Add parallel Print Page Options

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

125 Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni,
    limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
Monga mapiri azungulira Yerusalemu,
    momwemonso Yehova azungulira anthu ake
    kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala
    pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama,
kuti anthu olungamawo
    angachite nawonso zoyipa.

Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino,
    amene ndi olungama mtima
Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota,
    Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa.

Mtendere ukhale pa Israeli.

Psalm 125

A song of ascents.

Those who trust in the Lord are like Mount Zion,(A)
    which cannot be shaken(B) but endures forever.
As the mountains surround Jerusalem,(C)
    so the Lord surrounds(D) his people
    both now and forevermore.

The scepter(E) of the wicked will not remain(F)
    over the land allotted to the righteous,
for then the righteous might use
    their hands to do evil.(G)

Lord, do good(H) to those who are good,
    to those who are upright in heart.(I)
But those who turn(J) to crooked ways(K)
    the Lord will banish(L) with the evildoers.

Peace be on Israel.(M)