Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide.

109 Mulungu amene ndimakutamandani,
    musakhale chete,
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo
    atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane;
    iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
Andizungulira ndi mawu audani,
    amandinena popanda chifukwa.
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza,
    koma ine ndine munthu wapemphero.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino,
    ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.

Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye;
    lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa,
    ndipo mapemphero ake amutsutse.
Masiku ake akhale owerengeka;
    munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
Ana ake akhale amasiye
    ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha;
    apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Wokongoza alande zonse zimene ali nazo;
    alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima
    kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Zidzukulu zake zithe nʼkufa,
    mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova;
    tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse,
    kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.

16 Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo,
    koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka
    ndi osweka mtima.
17 Anakonda kutemberera,
    matembererowo abwerere kwa iye;
sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena,
    choncho madalitso akhale kutali naye.
18 Anavala kutemberera ngati chovala;
    kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi,
    kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho,
    ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga,
    kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.

21 Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse,
    muchite nane molingana ndi dzina lanu,
    chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 Pakuti ndine wosauka ndi wosowa,
    ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo,
    ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya,
    thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane;
    akandiona, amapukusa mitu yawo.

26 Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga;
    pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu,
    kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa;
    pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi,
    koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Onditsutsa adzavekedwa mnyozo,
    ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.

30 Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri;
    ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo,
    kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

Psalm 109

For the director of music. Of David. A psalm.

My God, whom I praise,(A)
    do not remain silent,(B)
for people who are wicked and deceitful(C)
    have opened their mouths against me;
    they have spoken against me with lying tongues.(D)
With words of hatred(E) they surround me;
    they attack me without cause.(F)
In return for my friendship they accuse me,
    but I am a man of prayer.(G)
They repay me evil for good,(H)
    and hatred for my friendship.

Appoint someone evil to oppose my enemy;
    let an accuser(I) stand at his right hand.
When he is tried, let him be found guilty,(J)
    and may his prayers condemn(K) him.
May his days be few;(L)
    may another take his place(M) of leadership.
May his children be fatherless
    and his wife a widow.(N)
10 May his children be wandering beggars;(O)
    may they be driven[a] from their ruined homes.
11 May a creditor(P) seize all he has;
    may strangers plunder(Q) the fruits of his labor.(R)
12 May no one extend kindness to him
    or take pity(S) on his fatherless children.
13 May his descendants be cut off,(T)
    their names blotted out(U) from the next generation.
14 May the iniquity of his fathers(V) be remembered before the Lord;
    may the sin of his mother never be blotted out.
15 May their sins always remain before(W) the Lord,
    that he may blot out their name(X) from the earth.

16 For he never thought of doing a kindness,
    but hounded to death the poor
    and the needy(Y) and the brokenhearted.(Z)
17 He loved to pronounce a curse—
    may it come back on him.(AA)
He found no pleasure in blessing—
    may it be far from him.
18 He wore cursing(AB) as his garment;
    it entered into his body like water,(AC)
    into his bones like oil.
19 May it be like a cloak wrapped(AD) about him,
    like a belt tied forever around him.
20 May this be the Lord’s payment(AE) to my accusers,
    to those who speak evil(AF) of me.

21 But you, Sovereign Lord,
    help me for your name’s sake;(AG)
    out of the goodness of your love,(AH) deliver me.(AI)
22 For I am poor and needy,
    and my heart is wounded within me.
23 I fade away like an evening shadow;(AJ)
    I am shaken off like a locust.
24 My knees give(AK) way from fasting;(AL)
    my body is thin and gaunt.(AM)
25 I am an object of scorn(AN) to my accusers;
    when they see me, they shake their heads.(AO)

26 Help me,(AP) Lord my God;
    save me according to your unfailing love.
27 Let them know(AQ) that it is your hand,
    that you, Lord, have done it.
28 While they curse,(AR) may you bless;
    may those who attack me be put to shame,
    but may your servant rejoice.(AS)
29 May my accusers be clothed with disgrace
    and wrapped in shame(AT) as in a cloak.

30 With my mouth I will greatly extol the Lord;
    in the great throng(AU) of worshipers I will praise him.
31 For he stands at the right hand(AV) of the needy,
    to save their lives from those who would condemn them.

Footnotes

  1. Psalm 109:10 Septuagint; Hebrew sought