Add parallel Print Page Options

115 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi
    koma ulemerero ukhale pa dzina lanu,
    chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.

Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti,
    “Mulungu wawo ali kuti?”
Mulungu wathu ali kumwamba;
    Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide,
    opangidwa ndi manja a anthu.
Pakamwa ali napo koma sayankhula,
    maso ali nawo koma sapenya;
makutu ali nawo koma samva,
    mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu;
    mapazi ali nawo koma sayenda;
    kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo,
    chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.

Inu Aisraeli, dalirani Yehova;
    Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova;
    Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova;
    Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.

12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa:
    adzadalitsa nyumba ya Israeli,
    adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova;
    aangʼono ndi aakulu omwe.

14 Yehova akuwonjezereni madalitso;
    inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova,
    Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16 Kumwamba ndi kwa Yehova,
    koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova,
    amene amatsikira kuli chete;
18 ndi ife amene timatamanda Yehova,
    kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Tamandani Yehova.

Psalm 115(A)

Not to us, Lord, not to us
    but to your name be the glory,(B)
    because of your love and faithfulness.(C)

Why do the nations say,
    “Where is their God?”(D)
Our God is in heaven;(E)
    he does whatever pleases him.(F)
But their idols are silver and gold,(G)
    made by human hands.(H)
They have mouths, but cannot speak,(I)
    eyes, but cannot see.
They have ears, but cannot hear,
    noses, but cannot smell.
They have hands, but cannot feel,
    feet, but cannot walk,
    nor can they utter a sound with their throats.
Those who make them will be like them,
    and so will all who trust in them.

All you Israelites, trust(J) in the Lord
    he is their help and shield.
10 House of Aaron,(K) trust in the Lord
    he is their help and shield.
11 You who fear him,(L) trust in the Lord
    he is their help and shield.

12 The Lord remembers(M) us and will bless us:(N)
    He will bless his people Israel,
    he will bless the house of Aaron,
13 he will bless those who fear(O) the Lord
    small and great alike.

14 May the Lord cause you to flourish,(P)
    both you and your children.
15 May you be blessed by the Lord,
    the Maker of heaven(Q) and earth.

16 The highest heavens belong to the Lord,(R)
    but the earth he has given(S) to mankind.
17 It is not the dead(T) who praise the Lord,
    those who go down to the place of silence;
18 it is we who extol the Lord,(U)
    both now and forevermore.(V)

Praise the Lord.[a](W)

Footnotes

  1. Psalm 115:18 Hebrew Hallelu Yah