Masalimo 116
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
116 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga;
Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Pakuti ananditchera khutu,
ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Zingwe za imfa zinandizinga,
zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera;
ndinapeza mavuto ndi chisoni.
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova:
“Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama
Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima;
pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Pumula iwe moyo wanga,
pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa,
maso anga ku misozi,
mapazi anga kuti angapunthwe,
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova
mʼdziko la anthu amoyo.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati,
“Ndasautsidwa kwambiri.”
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati,
“Anthu onse ndi abodza.”
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova,
chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso
ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova
pamaso pa anthu ake onse.
15 Imfa ya anthu oyera mtima
ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu:
ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu;
Inu mwamasula maunyolo anga.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu
ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova
pamaso pa anthu ake onse,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova,
mʼkati mwako iwe Yerusalemu.
Tamandani Yehova.
Psalm 116
New International Version
Psalm 116
1 I love the Lord,(A) for he heard my voice;
he heard my cry(B) for mercy.(C)
2 Because he turned his ear(D) to me,
I will call on him as long as I live.
3 The cords of death(E) entangled me,
the anguish of the grave came over me;
I was overcome by distress and sorrow.
4 Then I called on the name(F) of the Lord:
“Lord, save me!(G)”
5 The Lord is gracious and righteous;(H)
our God is full of compassion.(I)
6 The Lord protects the unwary;
when I was brought low,(J) he saved me.(K)
8 For you, Lord, have delivered me(N) from death,
my eyes from tears,
my feet from stumbling,
9 that I may walk before the Lord(O)
in the land of the living.(P)
10 I trusted(Q) in the Lord when I said,
“I am greatly afflicted”;(R)
11 in my alarm I said,
“Everyone is a liar.”(S)
12 What shall I return to the Lord
for all his goodness(T) to me?
13 I will lift up the cup of salvation
and call on the name(U) of the Lord.
14 I will fulfill my vows(V) to the Lord
in the presence of all his people.
15 Precious in the sight(W) of the Lord
is the death of his faithful servants.(X)
16 Truly I am your servant, Lord;(Y)
I serve you just as my mother did;(Z)
you have freed me from my chains.(AA)
17 I will sacrifice a thank offering(AB) to you
and call on the name of the Lord.
18 I will fulfill my vows(AC) to the Lord
in the presence of all his people,
19 in the courts(AD) of the house of the Lord—
in your midst, Jerusalem.(AE)
Praise the Lord.[a]
Footnotes
- Psalm 116:19 Hebrew Hallelu Yah
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.