Add parallel Print Page Options

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

121 Ndikweza maso anga ku mapiri;
    kodi thandizo langa limachokera kuti?
Thandizo langa limachokera kwa Yehova,
    wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Sadzalola kuti phazi lako literereke;
    Iye amene amakusunga sadzawodzera.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli
    sadzawodzera kapena kugona.

Yehova ndiye amene amakusunga;
    Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana,
    kapena mwezi nthawi ya usiku.

Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse;
    adzasunga moyo wako.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako;
    kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Psalm 121

A song of ascents.

I lift up my eyes to the mountains—
    where does my help come from?
My help comes from the Lord,
    the Maker of heaven(A) and earth.(B)

He will not let your foot slip—
    he who watches over you will not slumber;
indeed, he who watches(C) over Israel
    will neither slumber nor sleep.

The Lord watches over(D) you—
    the Lord is your shade at your right hand;
the sun(E) will not harm you by day,
    nor the moon by night.

The Lord will keep you from all harm(F)
    he will watch over your life;
the Lord will watch over your coming and going
    both now and forevermore.(G)