my drink with tears(Q)
10 because of your great wrath,(R)
    for you have taken me up and thrown me aside.
11 My days are like the evening shadow;(S)
    I wither(T) away like grass.

12 But you, Lord, sit enthroned forever;(U)
    your renown endures(V) through all generations.(W)
13 You will arise(X) and have compassion(Y) on Zion,
    for it is time(Z) to show favor(AA) to her;
    the appointed time(AB) has come.
14 For her stones are dear to your servants;
    her very dust moves them to pity.
15 The nations will fear(AC) the name of the Lord,
    all the kings(AD) of the earth will revere your glory.
16 For the Lord will rebuild Zion(AE)
    and appear in his glory.(AF)
17 He will respond to the prayer(AG) of the destitute;
    he will not despise their plea.

18 Let this be written(AH) for a future generation,
    that a people not yet created(AI) may praise the Lord:
19 “The Lord looked down(AJ) from his sanctuary on high,
    from heaven he viewed the earth,
20 to hear the groans of the prisoners(AK)
    and release those condemned to death.”
21 So the name of the Lord will be declared(AL) in Zion
    and his praise(AM) in Jerusalem
22 when the peoples and the kingdoms
    assemble to worship(AN) the Lord.

23 In the course of my life[b] he broke my strength;
    he cut short my days.(AO)
24 So I said:
“Do not take me away, my God, in the midst of my days;
    your years go on(AP) through all generations.
25 In the beginning(AQ) you laid the foundations of the earth,
    and the heavens(AR) are the work of your hands.(AS)
26 They will perish,(AT) but you remain;
    they will all wear out like a garment.
Like clothing you will change them
    and they will be discarded.
27 But you remain the same,(AU)
    and your years will never end.(AV)
28 The children of your servants(AW) will live in your presence;
    their descendants(AX) will be established before you.”

Footnotes

  1. Psalm 102:1 In Hebrew texts 102:1-28 is numbered 102:2-29.
  2. Psalm 102:23 Or By his power