Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

11 Mwa Yehova ine ndimathawiramo.
    Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti,
    “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
Pakuti taona oyipa akunga mauta awo;
    ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta,
pobisala pawo kuti alase
    olungama mtima.
Tsono ngati maziko awonongeka,
    olungama angachite chiyani?”

Yehova ali mʼNyumba yake yoyera;
    Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba.
Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu;
    maso ake amawayesa.
Yehova amayesa olungama,
    koma moyo wake umadana ndi oyipa,
    amene amakonda zachiwawa.
Iye adzakhuthulira pa oyipa
    makala amoto ndi sulufule woyaka;
    mphepo yotentha idzakhala yowayenera.

Pakuti Yehova ndi wolungama,
    Iye amakonda chilungamo;
    ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.

Psalm 11

For the director of music. Of David.

In the Lord I take refuge.(A)
    How then can you say to me:
    “Flee(B) like a bird to your mountain.(C)
For look, the wicked bend their bows;(D)
    they set their arrows(E) against the strings
to shoot from the shadows(F)
    at the upright in heart.(G)
When the foundations(H) are being destroyed,
    what can the righteous do?”

The Lord is in his holy temple;(I)
    the Lord is on his heavenly throne.(J)
He observes everyone on earth;(K)
    his eyes examine(L) them.
The Lord examines the righteous,(M)
    but the wicked, those who love violence,
    he hates with a passion.(N)
On the wicked he will rain
    fiery coals and burning sulfur;(O)
    a scorching wind(P) will be their lot.

For the Lord is righteous,(Q)
    he loves justice;(R)
    the upright(S) will see his face.(T)