Masalimo 115
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
115 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi
koma ulemerero ukhale pa dzina lanu,
chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti,
“Mulungu wawo ali kuti?”
3 Mulungu wathu ali kumwamba;
Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide,
opangidwa ndi manja a anthu.
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula,
maso ali nawo koma sapenya;
6 makutu ali nawo koma samva,
mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu;
mapazi ali nawo koma sayenda;
kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo,
chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova;
Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova;
Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova;
Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa:
adzadalitsa nyumba ya Israeli,
adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova;
aangʼono ndi aakulu omwe.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso;
inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova,
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Kumwamba ndi kwa Yehova,
koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova,
amene amatsikira kuli chete;
18 ndi ife amene timatamanda Yehova,
kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Tamandani Yehova.
Psalm 115
New International Version
Psalm 115(A)
1 Not to us, Lord, not to us
but to your name be the glory,(B)
because of your love and faithfulness.(C)
2 Why do the nations say,
“Where is their God?”(D)
3 Our God is in heaven;(E)
he does whatever pleases him.(F)
4 But their idols are silver and gold,(G)
made by human hands.(H)
5 They have mouths, but cannot speak,(I)
eyes, but cannot see.
6 They have ears, but cannot hear,
noses, but cannot smell.
7 They have hands, but cannot feel,
feet, but cannot walk,
nor can they utter a sound with their throats.
8 Those who make them will be like them,
and so will all who trust in them.
9 All you Israelites, trust(J) in the Lord—
he is their help and shield.
10 House of Aaron,(K) trust in the Lord—
he is their help and shield.
11 You who fear him,(L) trust in the Lord—
he is their help and shield.
12 The Lord remembers(M) us and will bless us:(N)
He will bless his people Israel,
he will bless the house of Aaron,
13 he will bless those who fear(O) the Lord—
small and great alike.
14 May the Lord cause you to flourish,(P)
both you and your children.
15 May you be blessed by the Lord,
the Maker of heaven(Q) and earth.
Footnotes
- Psalm 115:18 Hebrew Hallelu Yah
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.