Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

124 Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
    anene tsono Israeli,
akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
    potiwukira anthuwo,
iwo atatipsera mtima,
    akanatimeza amoyo;
chigumula chikanatimiza,
    mtsinje ukanatikokolola,
madzi a mkokomo
    akanatikokolola.

Atamandike Yehova,
    amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
    yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
    ndipo ife tapulumuka.
Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
    wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Psalm 124

A song of ascents. Of David.

If the Lord had not been on our side—
    let Israel say(A)
if the Lord had not been on our side
    when people attacked us,
they would have swallowed us alive
    when their anger flared against us;
the flood(B) would have engulfed us,
    the torrent(C) would have swept over us,
the raging waters
    would have swept us away.

Praise be to the Lord,
    who has not let us be torn by their teeth.
We have escaped like a bird
    from the fowler’s snare;(D)
the snare has been broken,(E)
    and we have escaped.
Our help is in the name(F) of the Lord,
    the Maker of heaven(G) and earth.