Add parallel Print Page Options

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

132 Inu Yehova, kumbukirani Davide
    ndi mavuto onse anapirira.

Iye analumbira kwa Yehova
    ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,
“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga
    kapena kugona pa bedi langa:
sindidzalola kuti maso anga agone,
    kapena zikope zanga ziwodzere,
mpaka nditamupezera malo Yehova,
    malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”

Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata,
    tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:
“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo;
    tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.
‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira,
    Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.
Ansembe anu avekedwe chilungamo;
    anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’ ”

10 Chifukwa cha Davide mtumiki wanu,
    musakane wodzozedwa wanu.

11 Yehova analumbira kwa Davide,
    lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha:
“Mmodzi wa ana ako
    ndidzamuyika pa mpando waufumu;
12 ngati ana ako azisunga pangano langa
    ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa,
pamenepo ana awo adzakhala pa mpando
    wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”

13 Pakuti Yehova wasankha Ziyoni,
    Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:
14 “Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi;
    ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.
15 Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri;
    anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.
16 Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso,
    ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.

17 “Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide
    ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.
18 Ndidzaveka adani ake manyazi,
    koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”

Psalm 132(A)

A song of ascents.

Lord, remember David
    and all his self-denial.(B)

He swore an oath to the Lord,
    he made a vow to the Mighty One of Jacob:(C)
“I will not enter my house(D)
    or go to my bed,
I will allow no sleep to my eyes
    or slumber to my eyelids,
till I find a place(E) for the Lord,
    a dwelling for the Mighty One of Jacob.”

We heard it in Ephrathah,(F)
    we came upon it in the fields of Jaar:[a](G)
“Let us go to his dwelling place,(H)
    let us worship at his footstool,(I) saying,
‘Arise, Lord,(J) and come to your resting place,
    you and the ark of your might.
May your priests be clothed with your righteousness;(K)
    may your faithful people(L) sing for joy.’”

10 For the sake of your servant David,
    do not reject your anointed one.

11 The Lord swore an oath to David,(M)
    a sure oath he will not revoke:
“One of your own descendants(N)
    I will place on your throne.
12 If your sons keep my covenant(O)
    and the statutes I teach them,
then their sons will sit
    on your throne(P) for ever and ever.”

13 For the Lord has chosen Zion,(Q)
    he has desired it for his dwelling,(R) saying,
14 “This is my resting place for ever and ever;(S)
    here I will sit enthroned,(T) for I have desired it.
15 I will bless her with abundant provisions;
    her poor I will satisfy with food.(U)
16 I will clothe her priests(V) with salvation,
    and her faithful people will ever sing for joy.(W)

17 “Here I will make a horn[b] grow(X) for David
    and set up a lamp(Y) for my anointed one.(Z)
18 I will clothe his enemies with shame,(AA)
    but his head will be adorned with a radiant crown.”(AB)

Footnotes

  1. Psalm 132:6 Or heard of it in Ephrathah, / we found it in the fields of Jearim. (See 1 Chron. 13:5,6) (And no quotation marks around verses 7-9)
  2. Psalm 132:17 Horn here symbolizes strong one, that is, king.