Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide.

12 Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika;
    okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
Aliyense amanamiza mʼbale wake;
    ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.

Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo
    ndi pakamwa paliponse podzikuza.
Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu;
    pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”

“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu
    ndi kubuwula kwa anthu osowa,
Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova,
    “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro
    monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi,
    oyengedwa kasanu nʼkawiri.

Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo
    mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
Oyipa amangoyendayenda ponseponse
    anthu akamayamikira zochita zawo.

Psalm 12[a]

For the director of music. According to sheminith.[b] A psalm of David.

Help, Lord, for no one is faithful anymore;(A)
    those who are loyal have vanished from the human race.
Everyone lies(B) to their neighbor;
    they flatter with their lips
    but harbor deception in their hearts.(C)

May the Lord silence all flattering lips(D)
    and every boastful tongue—(E)
those who say,
    “By our tongues we will prevail;(F)
    our own lips will defend us—who is lord over us?”

“Because the poor are plundered(G) and the needy groan,(H)
    I will now arise,(I)” says the Lord.
    “I will protect them(J) from those who malign them.”
And the words of the Lord are flawless,(K)
    like silver purified(L) in a crucible,(M)
    like gold[c] refined seven times.

You, Lord, will keep the needy safe(N)
    and will protect us forever from the wicked,(O)
who freely strut(P) about
    when what is vile is honored by the human race.

Footnotes

  1. Psalm 12:1 In Hebrew texts 12:1-8 is numbered 12:2-9.
  2. Psalm 12:1 Title: Probably a musical term
  3. Psalm 12:6 Probable reading of the original Hebrew text; Masoretic Text earth