Add parallel Print Page Options

136 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino.
Pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
Yamikani Mulungu wa milungu.
Pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
Yamikani Ambuye wa ambuye,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

Iye yekhayo amene amachita zodabwitsa zazikulu,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
Amene mwachidziwitso chake anapanga mayiko akumwamba,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
Amene anayala dziko lapansi pamwamba pa madzi,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
Amene anapanga miyuni ikuluikulu,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
Dzuwa lilamulire usana,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
Mwezi ndi nyenyezi zilamulire usiku,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

10 Amene anakantha ana woyamba kubadwa a Igupto,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
11 Natulutsa Israeli pakati pawo,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
12 Ndi dzanja lamphamvu ndi mkono wotambasuka,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

13 Amene anagawa Nyanja Yofiira pakati,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
14 Nadutsitsa Israeli pakati pa nyanjayo,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
15 Koma anakokolola Farao ndi ankhondo ake mʼNyanja Yofiira,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

16 Amene anatsogolera anthu ake mʼchipululu
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
17 Amene anakantha mafumu akuluakulu,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
18 Napha mafumu amphamvu,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
19 Siloni mfumu ya Aamori,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
20 Ogi mfumu ya Basani,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
21 Napereka dziko lawo ngati cholowa,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
22 Cholowa cha mtumiki wake Israeli;
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

23 Amene anatikumbukira ife anthu opeputsidwa,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
24 Amene anatimasula kwa adani athu,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.
25 Amene amapereka chakudya kwa cholengedwa chilichonse,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

26 Yamikani Mulungu wakumwamba,
pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.